< Nehemiya 4 >

1 Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri.
Ke Sanballat el lohng lah kut mwet Jew mutawauk tari in sifil musai pot uh, el kasrkusrak ac mutawauk in sufan kut.
2 Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”
El fahk ye mutun mwet lal ac un mwet mweun lun Samaria, “Mea mwet Jew afon inge oru uh? Ya elos nunku in sifil musai siti uh? Ya elos nunku mu ke sripen mwe kisa elos oru inge, ac ku in tari ke len sefanna? Ya elos ku in orek eot in musa ke yol in eot firirla ac mokutkuti?”
3 Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”
Tobiah el tu siskal na el fahk, “Pot fuka se elos ac ku in orala? Finne fox soko, el ac ku in rakinya!”
4 Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo.
Nga pre ac fahk, “O God, lohng kas in aksruksruk lalos kacsr inge. Lela angonkas lalos in folokyang nu faclos sifacna. Lela tuh ma lalos nukewa in pisreyukla, ac in utukla elos oana luman mwet kapir nu in sie mutunfacl ma elos mwetsac nu we.
5 Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”
Nikmet nunak munas ke ma koluk elos oru, ac nikmet mulkunla ma koluk lalos, ke sripen elos akkolukye kut su musa.”
6 Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.
Ouinge kut orekma na ke pot uh. Tia paht na sun tafu fulata, ke sripen mwet uh arulana insewowo in orekma.
7 Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri.
Sanballat, Tobiah, ac mwet Arabia, mwet Ammon, ac mwet Ashdod elos lohngak lah kilkilukyakna orekma lasr ke pot Jerusalem, ac acn ma soenna kupasreni ke pot ah fahsr in fonfonla, na elos kasrkusrakak.
8 Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo.
Ouinge elos nukewa pwapa in tukeni tuku fusauk orekma uh, ac mweuni Jerusalem.
9 Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.
Tusruktu kut pre nu sin God lasr, ac filiya mwet in topangi mwet lokoalok ke len ac fong.
10 Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”
Mwet Judah elos onkakin on in asor soko inge: “Kut munasla in us ma toasr, Ac puslana kutkut in utukla. Kut ac musai pot uh fuka?”
11 Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”
Mwet lokoalok lasr nunku mu kut ac tia liyalos ku etu ma elos akoo nwe ke elos sun kut ac unikuti, in pwanang orekma lasr uh in tui.
12 Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.
Tusruktu pacl pus, mwet Jew su muta inmasrlon mwet lokoalok lasr, elos fahsr fahk nu sesr ma elos akoo in oru lain kut.
13 Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo.
Ouinge nga sang cutlass, osra, ac pisr nu sin mwet lasr, ac oakelosi in sou, tuh elos in tu sisken pot uh nu loac, ke acn nukewa ma patpat ac srakna pusisel.
14 Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”
Nga akilen lah mwet uh fosrnga, ouinge nga fahk nu selos, ac nu sin mwet kol ac mwet pwapa, “Nik kowos sangeng sin mwet lokoalok lasr. Esam lupan fulat ac ku sakirik lun LEUM GOD, ac kowos in mweun ke mwet wiowos, tulik nutuwos, mutan kiowos, ac acn suwos.”
15 Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.
Mwet lokoalok lasr elos lohng lah kut etu tari pwapa lalos, ac elos akilen tuh God El sikulya lemlem lalos. Na kut nukewa folokla in sifil musai pot uh.
16 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse
In pacl sac me, tafu mwet luk uh orekma ke musa, ac tafu topangi mwet lokoalok. Elos nukum nuknuk in mweun ac sruokya osra, mwe loeyuk, ac pisr natulos. Ac mwet kolyasr elos arulana sang ku lalos in akpulaikye mwet
17 amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo.
su musai pot uh. Finne elos su til kufwen mwe orekma, elos orekma ke la paolos ac ke lac po ngia elos sruok mwe anwuk natulos.
18 Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.
Ac mwet musa nukewa elos sripisrya cutlass natulos ke pupalos. Mwet se ma ac sulkakin pacl in mweun ke pusren mwe ukuk el tu na siskuk.
19 Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma.
Nga fahk nu sin mwet uh ac mwet pwapa ac mwet kol lalos, “Ke sripen orekma uh arulana yohk, kut ac muta loes inmasrlosr sie sin sie fin pot uh.
20 Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”
Kowos fin lohng pusren ukuk, aksaye fahsreni nu yuruk. God lasr uh ac fah mweun kacsr.”
21 Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka.
Ouinge len nukewa, mutawauk ke kusrun len uh nwe ke itu uh takak ke fong, tafu sesr orekma ke pot uh, ac tafu tu sruok osra in mweun ac topang mwet lokoalok uh.
22 Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.”
Ke pacl se inge, nga fahk nu sin mwet kol orekma uh lah elos, ac mwet kasru lalos nukewa, in mutana Jerusalem ke fong uh, tuh kut in ku in forfor taran siti uh ke fong, ac orekma ke len.
23 Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.
Nga tiana sarukla nuknuk luk uh, finne ke fong, ac mwet wiyu su kulansupweyu ac karinginyu elos oru oapana. Ac kut nukewa sruok na mwe mweun natusr inpaosr.

< Nehemiya 4 >