< Nehemiya 3 >

1 Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
Ja Eljasib, ylimmäinen pappi, nousi pappein veljeinsä kanssa, rakensivat Lammasportin ja pyhittivät sen, ja panivat siihen ovet; ja he pyhittivät sen Mean torniin asti, hamaan Hananeelin torniin saakka.
2 Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
Ja Jerihon miehet rakensivat hänen vieressänsä, ja Sakkur Imrin poika rakensi hänen vieressänsä.
3 Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
Mutta Senaan lapset rakensivat Kalaportin, ja kattivat sen, ja panivat siihen ovet, lukot ja teljet.
4 Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
Ja Meremot Urian poika, Hakkotsin pojan, rakensi heidän vieressänsä, ja Mesullam Berekian poika, Mesesabelin pojan, rakensi heidän vieressänsä; Zadok Baenan poika rakensi heidän vieressänsä.
5 Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
Niiden tykönä rakensivat Tekoan miehet; mutta heidän sankarinsa ei kääntäneet kaulaansa Herransa palvelukseen.
6 Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
Vanhan portin rakensi Jojada Passean poika ja Mesullam Besodian poika, ja kattivat sen, ja panivat siihen ovet, lukot ja teljet.
7 Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
Melatia Gibeonilainen ja Jadon Meronotilainen rakensi heidän vieressänsä, Gibeonin ja Mitspan miehet, päämiehen istuimen tykönä, sillä puolella virtaa.
8 Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
Hänen vieressänsä rakensi Ussiel Harhakan kultasepän poika; hänen vieressänsä rakensi Hanania yrtteinmyyjän poika; ja he rakensivat Jerusalemia leviään muuriin asti.
9 Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
Hänen vieressänsä rakensi Rephaja Hurin poika, puolen Jerusalemin päämies.
10 Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
Heidän vieressänsä rakensi Jedaja Harumaphin poika, huoneensa kohdalla; hänen vieressänsä rakensi Hattus, Hasabnejan poika.
11 Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
Mutta Malkia Harimin poika ja Hasub Pahatmoabin poika rakensivat toista kulmaa, niin myös Pätsitornin.
12 Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
Hänen vieressänsä rakensi Sallum Haloeksen poika, puolen Jerusalemin päämies: hän itse ja hänen tyttärensä.
13 Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
Laaksoportin rakensi Hanun ja Sanoan asujamet; ne rakensivat sen ja panivat siihen ovet, lukot ja teljet, ja tuhannen kyynärää muuria Sontaporttiin asti.
14 Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
Mutta Malkia Rekabin poika, viinamäen kulmakunnan päämies, rakensi Sontaportin, hän rakensi sen ja pani siihen ovet, lukot ja teljet.
15 Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
Mutta Lähdeportin rakensi Sallun Kolhosen poika, Mitspan kulmakunnan päämies; hän rakensi ja katti sen, ja pani siihen ovet, lukot ja teljet; niin myös Selan lammin muurin kuninkaan yrttitarhan tykönä, niihin astuimiin asti, jotka tulevat alas Davidin kaupungista.
16 Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
Hänen vieressänsä rakensi Nehemia Asbukin poika, puolen Betsuurin päämies, aina Davidin hautain kohdalle, ja kaivettuun lammikkoon asti väkeväin huoneeseen asti.
17 Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
Häntä likimpänä rakensivat Leviläiset, Rehum Banin poika; hänen vieressänsä rakensi Hasabia, puolen Kegilan päämies kulmakuntansa puolesta.
18 Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
Häntä likimpänä rakensivat heidän veljensä Bavai Hanadadin poika, toisen puolen Kegilan päämies.
19 Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
Hänen vieressänsä rakensi Eser Jesuan poika, Mitspan päämies, toisen osan siinä kulmassa, asehuoneen puolessa.
20 Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
Häntä likinnä rakensi Baruk Sabbain poika kiivaasti toisen osan kulmasta Eljasibin ylimmäisen papin huoneen oveen asti.
21 Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
Häntä likinnä rakensi Meremot Urian poika, Hakkotsin pojan, toisen osan, Eljasibin huoneen ovesta Eljasibin huoneen loppuun asti.
22 Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
Ja hänen jälkeensä rakensivat papit, miehet lakeudelta.
23 Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
Heidän jälkeensä rakensi Benjamin ja Hassub oman huoneensa kohdalla; heidän perässänsä rakensi Asaria Maesejan poika, Ananian pojan, huoneensa tykönä.
24 Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
Hänen jälkeensä rakensi Binnui Henadadin poika, toisen osan, Asarian huoneesta niin loukkaasen ja hamaan kulmaan asti.
25 Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
Palal Usain poika loukasta vastaan ja tornia, joka menee kuninkaan ylisestä huoneesta, joka oli vankikartanon tykönä; hänen jälkeensä Pedaja Paroksen poika.
26 ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
Mutta Netinimit asuivat Ophelin tykönä Vesiporttiin asti itään päin, josta torni käy ulos.
27 Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
Sitälikin rakensivat Tekoalaiset toisen osan, isoa tornia päin, kuin näkyy ulos, Opelin muuriin asti,
28 Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
Mutta Hevosportin yläpuolelta rakensivat papit, jokainen huoneensa kohdalla.
29 Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
Heidän jälissänsä rakensi Zadok Immerin poika, huoneensa kohdalla; hänen jälissänsä rakensi Semaja Sekanian poika, Itäportin vartia.
30 Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
Hänen jälissänsä rakensi Hananian Selemian poika, ja Hanun kuudes Salaphin poika, toisen osan; hänen jälissänsä rakensi Mesullam Berekian poika, makaushuoneensa kohdalla.
31 Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
Hänen jälissänsä rakensi Malkia kultasepän poika, Netinimein ja kauppamiesten huoneesen asti, Käräjäportin kohdalla, hamaan Kulmasaliin saakka.
32 Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.
Kultasepät ja kauppamiehet rakensivat Kulmasalin välillä ja Lammasporttiin asti.

< Nehemiya 3 >