< Nehemiya 7 >
1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
Après que la muraille fut rebâtie, que j'eus mis les portes, et que les portiers, les chantres et les Lévites furent installés,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
Je donnai mes ordres à Hanani, mon frère, et à Hanania, commandant de la forteresse de Jérusalem, car c'était un homme fidèle et craignant Dieu, plus que beaucoup d'autres;
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
Et je leur dis: Que les portes de Jérusalem ne s'ouvrent point avant la chaleur du soleil; et pendant que les gardes seront encore là, que l'on ferme les portes, et qu'on y mette les barres; que l'on place comme gardes les habitants de Jérusalem, chacun à son poste, chacun devant sa maison.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Or la ville était spacieuse et grande, mais le peuple peu nombreux, et les maisons n'étaient point bâties.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
Alors mon Dieu me mit au cœur d'assembler les principaux, les magistrats et le peuple, pour en faire le dénombrement; et je trouvai le registre du dénombrement de ceux qui étaient montés la première fois. Or j'y trouvai écrit ce qui suit:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
Voici ceux de la province qui remontèrent de la captivité, d'entre ceux que Nébucadnetsar, roi de Babylone, avait transportés, et qui retournèrent à Jérusalem et en Juda, chacun en sa ville;
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
Qui vinrent avec Zorobabel, Jéshua, Néhémie, Azaria, Raamia, Nachamani, Mardochée, Bilshan, Mispéreth, Bigvaï, Néhum et Baana. Nombre des hommes du peuple d'Israël:
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
Les enfants de Parosh, deux mille cent soixante-douze;
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
Les enfants de Shéphatia, trois cent soixante-douze;
Les enfants d'Arach, six cent cinquante-deux;
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
Les enfants de Pachath-Moab, des enfants de Jéshua et de Joab, deux mille huit cent dix-huit;
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
Les enfants d'Élam, mille deux cent cinquante-quatre;
Les enfants de Zatthu, huit cent quarante-cinq;
14 Zidzukulu za Zakai 760
Les enfants de Zaccaï, sept cent soixante;
15 Zidzukulu za Binuyi 648
Les enfants de Binnuï, six cent quarante-huit;
16 Zidzukulu za Bebai 628
Les enfants de Bébaï, six cent vingt-huit;
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
Les enfants d'Azgad, deux mille trois cent vingt-deux;
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
Les enfants d'Adonikam, six cent soixante-sept;
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
Les enfants de Bigvaï, deux mille soixante-sept;
20 Zidzukulu za Adini 655
Les enfants d'Adin, six cent cinquante-cinq;
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
Les enfants d'Ater de la famille d'Ézéchias, quatre-vingt-dix-huit;
22 Zidzukulu za Hasumu 328
Les enfants de Hashum, trois cent vingt-huit;
23 Zidzukulu za Bezayi 324
Les enfants de Betsaï, trois cent vingt-quatre;
24 Zidzukulu za Harifu 112
Les enfants de Hariph, cent douze;
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
Les enfants de Gabaon, quatre-vingt-quinze;
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
Les gens de Bethléhem et de Nétopha, cent quatre-vingt-huit;
27 Anthu a ku Anatoti 128
Les gens d'Anathoth, cent vingt-huit;
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
Les gens de Beth-Azmaveth, quarante-deux;
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
Les gens de Kirjath-Jéarim, de Képhira et de Béeroth, sept cent quarante-trois;
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
Les gens de Rama et de Guéba, six cent vingt et un;
31 Anthu a ku Mikimasi 122
Les gens de Micmas, cent vingt-deux;
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
Les gens de Béthel et d'Aï, cent vingt-trois;
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
Les gens de l'autre Nébo, cinquante-deux;
34 Ana a Elamu wina 1,254
Les enfants de l'autre Élam, mille deux cent cinquante-quatre;
35 Zidzukulu za Harimu 320
Les enfants de Harim, trois cent vingt;
36 Zidzukulu za Yeriko 345
Les enfants de Jérico, trois cent quarante-cinq;
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
Les enfants de Lod, de Hadid, et d'Ono, sept cent vingt et un;
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
Les enfants de Sénaa, trois mille neuf cent trente.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
Sacrificateurs: les enfants de Jédaja, de la maison de Jéshua, neuf cent soixante-treize;
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
Les enfants d'Immer, mille cinquante-deux;
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
Les enfants de Pashur, mille deux cent quarante-sept;
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
Les enfants de Harim, mille dix-sept.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
Lévites: les enfants de Jéshua, de Kadmiel, enfants de Hodéva, soixante et quatorze.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
Chantres: les enfants d'Asaph, cent quarante-huit.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
Portiers: les enfants de Shallum, les enfants d'Ater, les enfants de Talmon, les enfants d'Akkub, les enfants de Hatita, les enfants de Shobaï, cent trente huit.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
Néthiniens: les enfants de Tsicha, les enfants de Hasupha, les enfants de Tabbaoth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
Les enfants de Kéros, les enfants de Sia, les enfants de Padon,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
Les enfants de Lébana, les enfants de Hagaba, les enfants de Salmaï,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
Les enfants de Hanan, les enfants de Guiddel, les enfants de Gachar,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
Les enfants de Réaja, les enfants de Retsin, les enfants de Nékoda,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
Les enfants de Gazam, les enfants d'Uzza, les enfants de Paséach,
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
Les enfants de Bésaï, les enfants de Méunim, les enfants de Néphishésim,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
Les enfants de Bakbuk, les enfants de Hakupha, les enfants de Harhur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
Les enfants de Batslith, les enfants de Méhida, les enfants de Harsha,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
Les enfants de Barkos, les enfants de Sisera, les enfants de Thamach,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
Les enfants de Netsiach, les enfants de Hatipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
Enfants des serviteurs de Salomon: les enfants de Sotaï, les enfants de Sophéreth, les enfants de Périda,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
Les enfants de Jaala, les enfants de Darkon, les enfants de Guiddel,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
Les enfants de Shéphatia, les enfants de Hattil, les enfants de Pokéreth-Hatsébaïm, les enfants d'Amon.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
Total des Néthiniens, et des enfants des serviteurs de Salomon: trois cent quatre-vingt-douze.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
Voici ceux qui montèrent de Thel-Mélach, de Thel-Harsha, de Kérub-Addon, et d'Immer, lesquels ne purent montrer la maison de leurs pères, ni leur race, ni s'ils étaient d'Israël:
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
Les enfants de Délaja, les enfants de Tobija, les enfants de Nékoda, six cent quarante-deux.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
Et les sacrificateurs: les enfants de Hobaja, les enfants de Kots, les enfants de Barzillaï, qui prit pour femme une des filles de Barzillaï, le Galaadite, et qui fut appelé de leur nom.
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
Ils cherchèrent leur inscription parmi les généalogies; mais elle n'y fut point trouvée; et ils furent exclus de la sacrificature.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
Le gouverneur leur dit donc qu'ils ne mangeassent point des choses très saintes, jusqu'à ce que le sacrificateur fût là, pour consulter avec l'Urim et le Thummim.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
L'assemblée tout entière était de quarante-deux mille trois cent soixante,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
Sans leurs serviteurs et leurs servantes, qui étaient au nombre de sept mille trois cent trente-sept; ils avaient deux cent quarante-cinq chantres ou chanteuses.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
Ils avaient sept cent trente-six chevaux, deux cent quarante-cinq mulets,
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
Quatre cent trente-cinq chameaux, et six mille sept cent vingt ânes.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
Quelques-uns des chefs des pères contribuèrent pour l'ouvrage. Le gouverneur donna au trésor mille dariques d'or, cinquante bassins, cinq cent trente tuniques de sacrificateurs.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
Et d'entre les chefs des pères, plusieurs donnèrent pour le trésor de l'ouvrage, vingt mille dariques d'or, et deux mille deux cents mines d'argent.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
Et ce que le reste du peuple donna fut vingt mille dariques d'or, deux mille mines d'argent, et soixante-sept tuniques de sacrificateurs.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
Et les sacrificateurs, les Lévites, les portiers, les chantres, les gens du peuple, les Néthiniens, et tous ceux d'Israël, habitèrent dans leurs villes. Ainsi, quand arriva le septième mois, les enfants d'Israël étaient dans leurs villes.