< Nehemiya 13 >
1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
On that day there was read in the book of Moses before the ears of the people; and there was found written therein, that no 'Ammonite or Moabite should come into the congregation of God for ever;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
Because they had not met the children of Israel with bread and with water, but had hired Bil'am against them, that he should curse them; although our God had changed the curse into a blessing.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
And it tame to pass, when they had heard the law, that they separated all the alien mixture from Israel.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
And before this, Elyashib the priest, appointed over the chambers of the house of our God, and a near [of kin] unto Tobiyah,
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
Had prepared for him a large chamber, where they had laid in former times the meat-offerings, the frankincense, and the vessels, and the tithes of the corn, the new wine, and the oil, which was ordained for the Levites, and the singers, and the gatekeepers, and the heave-offering of the priests.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
But during all this I was not at Jerusalem; for in the two and thirtieth year of Artaxerxes the king of Babylon I went back unto the king, and after the lapse of some time I obtained by request [leave] of the king;
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
And I came to Jerusalem, and perceived the evil that Elyashib had done for Tobiyah, in preparing for him a chamber in the courts of the house of God.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
And it displeased me greatly: wherefore I cast forth all the household vessels of Tobiyah away out of the chamber.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
And I gave the order, whereupon they cleansed the chambers; and I had brought thither again the vessels of the house of God, with the meat-offering and the frankincense.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
And I perceived that the portions of the Levites had not been given [them]: so that the Levites and the singers, that used to do the work, were fled every one to his field.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
Then contended I with the rulers, and said, Why hath the house of God become forsaken? And I gathered them together, and placed them on their posts.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
And all Judah brought the tithe of the corn and the new wine and the oil unto the treasuries.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
And I appointed receivers over the treasuries, Shelemyah the priest and Zadok the scribe, and Pedayah of the Levites; and with them acted Chanan the son of Zaccur, the son of Matthanyah; for they were accounted as faithful, and it was their duty to make a distribution among their brethren.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Remember me, O my God, concerning this, and wipe not out my pious deeds which I have done for the house of my God, and for those that had charge of it.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
In those days I saw in Judah some treading wine-presses on the sabbath, and bringing in sheaves, and lading burdens on asses, as also wine, grapes and figs, and all manner of burdens, which they brought into Jerusalem on the sabbath day; and I warned them on the day whereon they sold provisions.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
Also the men of Tyre [that] dwelt therein brought fish and all kinds of wares, and sold [them] on the sabbath unto the children of Judah and in Jerusalem.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Then I contended with the nobles of Judah, and said unto them, What evil thing is this which ye are doing, and profaning [thereby] the sabbath day?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Did not your fathers act thus, wherefore our God brought over us all this evil, and over this city? and ye bring yet more wrath over Israel by profaning the sabbath.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
And it came to pass, that, when the shadows were lengthened in the gates of Jerusalem before the sabbath, I gave the order, whereupon the gates were locked, and I ordered that they should not be opened till after the sabbath: and some of my young men did I place at the gates, that there should be brought in no burden on the sabbath-day.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
But the merchants and sellers of all kinds of wares lodged outside of Jerusalem once or twice.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
Thereupon did I warn them, and said unto them, Why do ye lodge along the wall? if ye do so again, I will lay hands on you. From that time forth they came no more on the sabbath.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
And I ordered the Levites that they should cleanse themselves, and that they should come and keep watch at the gates, to sanctify the sabbath-day. Also this remember unto me, O my God, and shield me according to the abundance of thy kindness.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
In those days also I saw certain Jews that had brought home wives of Ashdod, of 'Ammon, and of Moab:
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
And their children spoke partly in the speech of Ashdod, and did not understand to speak in the Jewish language, but according to the language of one or the other people.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
And I contended with them, and cursed them, and smote certain of them, and plucked out their hair, and made them swear by God, saying, Ye shall not give your daughters unto their sons, nor take their daughters for your sons, nor for yourselves.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Did not Solomon the king of Israel sin by these things? and although among the many nations there was never a king like him, and beloved as he was by his God, and God had placed him as king over all Israel: nevertheless even him did the alien women mislead to sin.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
Shall we then hear it said of you, that ye do all this great evil, to trespass against our God in bringing home alien wives?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
And one of the sons of Joyada', the son of Elyashib the high priest, was son-in-law to Sanballat the Choronite; wherefore I chased him away from me.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Remember [this] unto them, O my God, because of the defilements of the priesthood, and of the covenant of the priesthood, and of the Levites.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Thus cleansed I them from all aliens, and I appointed the watches of the priests and the Levites, every one in his work;
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
And for the procuring of the wood, at fixed time, and for the first-fruits. Remember this unto me, O my God, for good.