< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
and to gather all [the] people like/as man one to(wards) [the] street/plaza which to/for face: before gate [the] Water (Gate) and to say to/for Ezra [the] secretary to/for to come (in): bring [obj] scroll: book instruction Moses which to command LORD [obj] Israel
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
and to come (in): bring Ezra [the] priest [obj] [the] instruction to/for face: before [the] assembly from man and till woman and all to understand to/for to hear: hear in/on/with day one to/for month [the] seventh
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
and to call: read out in/on/with him to/for face: before [the] street/plaza which to/for face: before gate [the] Water (Gate) from [the] light till half [the] day before [the] human and [the] woman and [the] to understand and ear all [the] people to(wards) scroll: book [the] instruction
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
and to stand: stand Ezra [the] secretary upon tower tree: wood which to make to/for word: because and to stand: stand beside him Mattithiah and Shema and Anaiah and Uriah and Hilkiah and Maaseiah upon right his and from left his Pedaiah and Mishael and Malchijah and Hashum and Hashbaddanah Zechariah Meshullam
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
and to open Ezra [the] scroll: book to/for eye: seeing all [the] people for from upon all [the] people to be and like/as to open he to stand: stand all [the] people
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
and to bless Ezra [obj] LORD [the] God [the] great: large and to answer all [the] people amen amen in/on/with lifting hand their and to bow and to bow to/for LORD face land: soil [to]
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
and Jeshua and Bani and Sherebiah Jamin Akkub Shabbethai Hodiah Maaseiah Kelita Azariah Jozabad Hanan Pelaiah and [the] Levi to understand [obj] [the] people to/for instruction and [the] people upon post their
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
and to call: read out in/on/with scroll: book in/on/with instruction [the] God to declare and to set: name understanding and to understand in/on/with assembly
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
and to say Nehemiah he/she/it [the] governor and Ezra [the] priest [the] secretary and [the] Levi [the] to understand [obj] [the] people to/for all [the] people [the] day holy he/she/it to/for LORD God your not to mourn and not to weep for to weep all [the] people like/as to hear: hear they [obj] word [the] instruction
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
and to say to/for them to go: went to eat fat piece and to drink sweetness and to send: depart portion to/for nothing to establish: prepare to/for him for holy [the] day to/for lord our and not to hurt for joy LORD he/she/it security your
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
and [the] Levi be silent to/for all [the] people to/for to say to silence for [the] day holy and not to hurt
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
and to go: went all [the] people to/for to eat and to/for to drink and to/for to send: depart portion and to/for to make joy great: large for to understand in/on/with word which to know to/for them
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
and in/on/with day [the] second to gather head: leader [the] father to/for all [the] people [the] priest and [the] Levi to(wards) Ezra [the] secretary and to/for be prudent to(wards) word [the] instruction
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
and to find to write in/on/with instruction which to command LORD in/on/with hand: by Moses which to dwell son: descendant/people Israel in/on/with booth in/on/with feast in/on/with month [the] seventh
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
and which to hear: proclaim and to pass voice: message in/on/with all city their and in/on/with Jerusalem to/for to say to come out: come [the] mountain: mount and to come (in): bring leaf olive and leaf tree oil and leaf myrtle and leaf palm and leaf tree leafy to/for to make booth like/as to write
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
and to come out: come [the] people and to come (in): bring and to make to/for them booth man: anyone upon roof his and in/on/with court their and in/on/with court house: temple [the] God and in/on/with street/plaza gate [the] Water (Gate) and in/on/with street/plaza gate Ephraim (Gate)
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
and to make all [the] assembly [the] to return: return from [the] captivity booth and to dwell in/on/with booth for not to make: do from day Jeshua son: child Nun so son: descendant/people Israel till [the] day [the] he/she/it and to be joy great: large much
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
and to call: read out in/on/with scroll: book instruction [the] God day: daily in/on/with day: daily from [the] day: daily [the] first till [the] day: daily [the] last and to make: do feast seven day and in/on/with day: daily [the] eighth assembly like/as justice: judgement

< Nehemiya 8 >