< Nehemiya 5 >
1 Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
Der lød nu højrøstede Klager fra Folket og deres Kvinder mod deres Brødre, Jøderne.
2 Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
Nogle sagde: »Vore Sønner og Døtre maa vi give i Pant for at faa Korn til Livets Ophold!«
3 Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
Andre sagde: »Vore Marker, Vingaarde og Huse maa vi give i Pant for at faa Korn under Hungersnøden!«
4 Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
Atter andre sagde: »Vi har maattet laane paa vore Marker og Vingaarde for at kunne udrede de kongelige Skatter!
5 Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
Og vore Legemer er dog lige saa gode som vore Brødres og vore Sønner lige saa gode som deres; men vi er nødt til at give vore Sønner og Døtre hen til at blive Trælle, ja, nogle af vore Døtre er det allerede, og det stod ikke i vor Magt at hindre det, eftersom vore Marker og Vingaarde tilhører andre!«
6 Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
Da jeg hørte deres Klager og disse deres Ord, blussede Vreden heftigt op i mig;
7 Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
og efter at have tænkt over Sagen gik jeg i Rette med de store og Forstanderne og sagde til dem: I driver jo Aager over for eders Næste! Saa kaldte jeg en stor Folkeforsamling sammen imod dem
8 ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
og sagde til dem: Saa vidt vi var i Stand dertil, har vi frikøbt vore jødiske Brødre, der maatte sælge sig til Hedningerne; og I sælger eders Brødre, saa de maa sælge sig til os! Da tav de og fandt intet at svare.
9 Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
Men jeg fortsatte: Det er ikke ret af eder at handle saaledes! Skulde I ikke vandre i Frygt for vor Gud af Hensyn til Hedningerne, vore Fjenders Spot?
10 Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
Ogsaa jeg og mine Brødre og mine Folk har laant dem Penge og Korn; men lad os nu eftergive dem, hvad de skylder!
11 Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
Giv dem straks deres Marker, Vingaarde, Oliventræer og Huse tilbage og eftergiv dem Pengene, Kornet, Mosten og Olien, som I har laant dem!
12 Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
Da svarede de: Ja, vi vil give det tilbage og ikke afkræve dem noget; som du siger, vil vi gøre! Jeg lod da Præsterne kalde og lod dem sværge paa, at de vilde handle saaledes.
13 Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
Og jeg rystede min Brystfold og sagde: Enhver, der ikke holder dette Ord, vil Gud saaledes ryste ud af hans Hus og Ejendom; ja, saaledes skal han blive udrystet og tømt! Da sagde hele Forsamlingen: Amen! Og de lovpriste HERREN; og Folket handlede efter sit Løfte.
14 Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
Desuden skal det nævnes, at fra den Dag Kong Artaxerxes bød mig være deres Statholder i Judas Land, fra Kong Artaxerxes's tyvende til hans to og tredivte Regeringsaar, hele tolv Aar, spiste hverken jeg eller mine Brødre det Brød, der tilkom Statholderen,
15 Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
medens mine Forgængere, de tidligere Statholdere, lagde Tynge paa Folket og for Brød og Vin daglig afkrævede dem fyrretyve Sekel Sølv, ligesom ogsaa deres Tjenere optraadte som Folkets Herrer. Det undlod jeg at gøre af Frygt for Gud.
16 Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
Og desuden tog jeg selv fat ved Arbejdet paa denne Mur, skønt vi ingen Mark havde købt, og alle mine Folk var samlet der ved Arbejdet.
17 Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
Og Jøderne, baade Forstanderne, 150 Mand, og de, der kom til os fra de omboende Hedningefolk, spiste ved mit Bord;
18 Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
og hvad der daglig lavedes til, et Stykke Hornkvæg, seks udsøgte Faar og Fjerkræ, afholdt jeg Udgifterne til; dertil kom hver tiende Dag en Masse Vin af alle Sorter. Men alligevel krævede jeg ikke det Brød, der tilkom Statholderen, fordi Arbejdet tyngede haardt paa Folket.
19 Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.
Kom i Hu alt, hvad jeg har gjort for dette Folk, og regn mig det til gode, min Gud!