< Nehemiya 3 >

1 Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
And Eliasiph, the greet preest, roos, and hise britheren, and prestis, and thei bildiden the yate of the floc; thei maden it stidfast; and settiden the yatis therof, and `til to the tour of an hundrid cubitis, thei maden it stidfast, `til to the tour of Ananehel.
2 Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
And bisidis hym the men of Jerico bildiden; and bisidis hem Zaccur, the sone of Amry, bildide.
3 Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
Forsothe the sones of Asamaa bildiden the yatis of fischis; thei hiliden it, and settiden the yatis therof, and lockis, and barris. And Marymuth, sone of Vrye, the sone of Accus, bildide bisidis hem.
4 Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
And Mosolla, sone of Barachie, the sone of Meseze, bildide bisidis hym. And Sadoch, the sone of Baana, bildide bisidis him.
5 Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
And men of Thecue bildiden bisidis hym; but the principal men of hem puttiden not her neckis vndur in the werk of her Lord God.
6 Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
And Joiada, the sone of Phasea, and Mosollam, the sone of Besoyda, bildiden the elde yate; thei hiliden it, and settiden the yatis therof, and lockis, and barris.
7 Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
And Melchie Gabaonyte, and Jaddon Methonatite, men of Gabaon and of Maspha, bildiden bisidis hem, for the duyk that was in the cuntrei biyende the flood.
8 Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
And Eziel, goldsmyyt, the sone of Araie, bildide bisidis hym; and Annany, the sone of `a makere of oynement, bildide bisidis him; and thei leften Jerusalem `til to the wal of the largere street.
9 Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
And Raphaie, the sone of Hahul, prince of a street of Jerusalem, bildide bisidis him.
10 Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
And Jeieda, the sone of Aramath, bildide bisidis him ayens his owne hous; and Accus, the sone of Asebonye, bildide bisidis hym.
11 Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
Forsothe Melchie, the sone of Herem, and Asub, the sone of Phet Moab, bildiden the half part of the street, and the tour of ouenys.
12 Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
Sellum, the sone of Aloes, prince of the half part of a street of Jerusalem, bildide bisidis hym, he and hise sones.
13 Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
And Amram, and the dwelleris of Zanoe, bildiden the yate of the valei; thei bildiden it, and settiden the yatis therof, and lockis, and barris therof; and thei bildiden a thousynde cubitis in the wal `til to the yate of the dunghil.
14 Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
And Melchie, the sone of Rechab, prynce of a street of Bethacarem, bildide the yate of the dunghil; he bildide it, and settide, and hilide the yatis therof, and lockis, and barris.
15 Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
And Sellum, the sone of Colozai, prince of a toun Maspha, bildide the yate of the welle; he bildide it, and hilide, and settide the yatis therof, and lockis, and barris; and he bildide the wallis of the cisterne of Ciloe `til in to the orchard of the kyng, and `til to the greces of the kyng, that comen doun fro the citee of Dauid.
16 Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
Nemye, the sone of Azboch, prince of the half part of the street of Bethsury, bildide after hym til ayens the sepulcre of Dauid, and `til to the cisterne, which is bildide with greet werk, and `til to the hous of stronge men.
17 Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
Dekenes bildiden after hym; and Reum, the sone of Beny, bildide aftir hem. Asebie, the prince of half part of the street of Cheile, bildide in his street aftir hym.
18 Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
The britheren of hem, Bethyn, the sone of Enadab, prince of the half part of Cheyla, bildiden after hym.
19 Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
And Aser, the sone of Josue, prince of Maspha, bildide bisidis hym the secounde mesure ayens the stiyng of the `moost stidefast corner.
20 Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
Baruch, the sone of Zachay, bildide aftir hym in the hil the secounde mesure fro the corner `til to the yate of the hows of Eliasiph, the greet prest.
21 Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
Marymuth, the sone of Vrie, sone of Zaccur, bildide after hym the secounde mesure fro the yate of Eliasiph, as fer as the hows of Eliasiph was stretchid forth.
22 Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
And prestis, men of the feeldi places of Jordan, bildiden aftir hym.
23 Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
Beniamyn and Asub bildiden after hem ayens her hows; and Azarie, the sone of Maasie, sone of Ananye, bildide aftir hym ayens his owne hows.
24 Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
Bennuy, the sone of Senadad, bildide after hym the secounde mesure fro the hows of Azarie `til to the bowyng and `til to the corner.
25 Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
Phalel, the sone of Ozi, bildide ayens the bowyng, and the tour that stondith forth, fro the hiy hows of the kyng, that is in the large place of the prisoun; Phadaie, the sone of Pheros, bildide after hym.
26 ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
Forsothe Nathynneis dwelliden in Ophel til ayens the yate of watris at the eest, and the tour that apperide.
27 Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
Aftir hym men of Thecue bildiden the secounde mesure euene ayens, fro the greet tour and apperynge `til to the wal of the temple.
28 Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
Forsothe prestis bildiden aboue at the yate of horsis, ech man ayens his hows.
29 Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
Seddo, the sone of Enner, bildide ayens his hows aftir hem. And Semeie, the sone of Sechenye, the kepere of the eest yate, bildide after hym.
30 Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
Ananye, the sone of Selemye, and Anon, the sixte sone of Selon, bildide aftir hym the secounde mesure. Mosallam, the sone of Barachie, bildide ayenus his tresorie after hym.
31 Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
Melchie, the sone of a goldsmiyt, bildide aftir hym `til to the hows of Nathynneis, and of men sillynge scheldis ayens the yate of iugis, and `til to the soler of the corner.
32 Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.
And crafti men and marchauntis bildiden with ynne the soler of the corner and the yate of the kyng.

< Nehemiya 3 >