< Nehemiya 7 >

1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
Forsothe aftir that the wal of Jerusalem was bildid, and Y hadde set yatis, and Y hadde noumbrid porters, and syngeris,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
and dekenys, Y comaundide to Aneny, my brother, and to Ananye, the prince of the hows of Jerusalem; for he semyde a sothefast man, and dredynge God more than othere men diden;
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
`and Y seide `to hem, The yatis of Jerusalem ben not openyd `til to the heete of the sunne; and, whanne Y was yit present, the yatis weren closid, and lockid. And Y settide keperis of the dwelleris of Jerusalem, alle men bi her whilis, and ech man ayens his hows.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Sotheli the citee was ful brood and greet, and litil puple was in myddis therof, and housis weren not bildid.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
Forsothe God yaf in myn herte, and Y gaderide togidere the principal men, and magistratis, and the comyn puple, for to noumbre hem; and Y foond the book of the noumbre of hem, that hadden stied first. And it was foundun writun ther ynne,
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
These ben the sones of the prouynce, `that stieden fro the caitifte of men passynge ouer, whiche Nabugodonosor, the kyng of Babiloyne, hadde `translatid, ether led ouer;
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
and thei that weren comun with Zorobabel turneden ayen in to Jerusalem and in to Judee, ech man in to his citee; Josue, Neemye, Azarie, Raanye, Naanum, Mardochee, Bethsar, Mespharath, Beggaay, Naum, Baana. The noumbre of men of the puple of Israel;
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
the sones of Pharos, two thousynde an hundrid and two and seuenti; the sones of Saphaie,
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
thre hundrid and two and seuenti;
10 Zidzukulu za Ara 652
the sones of Area, sixe hundrid and two and fifti; the sones of Phaeth Moab,
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
of the sones of Josue and of Joab, two thousynde eiyte hundrid and eiytene;
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
the sones of Helam, a thousynde eiyte hundrid and foure and fifti;
13 Zidzukulu za Zatu 845
the sones of Ezecua, eiyte hundrid and fyue and fourti;
14 Zidzukulu za Zakai 760
the sones of Zachai, seuene hundrid and sixti;
15 Zidzukulu za Binuyi 648
the sones of Bennuy, sixe hundrid and eiyte and fourti;
16 Zidzukulu za Bebai 628
the sones of Hebahi, sixe hundrid and eiyte and twenti;
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
the sones of Degad, two thousynde thre hundrid and two and twenti;
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
the sones of Azonicam, sixe hundrid and seuene and sixti;
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
the sones of Bagoamy, two thousynde and seuene and sixti;
20 Zidzukulu za Adini 655
the sones of Adyn, sixe hundrid and fiue and fifti;
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
the sones of Azer, sone of Ezechie, eiyte and twenti;
22 Zidzukulu za Hasumu 328
the sones of Asem, thre hundrid and eiyte and twenti; the sones of Bethsai,
23 Zidzukulu za Bezayi 324
thre hundrid and foure and twenti;
24 Zidzukulu za Harifu 112
the sones of Areph, an hundrid and seuene and twenti;
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
the sones of Zabaon, fyue and twenti;
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
the men of Bethleem and of Necupha, an hundrid foure score and eiyte;
27 Anthu a ku Anatoti 128
the men of Anatoth, an hundrid and eiyte and twenti;
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
the men of Bethamoth, two and fourti;
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
the men of Cariathiarym, of Cephura, and Beroth, seuene hundrid and thre and fourti;
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
the men of Rama and of Gabaa, sixe hundrid and oon and twenti; the men of Machimas,
31 Anthu a ku Mikimasi 122
two hundrid and two and twenti;
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
the men of Bethel and of Hay, an hundrid and thre and twenti; the men of the tother Nebo,
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
two and fifti;
34 Ana a Elamu wina 1,254
the men of the tother Helam, a thousynde two hundrid and foure and fifti;
35 Zidzukulu za Harimu 320
the sones of Arem, thre hundrid and twenti;
36 Zidzukulu za Yeriko 345
the sones of Jerico, thre hundrid and fyue and fourti;
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
the sones of Joiadid and Anon, seuene hundrid and oon and twenti;
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
the sones of Senaa, thre thousynde nyne hundrid and thritti; preestis,
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
the sones of Idaie, in the hous of Josua, nyne hundrid and foure and seuenti; the sones of Emmer,
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
a thousynde and two and fifti;
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
the sones of Phassur, a thousynd two hundrid and `seuene and fourti;
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
the sones of Arem, a thousynde and eiytene;
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
dekenes, the sones of Josue and of Gadymel,
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
sones of Odyna, foure and seuenti;
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
syngeris, the sones of Asaph, an hundrid and seuene and fourti;
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
porteris, the sones of Sellum, sones of Ater, sones of Thelmon, sones of Accub, sones of Accita, sones of Sobai, an hundrid and eiyte and thretti;
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
Nathynneis, sones of Soa, sones of Aspha, sones of Thebaoth, sones of Cheros,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
sones of Sicca, sones of Phado, sones of Lebana, sones of Agaba, sones of Selmon,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
sones of Anan, sones of Geddel,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
sones of Gaer, sones of Raaie, sones of Rasym,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
sones of Necuda, sones of Jezem, sones of Asa, sones of Phascha, sones of Besai,
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
sones of Mynum, sones of Nephusym,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
sones of Bechue, sones of Acupha, sones of Assur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
sones of Belloth, sones of Meida,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
sones of Arsa, sones of Berchos, sones of Sisara,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
sones of Thema, sones of Nesia,
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
sones of Atipha, sones of the seruauntis of Salomon, sones of Sothai, sones of Sophoreth,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
sones of Pherida, sones of Jacala, sones of Dalcon, sones of Geddel, sones of Saphatie,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
sones of Atthal, the sones of Phetereth, `that was borun of Abaim, sone of Amon;
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
alle Natynneis, and the sones of the seruauntis of Salomon, weren thre hundrid and two and twenti.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
Forsothe these it ben that stieden, Dethemel, Mela, Thelarsa, Cherub, Addo, and Emmer, and myyten not schewe the hows of her fadris, and her seed, whether thei weren of Israel; the sones of Dalaie,
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
the sones of Tobie, the sones of Nethoda, sixe hundrid and two and fourti;
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
and of prestis, the sones of Abia, the sones of Achos, the sones of Berzellai, that took a wijf of the douytris of Berzellai of Galaad, and was clepid bi the name of hem;
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
these souyten the scripture of her genelogie, and founden not, and weren cast out of presthod.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
And Athersata seide to hem, that thei schulden not eete of the hooli thingis of hooli men, til a wijs prest `and lerud roos.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
Al the multitude as o man, two and fourti thousynde sixe hundrid and sixti,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
outakun the seruauntis and handmaidis of hem, that weren seuene thousynde thre hundrid and seuene and thretti; and among the syngeris and syngeressis, sixe hundrid and fyue and fourti.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
The horsis of hem, sixe hundrid and sixe and thritti; the mulis of hem, two hundrid and fyue and fourti;
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
the camels of hem, foure hundrid and fyue and thritti; the assis of hem, sixe thousynde eiyte hundrid and thritti.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
Forsothe summe of the princes of meynees yauen costis in to the werk of God; Athersata yaf in to the tresour, a thousynde dragmes of gold, fifti viols, fyue hundrid and thritti cootis of prestis.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
And of the prynces of meynees thei yauen in to the tresour of the werk, twenti thousynde dragmes of gold, and two thousynde and two hundrid besauntis of siluer.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
And that that the residue puple yaf, twenti thousynde dragmes of gold, and two thousynde besauntis of siluer, and seuene and sixti cootis of prestis.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
Sotheli prestis, and dekenes, and porteris, and syngeris, and the residue puple, and Natynneis, and al Israel dwelliden in her citees.

< Nehemiya 7 >