< Nehemiya 2 >

1 Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake.
А месеца Нисана године двадесете Артаксеркса цара беше вино пред њим, и ја узевши вино дадох га цару. А пре не бејах невесео пред њим.
2 Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.” Ine ndinachita mantha kwambiri.
И рече ми цар: Што си лица невеселог, кад ниси болестан? Није друго него туга у срцу. А ја се уплаших врло.
3 Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”
И рекох цару: Да је жив цар до века! Како не бих био лица невеселог, кад је град где су гробови мојих отаца опустео и врата му огњем спаљена?
4 Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?” Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba.
А цар ми рече: Шта хоћеш? Тада се помолих Богу небеском,
5 Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”
И рекох цару: Ако је угодно цару и ако ти је мио слуга твој, пошљи ме у Јудеју у град где су гробови отаца мојих да га саградим.
6 Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.
А цар ми рече, а жена његова сеђаше до њега: Колико ти времена треба на пут, и кад ћеш се вратити? И би угодно цару, и пусти ме кад му казах време.
7 Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda.
Потом рекох цару: Ако је угодно цару, да ми се да књига на кнезове преко реке да ме прате докле не дођем у Јудеју,
8 Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane.
И књига на Асафа, чувара шуме цареве да ми да дрва за брвна на врата од двора уз дом Божји и за зид градски и за кућу у коју ћу ући. И даде ми цар, јер добра рука Бога мог беше нада мном.
9 Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.
И тако дођох са кнезовима преко реке, и дадох им књиге цареве. А цар посла са мном војводе и коњике.
10 Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.
А кад то чу Санавалат Ороњанин и Товија, слуга Амонац, би им врло мрско што дође човек да се постара за добро синовима Израиљевим.
11 Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu.
Потом дођох у Јерусалим, и бих онде три дана.
12 Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.
Па устах ноћу с неколико људи, а ником не казах шта ми је Бог мој дао у срце да учиним у Јерусалиму; и не имах кљусета са собом осим оног на коме јахах.
13 Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto.
И изиђох ноћу на врата од долине, на извор змајевски, и на врата гнојна, и разгледах зидове јерусалимске како беху разваљени и како му врата беху огњем попаљена.
14 Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse.
Отуда прођох на изворска врата и на царско језеро, а онде не беше места да кљусе пода мном пређе.
15 Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa.
Зато јахах уз поток по ноћи и разгледах зид, па се вратих на врата од долине, и тако дођох натраг.
16 Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.
Али поглавари не знаху куда сам ишао ни шта сам радио, јер дотада не бејах ништа рекао ни Јудејцима ни свештеницима ни кнезовима ни поглаварима ни другима који управљаху послом.
17 Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.”
Зато им рекох: Видите у каквом смо злу, Јерусалим пуст и врата му попаљена огњем; дајте да зидамо зидове јерусалимске, да више не будемо руг.
18 Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza. Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.
И казах им како је добра рука Бога мог нада мном и речи цареве које ми је рекао. Тада рекоше: Устанимо и зидајмо. И укрепише им се руке на добро.
19 Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”
А кад то чу Санавалат Ороњанин и Товија, слуга Амонац и Гисем Арапин, подсмеваше нам се и ругаше нам се говорећи: Шта то радите? Да се нећете одметнути цару?
20 Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”
А ја им одговорих и рекох: Бог небески даће нам срећу, а ми, слуге Његове устасмо и зидамо; али ви немате дела ни права ни спомена у Јерусалиму.

< Nehemiya 2 >