< Nehemiya 1 >

1 Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
Slova Nehemiáše syna Chachaliášova. I stalo se měsíce Kislev léta dvadcátého, když jsem byl na hradě Susan,
2 Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
Že přišel Chanani, jeden z bratří mých, s některými muži z Judstva. Kterýchžto vzeptal jsem se na Židy, na ostatky pozůstalé z zajetí a na Jeruzalém.
3 Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
I řekli mi: Ostatkové ti, kteříž pozůstali z zajetí tam v té krajině, jsou u velikém nátisku a v pohanění, nadto i zed Jeruzalémská rozbořena jest, a brány jeho ohněm zkaženy.
4 Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
Kterážto slova když jsem uslyšel, sedna plakal jsem a kvílil za několik dní, a postil jsem se, i modlil před Bohem nebeským.
5 Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
A řekl jsem: Prosím, Hospodine Bože nebeský, silný, veliký a hrozný, ostříhající smlouvy a milosrdenství těm, jenž tě milují, a ostříhají přikázaní tvých,
6 Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
Budiž, prosím, ucho tvé nakloněné, a oči tvé otevřené, abys slyšel modlitbu služebníka svého, kterouž já se modlím před tebou nyní dnem i nocí za syny Izraelské, služebníky tvé, a vyznávám hříchy synů Izraelských, jimiž jsme hřešili proti tobě. Já také i dům otce mého hřešili jsme.
7 Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
Zpronevěřili jsme se tobě, a neostříhali jsme přikázaní a ustanovení a soudů, kteréž jsi vydal skrze Mojžíše služebníka svého.
8 “Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
Budiž pamětliv, prosím, na slovo, kteréž jsi přikázal Mojžíšovi služebníku svému, řka: Vy přestoupíte, já pak rozptýlím vás mezi národy.
9 Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
Ale když se obrátíte ke mně, a budete ostříhati přikázaní mých, a plniti je, by pak někteří z vás až na kraj světa zahnáni byli, i odtud shromáždím je, a přivedu je zase na místo, kteréž jsem vyvolil, aby tam přebývalo jméno mé.
10 “Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
Však tito jsou služebníci tvoji a lid tvůj, kteréž jsi vykoupil mocí svou převelikou, a rukou svou přesilnou.
11 Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.
Prosím, ó Hospodine, nechť jest nakloněné ucho tvé k modlitbě služebníka tvého, a k modlitbě služebníků tvých, kteříž žádají báti se jména tvého, a dej šťastný prospěch, prosím, služebníku svému dnes, nakloně k němu lítostí člověka toho. Já pak byl jsem šeňkéřem královským.

< Nehemiya 1 >