< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Kwathi sekuyinyanga yesikhombisa abako-Israyeli basebehlezi emadolobheni akibo. Bonke abantu babuthana ngangqondo yinye egcekeni elaliphambi kweSango laManzi. Bacela u-Ezra umbhali ukuthi alethe iNcwadi yoMthetho kaMosi, uThixo ayelaye ngawo ama-Israyeli.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
Yikho kwathi ngelanga lokuqala lenyanga yesikhombisa u-Ezra umphristi wawuletha uMthetho phambi komhlangano, owawugcwele amadoda labafazi labo bonke ababelokuzwisisa.
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
Wafunda kakhulu kusukela ekuphumeni kwelanga kwaze kwaba semini enkulu ekhangele egcekeni leSango laManzi phambi kwamadoda, labafazi labanye ababelokuzwisisa. Bonke abantu balalelisisa ukuzwa iNcwadi yoMthetho.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
U-Ezra umbhali wayemi phezu kwethala eliphakemeyo elalenziwe ngezigodo lenzelwe umkhosi lo. Eceleni kwakhe kwesokunene kwakumi uMathithiya, loShema, lo-Anaya, lo-Uriya, loHilikhiya, loMaseya; kwathi kwesokhohlo kunguPhedaya, loMishayeli, loMalikhija, loHashumi, loHashibhadana, loZakhariya loMeshulami.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
U-Ezra wayivula incwadi. Bonke abantu babembona ngoba wayemi ekuphakameni ngaphezu kwabo; kwathi lapho eyivula abantu basukuma.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
U-Ezra wamdumisa uThixo, uNkulunkulu omkhulu, kwathi bonke abantu baphendula baphakamisa izandla zabo bathi, “Ameni! Ameni!” Basebekhothama bekhonza uThixo bethe mbo ngobuso phansi.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
AbaLevi ababalisa uJeshuwa, loBhani, loSherebhiya, loJamini, lo-Akhubi, loShabhethayi, loHodiya, loMaseya, loKhelitha, lo-Azariya, loJozabhadi, loHanani loPhelaya bafundisa abantu uMthetho abantu belokhu bemi khonapho.
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
Babebala eNcwadini yoMthetho kaNkulunkulu, bewuchasisa baveze lokho okutshoyo ukuze abantu bakuzwisise lokho okwakubalwa.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Kwasekusithi uNehemiya umbusi, lo-Ezra umphristi lombhali, kanye labaLevi ababefundisa abantu bathi kubo bonke, “Lelilanga lingcwele kuThixo uNkulunkulu wenu. Lingalili kumbe likhale.” Kwakungoba bonke babekhala lapho babelalele amazwi oMthetho.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
UNehemiya wathi, “Hambani liyozitika ngokudla okumnandi lokunathwayo okumnandi, okunye likuthumele labo abangelakho okulungisiweyo. Ilanga lanamhla lingcwele kuThixo wethu. Malingadani, ngoba ukuthokoza kukaThixo kungamandla enu.”
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
AbaLevi babathulisa bonke abantu, bathi, “Thulani, ngoba lolu lusuku olungcwele. Lingadani.”
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
Kwathi abantu bonke basebehamba bayakudla banatha, bathumela okunye ukudla kwabanye bazithokozisa kakhulu, ngoba manje basebewazwisisa lawomazwi abasebewazwile.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
Ngosuku lwesibili lwenyanga, abazinhloko zezimuli zonke, kanye labaphristi labaLevi, babuthana ku-Ezra umbhali ukuba bahlolisise amazwi oMthetho.
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Bakufumana kubhaliwe eMthethweni, owalaywa nguThixo ngoMosi, ukuthi ama-Israyeli babemele bahlale ezihonqweni ngesikhathi somkhosi wenyanga yesikhombisa
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
lokuthi njalo lelilizwi babemele balimemezele liye kuwo wonke amadolobho abo laseJerusalema elithi: “Phumani liye emaqaqeni liyokhwebula amagatsha ama-oliva lama-oliva eganga, lamamithili, lamalala lezihlahla ezilomthunzi, lenze izihonqo,” njengoba kulotshiwe.
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
Ngakho abantu baphuma babuya lamagatsha bazakhela izihonqo ephahleni lwezindlu zabo, emagumeni abo, emagumeni endlu kaNkulunkulu lasegcekeni eliseSangweni laManzi lalelo elaliseSangweni lika-Efrayimi.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
Ixuku lonke elavela ebugqilini lakha izihonqo lahlala kuzo. Kusukela ensukwini zikaJoshuwa indodana kaNuni kuze kube yilolosuku, ama-Israyeli ayengazange awenze kanjalo lowo mkhosi. Kwakukukhulu ukuthokoza kwabo.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
Insuku ngensuku, kusukela kolokuqala kusiya kolokucina, u-Ezra wayebala eNcwadini yoMthetho kaNkulunkulu. Bawuthakazelela lowo mkhosi okwensuku eziyisikhombisa, kwathi ngosuku lwesificaminwembili, kwabakhona umhlangano omkhulu, njengokumisiweyo emthethweni.

< Nehemiya 8 >