< Nehemiya 5 >
1 Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
I wszczęło się wielkie wołanie ludu i żon ich przeciw Żydom, braciom swym.
2 Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
Albowiem niektórzy mówili: Wiele nas, co synów naszych i córki nasze zastawiamy, abyśmy nabywszy zboża, jeść i żyć mogli.
3 Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
Inni zaś mówili: Role nasze, i winnice nasze, i domy nasze zastawiać musimy, abyśmy nabyli zboża w tym głodzie.
4 Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
Inni zaś mówili: Napożyczaliśmy pieniędzy, żebyśmy dali podatek królowi, zastawiwszy role nasze i winnice nasze.
5 Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
Choć oto ciało nasze jest jako ciało braci naszych, a synowie nasi są jako synowie ich: wszakże oto my musimy dawać synów naszych i córki nasze w niewolę, i niektóre z córek naszych są już w niewolę podane, a nie mamy przemożenia w rękach naszych, abyśmy je wykupili, gdyż role nasze i winnice nasze inni trzymają.
6 Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
Przetoż rozgniewałem się bardzo, gdym usłyszał wołanie ich, i słowa takowe.
7 Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
I umyśliłem w sercu swem, abym sfukał przedniejszych i przełożonych, mówiąc do nich: Wy jesteście, którzy obciążacie każdy brata swego; i zebrałem przeciwko nim zgromadzenie wielkie;
8 ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
I rzekłem do nich: Myśmy odkupili braci naszych, Żydów, którzy byli zaprzedani poganom, podług przemożenia naszego; a jeszczeż wy sprzedawać będziecie braci waszych, a tak jakoby nam ich sprzedawać będziecie? I umilknęli, i nie znaleźli, coby odpo wiedzieć.
9 Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
Nadtom rzekł: Nie dobra to rzecz, którą wy czynicie; azaż nie w bojaźni Boga naszego chodzić macie raczej niż w hańbie poganów, nieprzyjaciół naszych?
10 Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
I jać też z braćmi moimi, i z sługami moimi, pożyczyliśmy im pieniędzy, i zboża; odpuśćmyż im proszę ten ciężar.
11 Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
Wróćcież im dziś proszę role ich, winnice ich, oliwnice ich, i domy ich, i setną część pieniędzy i zboża, wina, i oliwy, którą wy od nich wyciągacie.
12 Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
Tedy odpowiedzieli: Wrócimy, a nie będziemy się od nich tego upominać; tak uczynimy, jakoś ty powiedział. Wezwałem też i kapłanów, a poprzysiągłem ich, aby także uczynili.
13 Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
Potemem wytrząsnął zanadrza moje, i rzekłem: Niech tak wytrząśnie Bóg każdego męża z domu jego i z pracy jego, któryby nie uczynił dosyć temu słowu; a niech tak będzie wytrząśniony i wypróżniony. I rzekło wszystko zgromadzenie: Amen. I chwalili Pana, a lud uczynił jako było rzeczono.
14 Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
Owszem ode dnia, którego mi przykazał król, abym był książęciem ich w ziemi Judzkiej, od roku dwudziestego aż do roku trzydziestego i wtórego Artakserksesa króla, przez dwanaście lat, ja i bracia moi obrokuśmy książęcego nie jedli.
15 Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
Choć książęta pierwsi, którzy byli przedemną, obciążali lud, biorąc od nich chleb i wino, mimo srebra syklów czterdzieści; także i słudzy ich używali okrucieństwa nad ludem; alem ja tak nie czynił dla bojaźni Bożej.
16 Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
Owszem i około poprawy tego muru pracowałem, a przecięśmy roli nie kupili; więc i wszyscy słudzy moi byli tam zgromadzeni dla roboty.
17 Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
Nadto z Żydów i przełożonych sto i pięćdziesiąt mężów, i którzy do nas przychodzili z pogan okolicznych, jadali u stołu mego.
18 Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
Przetoż gotowano na każdy dzień wołu jednego, owiec sześć wybornych, i ptaki gotowano dla mnie, a każdego dziesiątego dnia rozmaitego wina hojnie dawano; wszakżem się obroku książęcego nie upominał; albowiem ciężka była niewola na ten lud.
19 Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.
Wspomnijże na mię, Boże mój! ku dobremu według wszystkiego, com czynił ludowi twemu.