< Nehemiya 3 >

1 Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
Ylimmäinen pappi Eljasib ja hänen veljensä, papit, nousivat ja rakensivat Lammasportin, jonka he pyhittivät ja jonka ovet he asettivat paikoilleen, edelleen Hammea-torniin asti, jonka he pyhittivät, ja edelleen Hananelin-torniin asti.
2 Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
Heistä eteenpäin rakensivat Jerikon miehet; ja näistä eteenpäin rakensi Sakkur, Imrin poika.
3 Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
Ja Kalaportin rakensivat senaalaiset; he kattoivat sen ja asettivat paikoilleen sen ovet, teljet ja salvat.
4 Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
Heistä eteenpäin korjasi muuria Meremot, Uurian poika, joka oli Koosin poika; hänestä eteenpäin korjasi Mesullam, Berekjan poika, joka oli Mesesabelin poika; ja hänestä eteenpäin korjasi Saadok, Baanan poika.
5 Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
Hänestä eteenpäin korjasivat muuria tekoalaiset; mutta heidän ylhäisensä eivät notkistaneet niskaansa Herransa palvelukseen.
6 Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
Vanhan portin korjasivat Joojada, Paaseahin poika, ja Mesullam, Besodjan poika; he kattoivat sen ja asettivat paikoilleen sen ovet, teljet ja salvat.
7 Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
Heistä eteenpäin korjasivat muuria gibeonilainen Melatja ja meeronotilainen Jaadon sekä Gibeonin ja Mispan miehet, jotka olivat Eufrat-virran tämänpuoleisen käskynhaltijan vallan alaisia.
8 Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
Heistä eteenpäin korjasi muuria Ussiel, Harhajan poika, yksi kultasepistä, ja hänestä eteenpäin korjasi Hananja, yksi voiteensekoittajista; he panivat kuntoon Jerusalemia Leveään muuriin saakka.
9 Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
Heistä eteenpäin korjasi muuria Refaja, Huurin poika, Jerusalemin piirin toisen puolen päällikkö.
10 Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
Hänestä eteenpäin korjasi Jedaja, Harumafin poika, oman talonsa kohdalta; hänestä eteenpäin korjasi Hattus, Hasabnejan poika.
11 Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
Toisen osan korjasivat Malkia, Haarimin poika, ja Hassub, Pahat-Mooabin poika, sekä sen lisäksi Uunitornin.
12 Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
Heistä eteenpäin korjasi Sallum, Looheksen poika, Jerusalemin piirin toisen puolen päällikkö, hän ja hänen tyttärensä.
13 Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
Laaksoportin korjasivat Haanun ja Saanoahin asukkaat; he rakensivat sen ja asettivat paikoilleen sen ovet, teljet ja salvat. Sen lisäksi he korjasivat tuhat kyynärää muuria, Lantaporttiin saakka.
14 Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
Lantaportin korjasi Malkia, Reekabin poika, Beet-Keremin piirin päällikkö; hän rakensi sen ja asetti paikoilleen sen ovet, teljet ja salvat.
15 Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
Lähdeportin korjasi Sallum, Kolhoosen poika, Mispan piirin päällikkö; hän rakensi sen, teki siihen katon ja asetti paikoilleen sen ovet, teljet ja salvat. Sen lisäksi hän korjasi Vesijohtolammikon muurin, kuninkaan puutarhan luota, aina niihin portaisiin saakka, jotka laskeutuvat Daavidin kaupungista.
16 Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
Hänen jälkeensä korjasi Nehemia, Asbukin poika, Beet-Suurin piirin toisen puolen päällikkö, aina Daavidin hautojen kohdalle ja Tekolammikolle ja Urhojentalolle saakka.
17 Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
Hänen jälkeensä korjasivat muuria leeviläiset: Rehum, Baanin poika; hänestä eteenpäin korjasi Hasabja, Kegilan piirin toisen puolen päällikkö, piirinsä puolesta.
18 Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
Hänen jälkeensä korjasivat heidän veljensä: Bavvai, Heenadadin poika, joka oli Kegilan piirin toisen puolen päällikkö.
19 Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
Hänestä eteenpäin korjasi Eeser, Jeesuan poika, Mispan päällikkö, toisen osan, siltä kohdalta, mistä noustaan asehuoneeseen, joka on Kulmauksessa.
20 Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
Hänen jälkeensä korjasi Baaruk, Sabbain poika, suurella innolla toisen osan, Kulmauksesta aina ylimmäisen papin Eljasibin talon oveen saakka.
21 Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
Hänen jälkeensä korjasi Meremot, Uurian poika, joka oli Koosin poika, toisen osan, Eljasibin talon ovesta Eljasibin talon päähän.
22 Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
Hänen jälkeensä korjasivat papit, Lakeuden miehet.
23 Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
Heidän jälkeensä korjasivat Benjamin ja Hassub oman talonsa kohdalta; heidän jälkeensä korjasi Asarja, Maasejan poika, joka oli Ananjan poika, talonsa viereltä.
24 Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
Hänen jälkeensä korjasi Binnui, Heenadadin poika, toisen osan, Asarjan talosta aina Kulmaukseen ja kulmaan saakka.
25 Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
Paalal, Uusain poika, korjasi Kulmauksen ja Ylätornin kohdalta, joka ulkonee kuninkaan linnasta vankilan pihaan päin; hänen jälkeensä Pedaja, Paroksen poika
26 ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
-temppelipalvelijat asuivat Oofelilla-itäisen Vesiportin ja ulkonevan tornin kohdalta.
27 Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
Hänen jälkeensä korjasivat tekoalaiset toisen osan, suuren, ulkonevan tornin kohdalta aina Oofelin muuriin saakka.
28 Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
Hevosportin yläpuolelta korjasivat papit, kukin oman talonsa kohdalta.
29 Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
Heidän jälkeensä korjasi Saadok, Immerin poika, oman talonsa kohdalta. Ja hänen jälkeensä korjasi Semaja, Sekanjan poika, Itäportin vartija.
30 Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
Hänen jälkeensä korjasivat Hananja, Selemjan poika, ja Haanun, Saalafin kuudes poika, toisen osan; hänen jälkeensä korjasi Mesullam, Berekjan poika, yliskammionsa kohdalta.
31 Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
Hänen jälkeensä korjasi Malkia, yksi kultasepistä, temppelipalvelijain ja kauppiasten taloon asti, Vartiotornin kohdalta, ja aina Kulmasaliin saakka.
32 Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.
Kultasepät ja kauppiaat korjasivat muurin Kulmasalin ja Lammasportin väliltä.

< Nehemiya 3 >