< Nehemiya 7 >

1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
Y LUEGO que el muro fué edificado, y asenté las puertas, y fueron señalados porteros y cantores y Levitas,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
Mandé á mi hermano Hanani, y á Hananías, príncipe del palacio de Jerusalem, (porque era éste, como varón de verdad y temeroso de Dios, sobre muchos; )
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
Y díjeles: No se abran las puertas de Jerusalem hasta que caliente el sol: y aun ellos presentes, cierren las puertas, y atrancad. Y señalé guardas de los moradores de Jerusalem, cada cual en su guardia, y cada uno delante de su casa.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Y la ciudad era espaciosa y grande, pero poco pueblo dentro de ella, y no había casas reedificadas.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
Y puso Dios en mi corazón que juntase los principales, y los magistrados, y el pueblo, para que fuesen empadronados por el orden de sus linajes: y hallé el libro de la genealogía de los que habían subido antes, y encontré en él escrito:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
Estos son los hijos de la provincia que subieron de la cautividad, de la transmigración que hizo pasar Nabucodonosor rey de Babilonia, y que volvieron á Jerusalem y á Judá cada uno á su ciudad;
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
Los cuales vinieron con Zorobabel, Jesuá, Nehemías, Azarías, Raamías, Nahamani, Mardochêo, Bilsán, Misperet, Bigvai, Nehum, Baana. La cuenta de los varones del pueblo de Israel:
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
Los hijos de Paros, dos mil ciento setenta y dos;
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
Los hijos de Sephatías, trescientos setenta y dos;
10 Zidzukulu za Ara 652
Los hijos de Ara, seiscientos cincuenta y dos;
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
Los hijos de Pahath-moab, de los hijos de Jesuá y de Joab, dos mil ochocientos dieciocho;
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
Los hijos de Elam, mil doscientos cincuenta y cuatro;
13 Zidzukulu za Zatu 845
Los hijos de Zattu, ochocientos cuarenta y cinco;
14 Zidzukulu za Zakai 760
Los hijos de Zachâi, setecientos y sesenta;
15 Zidzukulu za Binuyi 648
Los hijos de Binnui, seiscientos cuarenta y ocho;
16 Zidzukulu za Bebai 628
Los hijos de Bebai, seiscientos veintiocho;
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
Los hijos de Azgad, dos mil seiscientos veintidós;
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
Los hijos de Adonicam, seiscientos sesenta y siete;
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
Los hijos de Bigvai, dos mil sesenta y siete;
20 Zidzukulu za Adini 655
Los hijos de Addin, seiscientos cincuenta y cinco;
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
Los hijos de Ater, de Ezechîas, noventa y ocho;
22 Zidzukulu za Hasumu 328
Los hijos de Hasum, trescientos veintiocho;
23 Zidzukulu za Bezayi 324
Los hijos de Besai, trescientos veinticuatro;
24 Zidzukulu za Harifu 112
Los hijos de Hariph, ciento doce;
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
Los hijos de Gabaón, noventa y cinco;
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
Los varones de Beth-lehem y de Netopha, ciento ochenta y ocho;
27 Anthu a ku Anatoti 128
Los varones de Anathoth, ciento veintiocho;
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
Los varones de Beth-azmaveth, cuarenta y dos;
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
Los varones de Chîriath-jearim, Chephira y Beeroth, setecientos cuarenta y tres;
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
Los varones de Rama y de Gebaa, seiscientos veintiuno;
31 Anthu a ku Mikimasi 122
Los varones de Michmas, ciento veintidós;
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
Los varones de Beth-el y de Ai, ciento veintitrés;
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
Los varones de la otra Nebo, cincuenta y dos;
34 Ana a Elamu wina 1,254
Los hijos de la otra Elam, mil doscientos cincuenta y cuatro;
35 Zidzukulu za Harimu 320
Los hijos de Harim, trescientos y veinte;
36 Zidzukulu za Yeriko 345
Los hijos de Jericó, trescientos cuarenta y cinco;
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
Los hijos de Lod, de Hadid, y Ono, setecientos veintiuno;
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
Los hijos de Senaa, tres mil novecientos y treinta.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
Sacerdotes: los hijos de Jedaías, de la casa de Jesuá, novecientos setenta y tres;
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
Los hijos de Immer, mil cincuenta y dos;
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
Los hijos de Pashur, mil doscientos cuarenta y siete;
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
Los hijos de Harim, mil diez y siete.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
Levitas: los hijos de Jesuá, de Cadmiel, de los hijos de Odevía, setenta y cuatro.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
Cantores: los hijos de Asaph, ciento cuarenta y ocho.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
Porteros: los hijos de Sallum, los hijos de Ater, los hijos de Talmón, los hijos de Accub, los hijos de Hatita, los hijos de Sobai, ciento treinta y ocho.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
Nethineos: los hijos de Siha, los hijos de Hasupha, los hijos de Thabaoth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
Los hijos de Chêros, los hijos de Siaa, los hijos de Phadón,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
Los hijos de Lebana, los hijos de Hagaba, los hijos de Salmai,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
Los hijos de Hanán, los hijos de Giddel, los hijos de Gahar,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
Los hijos de Rehaía, los hijos de Resín, los hijos de Necoda,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
Los hijos de Gazzam, los hijos de Uzza, los hijos de Phasea,
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
Los hijos de Besai, los hijos de Meunim, los hijos de Nephisesim,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
Los hijos de Bacbuc, los hijos de Hacupha, los hijos de Harhur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
Los hijos de Baslith, los hijos de Mehida, los hijos de Harsa,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
Los hijos de Barcos, los hijos de Sísera, los hijos de Tema,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
Los hijos de Nesía, los hijos de Hatipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
Los hijos de los siervos de Salomón: los hijos de Sotai, los hijos de Sophereth, los hijos de Perida,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
Los hijos de Jahala, los hijos de Darcón, los hijos de Giddel,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
Los hijos de Sephatías, los hijos de Hattil, los hijos de Pochêreth-hassebaim, los hijos de Amón.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
Todos los Nethineos, é hijos de los siervos de Salomón, trescientos noventa y dos.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
Y estos son los que subieron de Telmelah, Tel-harsa, Chêrub, Addón, é Immer, los cuales no pudieron mostrar la casa de sus padres, ni su linaje, si eran de Israel:
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
Los hijos de Delaía, los hijos de Tobías, los hijos de Necoda, seiscientos cuarenta y dos.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
Y de los sacerdotes: los hijos de Habaías, los hijos de Cos, los hijos de Barzillai, el cual tomó mujer de las hijas de Barzillai Galaadita, y se llamó del nombre de ellas.
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
Estos buscaron su registro de genealogías, y no se halló; y fueron echados del sacerdocio.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
Y díjoles el Tirsatha que no comiesen de las cosas más santas, hasta que hubiese sacerdote con Urim y Thummim.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
La congregación toda junta era [de] cuarenta y dos mil trescientos y sesenta,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
Sin sus siervos y siervas, que eran siete mil trescientos treinta y siete; y entre ellos había doscientos cuarenta y cinco cantores y cantoras.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
Sus caballos, setecientos treinta y seis; sus mulos, doscientos cuarenta y cinco;
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
Camellos, cuatrocientos treinta y cinco; asnos, seis mil setecientos y veinte.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
Y algunos de los príncipes de las familias dieron para la obra. El Tirsatha dió para el tesoro mil dracmas de oro, cincuenta tazones, y quinientas treinta vestiduras sacerdotales.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
Y de los príncipes de las familias dieron para el tesoro de la obra, veinte mil dracmas de oro, y dos mil y doscientas libras de plata.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
Y lo que dió el resto del pueblo fué veinte mil dracmas de oro, y dos mil libras de plata, y sesenta y siete vestiduras sacerdotales.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
Y habitaron los sacerdotes y los Levitas, y los porteros, y los cantores, y los del pueblo, y los Nethineos, y todo Israel, en sus ciudades. Y venido el mes séptimo, los hijos de Israel estaban en sus ciudades.

< Nehemiya 7 >