< Nehemiya 8 >
1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Da den syvende Måned indtraf - Israeliterne boede nu i deres Byer - samledes hele Folket fuldtalligt på den åbne Plads foran Vandporten og bad Ezra den Skriftlærde om at hente Bogen med Mose Lov, som HERREN havde pålagt Israel.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
Så hentede Præsten Ezra Loven og fremlagde den for forsamlingen, Mænd, Kvinder og alle, der havde Forstand til at høre; det var den første Dag i den syvende Måned;
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
og vendt mod den åbne Plads foran Vandporten læste han den op fra Daggry til Middag for Mændene, Kvinderne og dem, der kunde fatte del, og alt Folket lyttede til Lovbogens Ord.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
Ezra den Skriftlærde stod på en Forhøjning af Træ, som var lavet i den Anledning, og ved Siden af ham stod til højre Mattitja, Sjema, Anaja, Urija, Hilkija og Ma'aseja, til venstre Pedaja, Misjael, Malkija, Hasjum, Hasjbaddana, Zekarja og Mesjullam.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
Og Ezra åbnede Bogen i hele Folkets Påsyn, thi han stod højere end Folket, og da han åbnede den, rejste hele Folket sig op.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
Derpå lovpriste Ezra HERREN, den store Gud, og hele Folket svarede med oprakte Hænder: Amen, Amen! Og de bøjede sig og kastede sig med Ansigtet til Jorden for HERREN.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
Og Leviterne Jesua, Bani, Sjerebja, Jamin, Akkub, Sjabbetaj, Hodija, Ma'aseja, Kelita, Azarja, Jozabad, Hanan og Pelaja udlagde Loven for Folket, medens Folket blev på sin Plads,
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
og de oplæste Stykke for Stykke af Bogen med Guds Lov og udlagde det, så man kunde fatte det.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Derpå sagde Nehemias, det er Statholderen, og Præsten Ezra den Skriftlærde og Leviterne, der underviste Folket, til alt Folket: Denne Dag er helliget HERREN eders Gud! Sørg ikke og græd ikke! Thi hele Folket græd, da de hørte Lovens Ord.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
Og han sagde til dem: Gå hen og spis fede Spiser og drik søde brikke og send noget til dem, der intet har, thi denne Dag er helliget vor Herre; vær ikke nedslåede, thi HERRENs Glæde er eders Styrke!
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
Og Leviterne tyssede på alt Folket og sagde: Vær stille, thi denne Dag er hellig, vær ikke nedslåede!
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
Da gik alt Folket hen og spiste og drak og sendte Gaver, og de fejrede en stor Glædesfest; thi de fattede Ordene, man havde kundgjort dem.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
Næste Dag samledes Overhovederne for alt Folkets Fædrenehuse og Præsterne og Leviterne hos Ezra den Skriftlærde for at mærke sig Lovens Ord,
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
og i Loven som HERREN havde påbudt ved Moses, fandt de skrevet, at Israeliterne på Højtiden i den syvende Måned skulde bo i Løvhytter,
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
og at man i alle deres Byer og i Jerusalem skulde udråbe og kundgøre følgende Budskab: Gå ud i Bjergene og hent Grene af ædle og vilde Oliventræer, Myrter, Palmer og andre Løvtræer for at bygge Løvhytter som foreskrevet!
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
Så gik Folket ud og hentede det og byggede sig Løvhytter på deres Tage og i deres Forgårde og i Guds Hus's Forgårde og på de åbne Pladser ved Vandporten og Efraimsporfen.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
Og hele Forsamlingen, der var vendt tilbage fra Fangenskabet, byggede Løvbytter og boede i dem. Thi fra Josuas, Nuns Søns, Dage og lige til den Dag havde Israeliterne ikke gjort det, og der herskede såre stor Glæde.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
Og han læste op af Bogen med Guds Lov Dag for Dag fra den første til den sidste; og de fejrede Højtiden i syv Dage, og på den ottende holdtes der festlig Samling på foreskreven Måde.