< Nehemiya 3 >
1 Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
Potem je vstal Eljašíb, véliki duhovnik, s svojimi brati duhovniki in zgradili so Ovčja velika vrata. Posvetili so jih in vstavili vrata, celo do stolpa Mea so to posvetili, do Hananélovega stolpa.
2 Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
Poleg njega so gradili možje iz Jerihe. Poleg njih je gradil Imríjev sin Zahúr.
3 Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
Toda Ribja velika vrata so gradili Senaájevi sinovi, ki so tudi položili njena bruna in postavili njena vrata, njene ključavnice in njene zapahe.
4 Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
Poleg njih je popravljal Meremót, Urijájev sin, Kocov sin. Poleg njih je popravljal Mešulám, Berehjájev sin, Mešezabélov sin. In poleg njih Baanájev sin Cadók.
5 Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
Poleg njih so popravljali Tekójčani, toda njihovi plemiči svojih vratov niso pristavili k delu njihovega Gospoda.
6 Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
Poleg tega sta Stara velika vrata popravljala Jojadá, sin Paséaha in Mešulám, Besodjájev sin. Položila sta njena bruna in postavila njena vrata in njene ključavnice in njene zapahe.
7 Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
Poleg njiju so popravljali Gibeónec Melatjá in Meronočán Jadón, možje iz Gibeóna in iz Micpe, do prestola voditelja na tej strani reke.
8 Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
Poleg njega je popravljal Uziél, Harhajájev sin izmed zlatarjev. Poleg njega je popravljal tudi Hananjá, sin enega izmed lekarnarjev in Jeruzalem so utrdili do širokega zidu.
9 Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
Poleg njih je popravljal Hurov sin Refajá, vladar polovice Jeruzalema.
10 Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
Poleg njega je popravljal Harumáfov sin Jedajája, celo nasproti svoje hiše. Poleg njega je popravljal Hašabnejájev sin Hatúš.
11 Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
Harímov sin Malkijája in Pahat Moábov sin Hašúb sta popravljala drug kos in stolp talilne peči.
12 Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
Poleg njega je popravljal Lohéšev sin Šalúm, vladar polovice Jeruzalema, on in njegove hčere.
13 Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
Dolinska velika vrata so popravljali Hanún in prebivalci Zanóaha. Zgradili so jih in postavili njena vrata, njene ključavnice in njene zapahe in tisoč komolcev na obzidju do Gnojnih velikih vrat.
14 Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
Toda Gnojna velika vrata je popravljal Rehábov sin Malkijáj, vladar dela Bet Kerema. Zgradil jih je, postavil njena vrata, njene ključavnice in njene zapahe.
15 Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
Toda Studenčna velika vrata je popravljal Kolhozéjev sin Šalún, vladar dela Micpe. On je to zgradil, pokril in postavil njena vrata, njene ključavnice in njene zapahe in zid ribnika Síloa, poleg kraljevega vrta in do stopnic, ki gredo dol od Davidovega mesta.
16 Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
Za njim je popravljal Azbúkov sin Nehemija, vladar polovice Bet Cura, do kraja nasproti Davidovih mavzolejev in do ribnika, ki je bil narejen in do hiše mogočnega.
17 Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
Za njim so popravljali Lévijevci, Baníjev sin Rehúm. Poleg njega je na svojem delu popravljal Hašabjá, vladar polovice Keíle.
18 Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
Za njim so popravljali njihovi bratje, Henadádov sin Bavaj, vladar polovice Keíle.
19 Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
Poleg njega je popravljal Ješúajev sin Ecer, vladar Micpe, drug del nasproti vzpona do orožarne, ob [delu, kjer se] zid obrne.
20 Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
Za njim je Zabájev sin Baruh vneto popravljal drugi kos, od [dela, kjer se] zid obrne, do vrat hiše vélikega duhovnika Eljašíba.
21 Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
Za njim je drug del popravljal Meremót, Urijájev sin, Kocov sin, od vrat Eljašíbove hiše, celo do konca Eljašíbove hiše.
22 Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
Za njim so popravljali duhovniki, možje ravnine.
23 Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
Za njim sta nasproti njuni hiši popravljala Benjamin in Hašúb. Za njima je ob njegovi hiši popravljal Azarjá, Maasejájev sin, sin Ananjája.
24 Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
Za njim je popravljal Henadádov sin Binúj, drug del od Azarjájeve hiše do [dela, kjer se] zid obrne, celo do vogala.
25 Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
Uzájev sin Palál nasproti [dela, kjer se] zid obrne in stolpa, ki se nahaja zunaj kraljeve velike hiše, ki je bila ob dvorišču ječe. Za njim Paróšev sin Pedajá.
26 ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
Poleg tega so Netinimci prebivali v Ofelu, do kraja nasproti Vodnih velikih vrat proti vzhodu in stolpa, ki se nahaja zunaj.
27 Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
Za njimi so Tekójčani popravljali drug del, nasproti velikemu stolpu, ki leži zunaj, celo do ofelskega obzidja.
28 Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
Od zgoraj, iznad Konjskih velikih vrat so popravljali duhovniki, vsak nasproti svoji hiši.
29 Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
Za njimi je popravljal Imêrjev sin Cadók nasproti svoji hiši. Za njim je popravljal tudi Šehanjájev sin Šemajá, čuvaj Vzhodnih velikih vrat.
30 Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
Za njim je drug del popravljal Šelemjájev sin Hananjá in Hanún, šesti Caláfov sin. Za njim je popravljal Berehjájev sin Mešulám nasproti svoje sobe.
31 Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
Za njim je popravljal zlatarjev sin Malkijá do kraja Netinimcev in trgovcev, nasproti velikih vrat Mifkada in do vzpona vogala.
32 Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.
Med vzponom vogala, do Ovčjih velikih vrat, so popravljali zlatarji in trgovci.