< Nehemiya 7 >

1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
And it came to pass, when the wall was built, that I set up the doors; and then were appointed the gatekeepers and the singers and the [other] Levites [to their office].
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
And I gave my brother Chanani, and Chananyah the commander of the fortress, charge over Jerusalem; for he was esteemed a faithful man, and one that feared God these many days.
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
And I said unto them, The gates of Jerusalem must not be opened until the sun be hot; and while ye stand by, let them shut the doors, and do ye bar them; and station watches of the inhabitants of Jerusalem, every one in his watch, and every one opposite to his house.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
But the city was roomy in space and large: while the people therein were few, and the houses were not yet built.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
Then did my God put it into my heart, and I assembled together the nobles, and the rulers, and the people, that they might give in their genealogy; and I found a register of the genealogy of those who were come up at the first, and I found written therein:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
These arc the children of the province, that came up out of the captivity of the exiles, whom Nebuchadnezzar the king of Babylon had carried into exile, and who returned to Jerusalem and to Judah, every one unto his own city;
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
Who came with Zerubbabel, Jeshua', Nehemiah, 'Azaryah, Ra'amyah, Nachamani, Mordecai, Bilshan, Misspereth, Bigvai, Nechum, Ba'anah. The number of the men of the people of Israel was:
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
The children of Par'osh, two thousand one hundred and seventy and two.
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
The children of Shephatyah, three hundred seventy and two.
10 Zidzukulu za Ara 652
The children of Arach, six hundred fifty and two.
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
The children of Pachath-moab, of the children of Jeshua' and Joab, two thousand and eight hundred and eighteen.
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
The children of 'Elam, one thousand two hundred fifty and four.
13 Zidzukulu za Zatu 845
The children of Zatthu, eight hundred forty and five.
14 Zidzukulu za Zakai 760
The children of Zaccai, seven hundred and sixty.
15 Zidzukulu za Binuyi 648
The children of Binnui, six hundred forty and eight.
16 Zidzukulu za Bebai 628
The children of Bebai, six hundred twenty and eight.
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
The children of 'Azgad, two thousand three hundred twenty and two.
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
The children of Adonikam, six hundred sixty and seven.
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
The children of Bigvai, two thousand sixty and seven.
20 Zidzukulu za Adini 655
The children of 'Adin, six hundred fifty and five.
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
The children of Ater of Hezekiah, ninety and eight.
22 Zidzukulu za Hasumu 328
The children of Chashum, three hundred twenty and eight.
23 Zidzukulu za Bezayi 324
The children of Bezai, three hundred twenty and four.
24 Zidzukulu za Harifu 112
The children of Chariph, one hundred and twelve.
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
The children of Gib'on, ninety and five.
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
The men of Beth-lechem and Netophah, one hundred eighty and eight.
27 Anthu a ku Anatoti 128
The men of 'Anathoth, one hundred twenty and eight.
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
The men of Beth-'azmaveth, forty and two.
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
The men of Kiryath-ye'arim, Kephirah, and Beeroth, seven hundred forty and three.
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
The men of Ramah and Gaba', six hundred twenty and one,
31 Anthu a ku Mikimasi 122
The men of Michmass, one hundred twenty and two.
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
The men of Beth-el and 'Ai, one hundred twenty and three.
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
The men of the other Nebo, fifty and two.
34 Ana a Elamu wina 1,254
The children of the other 'Elam, one thousand two hundred fifty and four.
35 Zidzukulu za Harimu 320
The children of Charim, three hundred and twenty.
36 Zidzukulu za Yeriko 345
The people of Jericho, three hundred forty and five.
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
The people of Lod, Chadid, and Ono, seven hundred and twenty and one.
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
The people of Senaah, three thousand nine hundred and thirty.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
The priests: the children of Jeda'yah, of the house of Jeshua', nine hundred seventy and three.
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
The children of Immer, one thousand fifty and two.
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
The children of Pashchur, one thousand two hundred forty and seven.
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
The children of Charim, one thousand and seventeen.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
The Levites: The children of Jeshua', of Kadmiel, of the children of Hodevah, seventy and four.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
The singers: The children of Assaph, one hundred forty and eight.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
The gatekeepers: The children of Shallum, the children of Ater, the children of Talmon, the children of 'Akkub, the children of Chatita, the children of Shobai, one hundred thirty and eight.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
The temple-servants: The children of Zicha, the children of Chassupha, the children of Tabba'oth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
The children of Keross, the children of Si'a, the children of Padon,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
The children of Lebana, the children of Chagaba, the children of Salmai,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
The children of Chanan, the children of Giddel, the children of Gachar,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
The children of Reayah, the children of Rezin, the children of Nekoda.
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
The children of Gazzam, the children of 'Uzza, the children of Passeach.
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
The children of Bessai, the children of Me'unim, the children of Nephishessim,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
The children of Bakbuk, the children of Chakupha, the children of Charchur.
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
The children of Bazlith, the children of Mechida, the children of Charsha,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
The children of Barkoss, the children of Sissera, the children of Thamach,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
The children of Neziach, the children of Chatipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
The children of Solomon's servants: The children of Sotai, the children of Sophereth, the children of Perida,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
The children of Ya'ala, the children of Darkon, the children of Giddel,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
The children of Shephatyah, the children of Chattil, the children of Pochereth-hazzebayim, the children of Amon.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
All the temple-servants, and the children of Solomon' servants, were three hundred ninety and two.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
And these were they who came up from Thel-melach, Thelcharsha, Kerub, Addon, and Immer, but they could not tell their family division and their descent, whether they were of Israel.
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
The children of Delayah, the children of Tobiyah, the children of Nekoda, six hundred forty and two.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
And of the priests: The children of Chobayah, the children of Hakkoz, the children of Barzillai who had taken a wife from the daughters of Barzillai the Gil'adite, and was called after their name.
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
These sought for their family register, but it was not found: wherefore they were excluded, as unfit, from the priesthood.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
And the Thirshatha said unto them, that they should not eat of the most holy things, till there should stand up a priest with the Urim and Thummim.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
The whole congregation together was forty and two thousand three hundred and sixty:
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
Besides these were their man-servants and their maid-servants, of whom there were seven thousand three hundred thirty and seven: and they had two hundred and forty and five singing men and singing women.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
Their horses were seven hundred thirty and six; their mules, two hundred forty and five;
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
[Their] camels, four hundred thirty and five: [their] asses, six thousand seven hundred and twenty.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
And a portion of the chiefs of the divisions gave unto the work. The Thirshatha gave to the treasure, of gold one thousand drachms, fifty bowls, five hundred and thirty coats for the priests.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
And some of the chiefs of the divisions gave to the treasury of the work, of gold twenty thousand drachms, and of silver two thousand and two hundred manehs.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
And what the rest of the people gave was, of gold twenty thousand drachms, and of silver two thousand manehs, and priests coats sixty and seven.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
So the priests, and the Levites, and the gatekeepers, and the singers, and some of the people, and the temple-servants, and all Israel, dwelt in their cities: and so came round the seventh month, while the children of Israel were in their cities.

< Nehemiya 7 >