< Nehemiya 7 >
1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
And it came to pass, when the wall was built, and I had set up the doors, and the porters and the singers and the Levites were appointed,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
that I gave charge to Ananias my brother, and Ananias the ruler of the palace, over Jerusalem: for he was a true man, and one that feared God beyond many.
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
And I said to them, The gates of Jerusalem shall not be opened till sunrise; and while they are still watching, let the doors be shut, and bolted; and set watches of them that dwell in Jerusalem, [every] man at his post, and [every] man over against his house.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Now the city [was] wide and large; and the people [were] few in it, and the houses were not built.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
And God put [it] into my heart, and I gathered the nobles, and the rulers, and the people, into companies: and I found a register of the company that came up first, and I found written in it as follows:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
Now these [are] the children of the country, that came up from captivity, of the number which Nabuchodonosor king of Babylon carried away, and they returned to Jerusalem and to Juda, [every] man to his city;
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
with Zorobabel, and Jesus, and Neemia, Azaria, and Reelma, Naemani, Mardochaeus, Balsan, Maspharath, Esdra, Boguia, Inaum, Baana, Masphar, men of the people of Israel.
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
The children of Phoros, two thousand one hundred and seventy-two.
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
The children of Saphatia, three hundred and seventy-two.
The children of Era, six hundred and fifty-two.
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
The children of Phaath Moab, with the children of Jesus and Joab, two thousand six hundred and eighteen.
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
The children of Aelam, a thousand two hundred and fifty-four.
The children of Zathuia, eight hundred and forty-five.
14 Zidzukulu za Zakai 760
The children of Zacchu, seven hundred and sixty.
15 Zidzukulu za Binuyi 648
The children of Banui, six hundred and forty-eight.
16 Zidzukulu za Bebai 628
The children of Bebi, six hundred and twenty-eight.
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
The children of Asgad, two thousand three hundred and twenty-two.
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
The children of Adonicam, six hundred and sixty-seven.
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
The children of Bagoi, two thousand and sixty-seven.
20 Zidzukulu za Adini 655
The children of Edin, six hundred and fifty-five.
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
The children of Ater, [the son] of Ezekias, ninety-eight.
22 Zidzukulu za Hasumu 328
The children of Esam, three hundred and twenty-eight.
23 Zidzukulu za Bezayi 324
The children of Besei, three hundred and twenty-four.
24 Zidzukulu za Harifu 112
The children of Ariph, a hundred and twelve: the children of Asen, two hundred and twenty-three.
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
The children of Gabaon, ninety-five.
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
The children of Baethalem, a hundred and twenty-three: the children of Atopha, fifty-six.
27 Anthu a ku Anatoti 128
The children of Anathoth, a hundred and twenty-eight.
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
The men of Bethasmoth, forty-two.
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
The men of Cariatharim, Caphira, and Beroth, seven hundred and forty-three.
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
The men of Arama and Gabaa, six hundred and twenty.
31 Anthu a ku Mikimasi 122
The men of Machemas, a hundred and twenty-two.
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
The men of Baethel and Ai, a hundred and twenty-three.
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
The men of Nabia, a hundred an fifty-two.
34 Ana a Elamu wina 1,254
The men of Elamaar, one thousand two hundred and fifty-two.
35 Zidzukulu za Harimu 320
The children of Eram, three hundred and twenty.
36 Zidzukulu za Yeriko 345
The children of Jericho, three hundred and forty-five.
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
The children of Lodadid and Ono, seven hundred and twenty-one.
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
The children of Sanana, three thousand nine hundred and thirty.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
The priests; the sons of Jodae, [pertaining] to the house of Jesus, nine hundred and seventy-three.
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
The children of Emmer, one thousand and fifty-two.
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
The children of Phaseur, one thousand two hundred and forty-seven.
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
The children of Eram, a thousand and seventeen.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
The Levites; the children of Jesus the son of Cadmiel, with the children of Uduia, seventy-four.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
The singers; the children of Asaph, a hundred and forty-eight.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
The porters; the children of Salum, the children of Ater, the children of Telmon, the children of Acub, the children of Atita, the children of Sabi, a hundred and thirty-eight.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
The Nathinim; the children of Sea, the children of Aspha, the children of Tabaoth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
the children of Kiras, the children of Asuia, the children of Phadon,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
the children of Labana, the children of Agaba, the children of Selmei,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
the children of Anan, the children of Gadel, the children of Gaar,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
the children of Raaia, the children of Rasson, the children of Necoda,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
the children of Gezam, the children of Ozi, the children of Phese,
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
the children of Besi, the children of Meinon, the children of Nephosasi,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
the children of Bacbuc, the children of Achipha, the children of Arur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
the children of Basaloth, the children of Mida, the children of Adasan,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
the children of Barcue, the children of Sisarath, the children of Thema,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
the children of Nisia, the children of Atipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
The children of the servants of Solomon; the children of Sutei, the children of Sapharat, the children of Pherida,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
the children of Jelel, the children of Dorcon, the children of Gadael,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
the children of Saphatia, the children of Ettel, the children of Phacarath, the children of Sabaim, the children of Emim.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
All the Nathinim, and children of the servants of Solomon, [were] three hundred and ninety-two.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
And these went up from Thelmeleth, Thelaresa, Charub, Eron, Jemer: but they could not declare the houses of their families, or their seed, whether they were of Israel.
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
The children of Dalaia, the children of Tobia, the children of Necoda, six hundred and forty-two.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
And of the priests; the children of Ebia, the children of Acos, the children of Berzelli, for they took wives of the daughters of Berzelli the Galaadite, and they were called by their name.
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
These sought the pedigree of their company, and it was not found, and they were removed [as polluted] from the priesthood.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
And the Athersastha said, that they should not eat of the most holy things, until a priest should stand up to give light.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
And all the congregation was about forty-two thousand three hundred and sixty,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
besides their menservants and their maidservants: these were seven thousand three hundred and thirty seven: and the singing-men and singing-women, two hundred and forty-five.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
Two thousand seven hundred asses.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
And part of the heads of families gave into the treasury to Neemias for the work a thousand pieces of gold, fifty bowls, and thirty priests' [garments].
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
And [some] of the heads of families gave into the treasuries of the work, twenty thousand pieces of gold, and two thousand three hundred pounds of silver.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
And the rest of the people gave twenty thousand pieces of gold, and two thousand two hundred pounds of silver, and sixty-seven priests' [garments].
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
And the priests, and Levites, and porters, and singers, and [some] of the people, and the Nathinim, and all Israel, lived in their cities.