< Nehemiya 6 >
1 Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
Ita, idi nadamag da Sanballat, Tobias ken Gesem a taga-Arabia ken dagiti dadduma a kabusormi a naibangonkon ti pader ken awanen dagiti paset a nabati nga adda giwangna, nupay saankopay a naikabil dagiti ridaw kadagiti ruangan,
2 Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
nangipatulod kaniak iti mensahe da Sanballat ken Gesem a kunada, “Umayka, agsasaraktayo iti kapatadan ti Ono.” Ngem ginandatdak a dangran.
3 Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
Nangibaonak kadagiti mensahero a mapan kadakuada, a kunada, “Adu ti ar-aramidek ket saanak sumalog. Apay koma a maisardeng ti trabaho inton ibatik daytoy ket sumalogak a mapan kadakayo?”
4 Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
Namin-uppat a nangipatulodda kaniak iti isu met laeng a mensahe, ket isu met laeng ti insungbatakko kadakuada tunggal mangipatulodda iti mensahe.
5 Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
Imbaon ni Sanballat ti adipenna kaniak iti isu met laeng a wagas iti maikalima a daras, nga adda nakalukat a surat iti imana.
6 Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
Naisurat iti daytoy, “Naipadamag daytoy kadagiti nasion, ket imbaga pay ni Gesem daytoy, a sika ken dagiti Judio ket agpangpanggep nga agrebelde, dayta ti gapuna a bangbangonenyo manen ti pader. Iti ibagbaga dagitoy a damag, ngannganikan nga agbalin nga arida.
7 Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
Ket nangdutokka pay kadagiti profeta a mangiwaragawag iti maipapan kenka idiay Jerusalem, a mangibagbaga, 'Adda ti ari idiay Juda!' Masiguradom a madamagto daytoy ti ari. Umayka ngarud ta agtutungtongta koma.”
8 Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
Ket nangipatulodak iti mensahe kenkuana a kunak, “Awan ti kasta a banbanag a napasamak a kas iti ibagbagam, pinarbom dagitoy iti pusom.”
9 Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
Gapu ta kayatda amin nga agbutengtayo, ipagpagarupda nga, “Isardengdanto nga agtrabaho, ket saanto a malpas daytoy.” Ngem ita, O Dios, pangngaasim ta papigsaem dagiti imak.
10 Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
Napanak iti balay ni Semaias, a putot ni Delaias, a putot ni Mehetabel, ta saanna a mapanawan ti balayna. Kinunana, “Agsarakta koma iti balay ti Dios, iti uneg ti templo, ket irekepta dagiti ridaw ti templo, gapu ta umaydaka patayen. Umayda iti rabii a mangpatay kenka.”
11 Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
Insungbatko, “Tumaray aya met ti lalaki a kas kaniak? Mapan aya met iti templo ti lalaki a kas kaniak tapno agbiagak laeng? Saanak a mapan.”
12 Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
Naamirisko a saan a ti Dios ti nangibaon kenkuana, ngem ketdi nangipadto isuna iti maibusor kaniak. Tinangdanan isuna da Sanballat kenTobias.
13 Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
Tinangdananda isuna a mangbutbuteng kaniak, tapno aramidek ti ibagbagana ket agbasolak, iti kasta ket mapadakesda ti naganko ken maibabaindak.
14 Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
Laglagipem O Diosko, da Tobias ken Sanballat, ken amin nga inaramidda. Laglapipem met ti mammadto a babai a ni Nodias ken dagiti dadduma a mammadto a nangbutbuteng kaniak.
15 Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
Isu a nalpas ti pader iti maikaduapulo ket lima nga aldaw iti bulan ti Elul, kalpasan iti limapulo ket dua nga aldaw.
16 Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
Idi nadamag dagiti amin a kabusortayo daytoy, dagiti amin a nasion iti agawlawtayo, nagbutengda ken naibabainda. Ta ammoda a nalpas ti trabaho babaen iti tulong ti Diostayo.
17 Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
Iti daytoy a tiempo, adu a sursurat ti impatulod dagiti natatakneng a tattao ti Juda kenni Tobias, ken nakadanon dagiti surat ni Tobias kadakuada.
18 pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
Ta adu kadagiti taga-Juda ti nagsapata kenkuana, gapu ta isuna ket manugang ni Secanias a putot ni Ara. Inasawa ti putotna a ni Jehohanan ti babai a putot ni Mesullam a putot ni Berekias.
19 Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.
Imbagada met kaniak ti maipapan kadagiti nasasayaat nga aramidna ken dagiti sasaok kenkuana. Nangipatulod ni Tobias kadagiti surat kaniak tapno butbutngennak.