< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Tout le peuple se rassembla comme un seul homme sur la grande place qui était devant la porte des eaux, et l'on dit à Esdras, le scribe, d'apporter le livre de la loi de Moïse, que Yahvé avait prescrite à Israël.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
Le prêtre Esdras apporta la loi devant l'assemblée, hommes et femmes, et devant tous ceux qui pouvaient entendre avec intelligence, le premier jour du septième mois.
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
Il en fit la lecture devant la grande place qui était devant la porte des eaux, depuis le matin jusqu'à midi, en présence des hommes et des femmes et de ceux qui étaient capables de comprendre. Les oreilles de tout le peuple étaient attentives au livre de la loi.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
Esdras, le scribe, se tenait debout sur une chaire de bois qu'on avait fabriquée à cet effet; à côté de lui se tenaient Mattithia, Shema, Anaja, Urie, Hilkija et Maaséja, à sa droite, et à sa gauche Pedaja, Mischaël, Malkija, Hashum, Hashbaddana, Zacharie et Meshullam.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
Esdras ouvrit le livre sous les yeux de tout le peuple (car il était au-dessus de tout le peuple), et quand il l'ouvrit, tout le peuple se leva.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
Puis Esdras bénit Yahvé, le grand Dieu. Tout le peuple répondit: « Amen, Amen », en levant les mains. Ils inclinèrent la tête et se prosternèrent devant Yahvé, le visage contre terre.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
Jeshua, Bani, Sherebiah, Jamin, Akkub, Shabbethai, Hodia, Maaseiah, Kelita, Azaria, Jozabad, Hanan, Pelaiah, et les Lévites, firent aussi comprendre la loi au peuple, qui resta à sa place.
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
Ils lisaient dans le livre, dans la loi de Dieu, distinctement; et ils en donnaient le sens, de sorte qu'ils comprenaient la lecture.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Néhémie, le gouverneur, Esdras, le prêtre et le scribe, et les Lévites qui enseignaient le peuple, dirent à tout le peuple: « Ce jour est consacré à Yahvé votre Dieu. Ne prenez pas le deuil et ne pleurez pas. » Car tout le peuple pleurait en entendant les paroles de la loi.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
Puis il leur dit: « Allez votre chemin. Mangez le gras, buvez le doux, et envoyez des portions à celui pour qui rien n'est préparé, car ce jour est saint pour notre Seigneur. Ne vous affligez pas, car la joie de Yahvé est votre force. »
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
Les Lévites calmèrent tout le peuple en disant: « Taisez-vous, car ce jour est saint. Ne vous affligez pas. »
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
Tout le peuple s'en alla manger, boire, envoyer des portions et célébrer, parce qu'ils avaient compris les paroles qui leur avaient été annoncées.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
Le second jour, les chefs de famille de tout le peuple, les prêtres et les Lévites s'assemblèrent auprès d'Esdras, le scribe, pour étudier les paroles de la loi.
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Ils trouvèrent écrit dans la loi que Yahvé avait ordonné par Moïse que les enfants d'Israël habitent dans des cabanes à la fête du septième mois;
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
et qu'ils devaient publier et proclamer dans toutes leurs villes et à Jérusalem, en disant: « Allez à la montagne, et prenez des branches d'olivier, des branches d'olivier sauvage, des branches de myrte, des branches de palmier et des branches d'arbres touffus, pour faire des abris temporaires, comme il est écrit. »
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
Et le peuple sortit et les apporta, et se fit des abris temporaires, chacun sur le toit de sa maison, dans leurs parvis, dans les parvis de la maison de Dieu, dans le grand espace de la porte des eaux, et dans le grand espace de la porte d'Ephraïm.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
Toute l'assemblée de ceux qui étaient revenus de la captivité fit des abris provisoires et habita dans les abris provisoires, car depuis l'époque de Josué, fils de Nun, jusqu'à ce jour, les enfants d'Israël n'avaient pas agi ainsi. Il y eut une très grande joie.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
Et chaque jour, du premier au dernier jour, il lisait dans le livre de la loi de Dieu. Ils célébrèrent la fête pendant sept jours; et le huitième jour, il y eut une assemblée solennelle, selon la coutume.

< Nehemiya 8 >