< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
Ngalolosuku babala egwalweni lukaMozisi endlebeni zabantu; kwasekutholwa kubhaliwe kulo ukuthi umAmoni lomMowabi kabasoze bangene ebandleni likaNkulunkulu phakade;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
ngoba bengahlangabezanga abantwana bakoIsrayeli ngesinkwa langamanzi, kodwa baqhatsha bemelene labo uBalami, ukubaqalekisa; kodwa uNkulunkulu wethu waphendula isiqalekiso saba yisibusiso.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
Kwasekusithi sebewuzwile umlayo behlukanisa koIsrayeli yonke ingxube yezizwe.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
Ngaphambi kwalokho-ke uEliyashibi umpristi owayemiswe phezu kwekamelo likaNkulunkulu wethu, wayeyisihlobo sikaTobiya.
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
Wayemlungisele ikamelo elikhulu lapho ababekade befaka khona umnikelo wokudla, impepha, lezitsha, lokwetshumi kwamabele, iwayini elitsha, lamafutha, okwakulayelwe amaLevi labahlabeleli labalindimasango, lomnikelo wabapristi.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
Kodwa kukho konke lokhu ngangingekho eJerusalema, ngoba ngomnyaka wamatshumi amathathu lambili kaAthakisekisi inkosi yeBhabhiloni ngeza enkosini; lekupheleni kwezinsuku ngacela imvumo enkosini,
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
ngeza eJerusalema, ngaqedisisa ngokubi uEliyashibi ayekwenzele uTobiya ngokumlungisela ikamelo emagumeni endlu kaNkulunkulu.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
Kwasekusiba kubi kakhulu kimi; ngakho ngaphosela phandle zonke impahla zendlu kaTobiya phandle kwekamelo.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
Ngasengilaya, bahlambulula amakamelo; ngabuyisela khona izitsha zendlu kaNkulunkulu lomnikelo wokudla lempepha.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
Ngasengisazi ukuthi izabelo zamaLevi zazinganikwanga, lokuthi amaLevi labahlabeleli ababesenza umsebenzi babalekela ngulowo ensimini yakhe.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
Ngasengiphikisana lababusi ngathi: Kungani indlu kaNkulunkulu itshiyiwe? Ngababuthanisa, ngabamisa endaweni yabo.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
Khona wonke uJuda waletha okwetshumi kwamabele lewayini elitsha lamafutha eziphaleni.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
Ngasengibeka abagciniziphala phezu kweziphala, oShelemiya umpristi, loZadoki umbhali, loPhedaya kumaLevi, leceleni kwabo uHanani indodana kaZakuri indodana kaMathaniya, ngoba kwathiwa bathembekile; njalo kwakuphezu kwabo ukwabela abafowabo.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Ngikhumbule, Nkulunkulu wami, mayelana lalokho, ungayicitshi imisebenzi yami yomusa engiyenzele indlu kaNkulunkulu wami lezinkonzo zayo.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
Ngalezonsuku ngabona koJuda abanyathela izikhamelo zewayini ngesabatha, labangenisa izithungo, abathwalisa obabhemi, lewayini futhi, izithelo zesivini, lemikhiwa, lawo wonke umthwalo, abakungenisa eJerusalema ngosuku lwesabatha. Ngafakaza mhla bethengisa ukudla.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
LabeTire bahlala kuyo, beletha inhlanzi lempahla yonke ethengiswayo, bakuthengisa ngesabatha kubantwana bakoJuda laseJerusalema.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Khona ngaphikisana lezikhulu zakoJuda, ngathi kuzo: Iyini le into embi eliyenzayo lingcolisa usuku lwesabatha?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Kabenzanga njalo yini oyihlo, loNkulunkulu wethu wehlisela phezu kwethu bonke lobububi laphezu kwalumuzi? Kanti lina landisa ulaka phezu kukaIsrayeli ngokungcolisa isabatha.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
Kwasekusithi lapho amasango eJerusalema eseqala ukuba mnyama mandulo kwesabatha, ngalaya ukuthi iminyango kayivalwe, njalo ngalaya ukuthi bangayivuli kuze kube ngemva kwesabatha. Ngabeka ezinye zenceku zami emasangweni ukuze kungangeni mthwalo ngosuku lwesabatha.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
Ngakho abathengi labathengisi bempahla yonke balala ngaphandle kweJerusalema kanye loba kabili.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
Khona ngafakaza ngimelene labo ngathi kibo: Lilalelani maqondana lomduli? Uba likwenza futhi, ngizalidumela ngesandla. Kusukela kulesosikhathi kababuyanga ngesabatha.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
Ngasengitshela amaLevi ukuthi azihlambulule, eze alinde amasango, ukungcwelisa usuku lwesabatha. Langalokho ungikhumbule, Nkulunkulu wami, ungihawukele ngokobunengi bomusa wakho.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
Futhi, ngalezonsuku ngabona amaJuda ayethethe abafazi, abangamaAshidodikazi, amaAmoni, amaMowabi.
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
Labantwana babo, ingxenye babekhuluma isiAshidodi njalo bengelakukhuluma isiJuda, kodwa ngokolimi lwezizwe ngezizwe.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
Ngasengiphikisana lawo, ngawaqalekisa, ngatshaya amanye awo, ngawangcothula inwele; ngawafungisa ngoNkulunkulu: Kaliyikunika amadodakazi enu kumadodana abo, njalo kaliyikuthathela amadodana enu emadodakazini abo, kumbe lina ngokwenu.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
USolomoni inkosi yakoIsrayeli konanga yini ngalezozinto? Kube kanti phakathi kwezizwe ezinengi kwakungelankosi enjengaye, owayethandeka kuNkulunkulu wakhe, loNkulunkulu wamenza inkosi phezu kukaIsrayeli wonke; laye abafazi bezizweni bamenza ukuthi one.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
Pho, sizalilalela yini ukwenza bonke lobobubi obukhulu, ngokona kuNkulunkulu wethu ngokuthatha abafazi bezizweni?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
Lenye yamadodana kaJehoyada indodana kaEliyashibi umpristi omkhulu, yayingumkhwenyana kaSanibhalathi umHoroni; ngakho ngayixotsha yasuka kimi.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Bakhumbule, Nkulunkulu wami, ngoba bangcolisile ubupristi lesivumelwano sobupristi lesamaLevi.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Ngokunjalo ngabahlambulula kubo bonke abezizweni, ngamisa imfanelo kubapristi lakumaLevi, ngulowo lalowo emsebenzini wakhe,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
leyomnikelo wenkuni ngezikhathi ezimisiweyo, leyezithelo zokuqala. Ngikhumbule, Nkulunkulu wami, ngokuhle.

< Nehemiya 13 >