< Nehemiya 6 >
1 Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
Lorsqu'on eut appris à Sanballat, à Tobija, à Guéshem l'Arabe et au reste de nos ennemis que j'avais construit la muraille et qu'il n'y avait plus de brèche, bien que je n'eusse pas encore posé les battants des portes,
2 Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
Sanballat et Guéshem m'envoyèrent dire: « Viens, rencontrons-nous dans les villages de la plaine d'Ono. Rencontrons-nous ensemble dans les villages de la plaine d'Ono. » Mais ils avaient l'intention de me faire du mal.
3 Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
J'ai envoyé des messagers vers eux, en disant: « Je fais une grande œuvre, de sorte que je ne peux pas descendre. Pourquoi l'œuvre cesserait-elle alors que je la quitte pour descendre vers vous? »
4 Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
Ils m'envoyèrent quatre fois de la sorte, et je leur répondis de la même manière.
5 Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
Alors Sanballat m'envoya son serviteur de la même manière, la cinquième fois, avec une lettre ouverte à la main,
6 Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
dans laquelle était écrit: « On raconte parmi les nations, et Gashmu le dit, que toi et les Juifs avez l'intention de vous rebeller. C'est pour cela que vous construisez le mur. Tu serais leur roi, selon ces paroles.
7 Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
Tu as aussi désigné des prophètes pour annoncer ta venue à Jérusalem, en disant: « Il y a un roi en Juda! ». Maintenant, on le rapportera au roi selon ces paroles. Viens donc maintenant, et tenons conseil ensemble. »
8 Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
Alors je lui envoyai dire: « Ce n'est pas ce que tu dis qui se fait, mais tu l'imagines de ton propre cœur. »
9 Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
Car tous auraient voulu nous effrayer, en disant: « Leurs mains seront affaiblies par l'œuvre, et elle ne se fera pas. » Mais maintenant, fortifie mes mains.
10 Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
Je me rendis à la maison de Shemahia, fils de Delaia, fils de Méhétabel, qui était enfermé chez lui, et il dit: « Réunissons-nous dans la maison de Dieu, à l'intérieur du temple, et fermons les portes du temple, car ils viendront te tuer. Oui, dans la nuit, ils viendront pour te tuer. »
11 Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
J'ai dit: « Un homme comme moi doit-il fuir? Qui est là qui, étant tel que moi, irait dans le temple pour sauver sa vie? Je n'y entrerai pas. »
12 Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
Je discernai, et voici, Dieu ne l'avait pas envoyé, mais il prononçait cette prophétie contre moi. Tobija et Sanballat l'avaient engagé.
13 Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
Ils l'avaient engagé pour que j'aie peur, que j'agisse ainsi et que je commette un péché, et pour qu'ils aient de quoi faire un mauvais rapport, afin de m'accabler de reproches.
14 Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
« Souviens-toi, mon Dieu, de Tobija et de Sanballat selon leurs œuvres, et aussi de la prophétesse Noadia et du reste des prophètes qui auraient voulu me faire peur. »
15 Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
Et la muraille fut achevée le vingt-cinquième jour d'Eloul, en cinquante-deux jours.
16 Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
Lorsque tous nos ennemis l'apprirent, toutes les nations qui nous entouraient eurent peur et perdirent leur confiance, car elles comprirent que cette œuvre avait été faite par notre Dieu.
17 Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
En ce temps-là, les nobles de Juda envoyèrent de nombreuses lettres à Tobija, et les lettres de Tobija leur parvenaient.
18 pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
Car il y en avait beaucoup en Juda qui lui juraient fidélité, parce qu'il était gendre de Shecania, fils d'Arach, et que son fils Jehohanan avait pris pour femme la fille de Meshullam, fils de Bérékia.
19 Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.
Ils parlèrent aussi de ses bonnes actions devant moi, et lui rapportèrent mes paroles. Tobija envoya des lettres pour me faire peur.