< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
En ce temps-là, on lut dans le livre de Moïse en présence du peuple, et l’on y trouva écrit que ni Ammonite ni Moabite ne seraient jamais admis dans l’assemblée de Dieu;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
pour n’avoir pas offert le pain et l’eau aux enfants d’Israël et pour avoir stipendié contre eux Balaam, à l’effet de les maudire malédiction que notre Dieu transforma en bénédiction.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
Lorsqu’on eut entendu la loi, on élimina d’Israël tout élément hétérogène.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
Avant cela, Elyachib, le prêtre, qui occupait une salle de la maison de notre Dieu et qui était parent de Tobia,
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
avait agencé pour celui-ci une grande salle, où l’on déposait précédemment les oblations, l’encens, les ustensiles, ainsi que la dîme du blé, du moût et de l’huile, redevance régulière des Lévites, des chanteurs et des portiers, et le tribut des prêtres.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
Pendant que tout cela se passait, j’étais absent de Jérusalem; car la trente-deuxième année d’Artahchasta, roi de Babylone, j’étais retourné auprès du roi. Au bout d’un certain temps, je sollicitai un nouveau congé du roi,
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
et je revins à Jérusalem. Alors je me rendis compte de la mauvaise action qu’avait commise Elyachib au profit de Tobia, en lui agençant une salle dans les parvis de la maison de Dieu,
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
cela me déplut beaucoup, et je fis jeter hors de la salle les ustensiles de ménage de Tobia.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
Sur mon ordre, on purifia les salles, et j’y fis réintégrer les vases de la maison de Dieu, les oblations et l’encens.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
J’Appris également que les redevances des Lévites n’étaient pas acquittées, et que Lévites et chanteurs, chargés du service, s’étaient enfuis chacun vers son champ.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
J’Adressai des remontrances aux chefs et leur dis: "Pourquoi le temple de Dieu est-il déserté?" Et je recueillis les fuyards et les rendis à leurs fonctions.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
Tout Juda apporta la dîme du blé, du moût et de l’huile dans les dépôts.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
Et je plaçai à la direction de ces dépôts Chélémia, le prêtre, Çadok, le scribe, et Pedaïa, un des Lévites, en leur adjoignant Hanân, fils de Zaccour, fils de Mattania, car ils étaient considérés comme intègres. A eux fut confié le soin de la répartition entre leurs frères.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Tiens-moi compte de cela, mon Dieu, et n’efface pas le souvenir des services que j’ai rendus à la maison de Dieu et à son fonctionnement!
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
A la même époque, je vis en Juda des gens qui foulaient des pressoirs le jour du sabbat et qui transportaient, à dos d’âne, des charges de blé et aussi du vin, des raisins, des figues et toute autre denrée pour les introduire à Jérusalem le jour du sabbat; et je les admonestai le jour où ils procédaient à la vente de ces comestibles.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
Les Tyriens s’étaient établis dans la ville, qui apportaient du poisson et d’autres marchandises et qui les débitaient, le sabbat, aux Judéens dans Jérusalem même.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Je fis des reproches aux nobles de Juda et leur dis: "Comment pouvez-vous commettre une si mauvaise action, de profaner le sabbat?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
N’Est-ce pas ainsi qu’ont agi vos pères, de telle sorte que notre Dieu a fait fondre tous ces désastres sur nous et sur cette ville? Et vous, vous augmentez encore la colère divine contre Israël, en profanant le sabbat!"
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
Dès que les portes de Jérusalem commençaient à s’assombrir, la veille du sabbat, je donnai ordre d’en fermer les battants et de ne les rouvrir que le sabbat une fois passé. Je postai aussi quelques-uns de mes gens près des portes pour empêcher qu’aucune charge ne fût introduite le jour du sabbat.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
Les marchands et les débitants de toute espèce passèrent donc la nuit en dehors de Jérusalem, une ou deux fois.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
Mais je leur donnai un avertissement et leur dis: "Pourquoi vous tenez-vous, la nuit, devant la muraille? Si vous recommencez, je vous repousserai par la force." A partir de ce moment, ils ne vinrent plus le sabbat.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
Je recommandai aussi aux Lévites de se mettre en état de pureté et de venir garder les portes pour sanctifier le jour du sabbat: cela aussi, tiens-m’en compte, ô mon Dieu, et protège-moi selon l’abondance de ta grâce!
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
En ces temps-là aussi, je vis les Judéens qui avaient épousé des femmes d’Asdod, d’Ammon et de Moab.
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
La moitié de leurs enfants parlaient la langue d’Asdod; ils ne savaient point parler le judéen, mais se servaient de l’idiome de tel ou tel autre peuple.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
Je les pris à partie, les menaçai de malédictions, en frappai quelques-uns, leur arrachai les cheveux; et je les adjurai au nom de Dieu: "Ne donnez pas, leur dis-je, vos filles à leurs fils et ne prenez pas de leurs filles comme épouses pour vos fils et pour vous!
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
N’Est-ce en cela que Salomon, roi d’Israël, a failli, lui qui n’avait point son pareil parmi les rois des grandes nations, qui était aimé de son Dieu, et qui avait été, par lui, établi roi de tout Israël? Pourtant les femmes étrangères l’entraînèrent au péché!
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
Quant à vous, n’est-ce pas une chose inouïe que vous commettiez ce grand méfait de vous montrer infidèles envers notre Dieu, en épousant des femmes étrangères?"
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
Même un des fils de Joïada, fils d’Elyachib, le grand-prêtre, était devenu le gendre de Sanballat, le Horonite: je le chassai de ma présence.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Mon Dieu, tiens-leur compte de cette profanation du pontificat et du pacte imposé aux prêtres et aux Lévites!
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Je les purifiai ainsi de tout élément étranger, et j’établis des sections pour les prêtres et les Lévites, assignant à chacun sa besogne,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
ainsi que des surveillants pour les offrandes du bois à des époques déterminées et pour les prémices. Mon Dieu, veuille m’en garder le souvenir pour mon bonheur!

< Nehemiya 13 >