< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
V ten den čteno jest v knize Mojžíšově, tak že lid slyšeti mohl. I nalezeno v ní napsáno, že nemá vjíti Ammonitský a Moábský do shromáždění Božího až na věky,
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
Proto že nevyšli proti synům Izraelským s chlebem a s vodou, ale najali ze mzdy proti nim Baláma, aby jim zlořečil, ačkoli obrátil Bůh náš to zlořečení v požehnání.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
Stalo se pak, když slyšeli zákon, že odmísili všecky přimíšené od Izraele.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
Ale před tím Eliasib kněz, správce komory domu Boha našeho, spříznil se s Tobiášem.
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
Kterémuž udělal pokoj veliký, kdež prvé skládali dary, kadidlo a nádoby, a desátky z obilé, mstu a oleje nového, nařízené Levítům a zpěvákům i vrátným, též i obět kněžím.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
Ale když se to vše dálo, nebyl jsem v Jeruzalémě. Nebo léta třidcátého druhého Artaxerxa krále Babylonského přišel jsem k králi, a po přeběhnutí let, vyžádán jsem na králi.
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Když jsem pak přišel do Jeruzaléma, srozuměl jsem tomu zlému, co učinil Eliasib pro Tobiáše, udělav mu pokoj v síních domu Božího.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
Což mi se velmi nelíbilo. Protož vyházel jsem všecko nádobí domu Tobiášova ven z toho pokoje.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
A rozkázal jsem očistiti ty pokoje. I vnesl jsem tam zase nádoby domu Božího, dary a kadidlo.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
Potom dověděv se, že dílové Levítům nebyli dáváni, a že rozběhli se jeden každý na svou rolí, Levítové i zpěváci vedoucí práci,
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
Protož domlouval jsem se na starší, řka: Proč jest opuštěn dům Boží? A shromáždiv je, postavil jsem je na místě jejich.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
A všecken Juda přinášeli desátky obilé, mstu a oleje nového do skladů.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
A ustanovil jsem úředníky nad sklady: Selemiáše kněze, a Sádocha učitele, a Pedaiáše z Levítů, přidav k nim Chanana syna Zakurova, syna Mattaniášova; nebo za věrné jmíni byli. A ti měli rozdělovati bratřím svým.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Budiž pamětliv na mne, Bože můj, pro to, a nevyhlazuj dobrodiní mých, kteráž jsem prokázal k domu Boha svého i k službám jeho.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
V těch dnech viděl jsem v Judstvu, ani tlačí presem v sobotu, a přinášejí snopy, kteréž nakládali na osly, též víno, hrozny, fíky i všeliká břemena, a snášejí v den sobotní do Jeruzaléma. I domlouval jsem jim v ten den, když prodávali potravu.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
Tyrští také, kteříž bydlili v něm, nosili ryby i všelijaké koupě, a prodávali v sobotu synům Juda, a to v Jeruzalémě.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Protož jsem domlouval starším Judským, a řekl jsem jim: Jaká jest to nepravost, kterouž činíte, poškvrňujíce dne sobotního?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Zdaliž jsou tak nečinili otcové vaši? Pročež Bůh náš přivedl na nás všecko toto zlé, i na toto město, a vy přidáváte hněvivosti na Izraele, poškvrňujíce soboty.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
Když tedy byly v stínu brány Jeruzalémské před sobotou, rozkázal jsem zavříti brány, a rozkázal jsem, aby jich neotvírali až po sobotě. K tomu i z služebníků svých některé postavil jsem v bráně, aby náklad nebyl vezen do města v sobotu.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
Protož zůstali kupci a prodavači všelijakých věcí prodajných vně před Jeruzalémem, jednou i podruhé.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
I osvědčil jsem se jim, řka jim: Proč zůstáváte přes noc naproti zdi? Učiníte-li to více, vztáhnu ruku na vás. Od té chvíle nepřicházeli v sobotu.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
Rozkázal jsem pak Levítům, aby se očistili, a přijdouce, ostříhali bran, a světili den sobotní. Také i v tom pamatuj na mne, Bože můj, a buď mi milostiv podlé množství milosrdenství svého.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
V těch dnech spatřil jsem také Židy, kteříž byli pojali ženy Azotské, Ammonitské a Moábské,
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
An synové jejich mluvili od polu Azotsky, a neuměli mluviti Židovsky, ale podlé jazyku každého toho lidu.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
Protož domlouval jsem jim, a zlořečil jsem jim, a některé z nich bil jsem a rval, přísahou je zavazuje skrze Boha, řka: Budete-li dávati dcery své synům jejich, aneb bráti dcery jejich synům svým neb sobě, zlořečení budete.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Zdaliž tím nezhřešil Šalomoun král Izraelský? Ješto ve mnohých národech nebylo krále jemu podobného, kterýž byl milý Bohu svému, tak že ustanovil jej Bůh králem nade vším Izraelem, však i toho k hříchu přivedly ženy cizozemky.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
A vám zdali povolíme, abyste se dopouštěli všeho toho zlého velikého, a přestupovali proti Bohu svému, pojímajíce ženy cizozemky?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
Z synů pak Joiady syna Eliasiba, kněze nejvyššího, jeden byl zeť Sanballata Choronského, kteréhož jsem zahnal od sebe.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Budiž pamětliv na to, Bože můj, proti těm, kteříž poškvrňují kněžství, a smlouvy kněžské i Levítské.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Protož jsem je vyčistil od všelikého cizozemce, a ustanovil jsem zase třídy kněžím a Levítům, jednomu každému v práci jeho,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
I nošení dříví k obětem časy uloženými, též i prvotin. Budiž pamětliv na mne, Bože můj, k mému dobrému.

< Nehemiya 13 >