< Nehemiya 4 >

1 Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri.
Lorsque Sanballat apprit que nous étions en train de rebâtir le mur, il en fut contrarié et entra dans une grande colère. II tourna en dérision les Judéens,
2 Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”
et dit devant ses frères et les gens de guerre de Samarie: "Que se proposent ces misérables Judéens? Les laissera-t-on faire? Offriront-ils des sacrifices? En viendront-ils à bout aujourd’hui? Rendront-ils la vie aux pierres tirées des tas de poussière et qui ont été brûlées?"
3 Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”
Tobia l’Ammonite, à côté de lui, ajoutait: "Qu’ils bâtissent toujours: il suffira qu’un renard monte dessus pour renverser leur muraille de pierres!"
4 Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo.
Ecoute, ô notre Dieu, comme nous sommes devenus un objet de mépris; fais retomber leurs outrages sur leur tête, et livre-les au pillage sur une terre de captivité.
5 Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”
Ne voile pas leur iniquité; que leur méfait ne s’efface point devant toi, puisqu’ils se sont déchaînés contre les travailleurs!
6 Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.
Cependant, nous continuâmes à rebâtir le mur; et lorsque tout le mur fut bouché jusqu’à mi-hauteur, le peuple eut de nouveau du cœur à l’ouvrage.
7 Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri.
Lorsque Sanballat, Tobia, les Arabes, les Ammonites et les gens d’Asdod apprirent que la restauration des murs de Jérusalem allait bon train, que les brèches commençaient à se fermer, ils en furent très dépités.
8 Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo.
Ils complotèrent tous ensemble d’aller attaquer Jérusalem et d’y jeter le désarroi.
9 Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.
Nous implorâmes notre Dieu et, pour nous défendre contre eux, nous établîmes un service de faction chargé de les surveiller jour et nuit.
10 Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”
Juda disait: "Les forces des porteurs de charges sont à bout et les décombres sont considérables; nous sommes hors d’état de rebâtir la muraille."
11 Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”
Et nos adversaires disaient: "Ils ne se douteront ni ne s’apercevront de rien jusqu’à ce que nous pénétrions au milieu d’eux pour les massacrer, et ainsi nous mettrons fin à ce travail."
12 Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.
Comme des Judéens établis parmi eux vinrent nous dire jusqu’à dix fois: "De quelque localité que vous soyez, il faut que-vous retourniez chez nous",
13 Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo.
je plaçai en contrebas, derrière la muraille, sur des terrains secs, je plaçai, dis-je, le peuple par familles, avec leurs épées, leurs lances et leurs arcs.
14 Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”
Ayant tout inspecté, je m’avançai et dis aux grands, aux chefs et au reste du peuple: "N’Ayez pas peur d’eux; pensez au Seigneur grand et redoutable et combattez pour vos frères, vos fils et vos filles, vos femmes et vos maisons."
15 Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.
Quand nos ennemis eurent été informés que nous étions avertis et que Dieu avait ruiné leur plan, nous retournâmes tous à la muraille, chacun à son ouvrage.
16 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse
A partir de ce jour, la moitié de mes gens s’occupait de l’ouvrage, et l’autre moitié était munie de lances, de boucliers, d’arcs et de cuirasses; les seigneurs se tenaient derrière toute la maison de Juda.
17 amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo.
De ceux qui étaient occupés à la bâtisse, d’une part les manœuvres, porteurs de charges, faisaient leur besogne d’une main et tenaient l’épée de l’autre;
18 Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.
d’autre part, les maçons construisaient, ayant chacun son épée attachée aux reins, et celui qui sonnait de la trompette était à mes côtés.
19 Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma.
Et je dis aux nobles, aux chefs et au reste du peuple: "L’Ouvrage est considérable et s’étend sur un vaste espace, de sorte que nous sommes dispersés le long de la muraille, éloignés l’un de l’autre.
20 Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”
A l’endroit d’où vous parviendra le son de la trompette, là vous viendrez vous rallier à nous: Dieu combattra en notre faveur."
21 Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka.
C’Est ainsi que nous nous occupions de l’ouvrage, la moitié des gens tenant les lances depuis le lever de l’aurore jusqu’à l’apparition des étoiles.
22 Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.”
En ce temps-là aussi, je demandai au peuple que chacun passât la nuit à Jérusalem avec son serviteur, pour nous servir de sentinelles pendant la nuit et consacrer le jour au travail.
23 Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.
Quant à moi, à mes frères, à mes gens et aux hommes de garde qui me suivaient, nous ne quittions point nos vêtements: chacun gardait son épée dans la main droite.

< Nehemiya 4 >