< Nehemiya 6 >
1 Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
Or il arriva que lorsque Sanaballat, Tobie, Gossem l’Arabe, et tous nos autres ennemis, eurent appris que j’avais bâti le mur, et qu’il n’y restait plus de brèche (jusqu’à ce temps-là, cependant, je n’avais pas mis les battants aux portes),
2 Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
Sanaballat et Gossem envoyèrent vers moi, disant: Viens, et faisons alliance ensemble dans les petits bourgs, dans la campagne d’Ono. Mais ils songeaient à me faire du mal.
3 Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
Je leur envoyai donc des messagers, disant: Je fais un grand travail; ainsi je ne puis descendre, de peur qu’il ne soit négligé lorsque j’irai et descendrai vers vous.
4 Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
Or ils renvoyèrent vers moi, d’après cette parole, par quatre fois, et je leur répondis selon la première parole.
5 Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
Alors Sanaballat m’envoya, pour la cinquième fois, son serviteur, qui avait en sa main une lettre écrite en ces termes:
6 Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
Parmi les nations, on a appris, et Gossem a dit, que toi et les Juifs vous songez à vous révolter, que pour cela tu bâtis le mur, que tu veux t’élever jusqu’à être roi sur eux, et que pour ce motif,
7 Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
Tu as même aposté des prophètes pour t’annoncer dans Jérusalem, disant: Il y a un roi en Judée. Le roi va apprendre ces choses; c’est pourquoi viens maintenant, afin que nous tenions conseil ensemble.
8 Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
Et j’envoyai vers eux disant: Il n’a pas été fait selon ces paroles que tu dis; mais c’est dans ton cœur que tu inventes toi-même ces choses.
9 Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
Car tous ces gens nous épouvantaient, pensant que nos mains cesseraient le travail et que nous nous reposerions. Pour ce motif, je fortifiai davantage mes mains.
10 Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
J’entrai ensuite secrètement dans la maison de Sémaia, fils de Dalaïa, fils de Métabéel, et il me dit: Consultons entre nous dans la maison de Dieu, au milieu du temple, et fermons les portes de la maison, parce qu’ils doivent venir pour te tuer, et c’est dans la nuit qu’ils doivent venir pour te détruire.
11 Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
Et je répondis: Est-ce que quelqu’un semblable à moi fuit? Et quel homme comme moi entrera dans le temple et vivra? Je n’y entrerai pas.
12 Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
Et je compris que Dieu ne l’avait pas envoyé, mais qu’il m’avait parlé en feignant d’être prophète, et que Tobie et Sanaballat l’avaient gagné;
13 Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
Car il avait reçu un salaire, afin que j’agisse et, épouvanté, je péchasse, et qu’ils eussent un mal à me reprocher.
14 Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
Souvenez-vous de moi, Seigneur, en considérant ces œuvres de Tobie et de Sanaballat; mais souvenez-vous aussi de Noadie, le prophète, et de tous les autres prophètes qui m’épouvantaient.
15 Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
Or le mur fut achevé le vingt-cinquième jour du mois d’Elul, en cinquante-deux jours.
16 Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
Il arriva donc, lorsque tous nos ennemis l’eurent appris, que toutes les nations qui étaient autour de nous craignirent et furent consternées en elles-mêmes, et qu’elles reconnurent que c’était par Dieu qu’avait été fait cet ouvrage.
17 Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
Mais, de plus, en ces jours-là, beaucoup de lettres des principaux des Juifs étaient envoyées à Tobie, et Tobie leur en adressait,
18 pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
Car il y en avait beaucoup en Judée qui lui avaient prêté serment, parce qu’il était gendre de Séchénias, fils d’Aréa, et que Johanan, son fils, avait épousé la fille de Mosollam, fils de Barachias,
19 Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.
Et ils le louaient même devant moi, et lui rapportaient mes paroles; et Tobie envoyait des lettres pour m’épouvanter.