< Nehemiya 11 >

1 Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
Ngakho ababusi babantu bahlala eJerusalema; abantu abaseleyo basebesenza inkatho yokuphosa ukuze balethe oyedwa kwabalitshumi ukuhlala eJerusalema umuzi ongcwele, lengxenye eziyisificamunwemunye kweminye imizi.
2 Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
Abantu basebebusisa wonke amadoda azinikela ngesihle ukuyahlala eJerusalema.
3 Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
Lezi-ke zinhloko zesabelo ezahlala eJerusalema. Kodwa emizini yakoJuda bahlala, ngulowo kumfuyo yakhe, emizini yabo: UIsrayeli, abapristi, lamaLevi, lamaNethini, labantwana benceku zikaSolomoni.
4 Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
EJerusalema kwahlala-ke abanye babantwana bakoJuda lababantwana bakoBhenjamini. Ebantwaneni bakoJuda: OAthaya indodana kaUziya indodana kaZekhariya indodana kaAmariya indodana kaShefathiya indodana kaMahalaleli, owabantwana bakoPerezi,
5 Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
loMahaseya indodana kaBharukhi indodana kaKolihoze indodana kaHazaya indodana kaAdaya indodana kaJoyaribi indodana kaZekhariya indodana kaShiloni.
6 Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
Wonke amadodana kaPerezi ayehlala eJerusalema ayengamakhulu amane lamatshumi ayisithupha lesificaminwembili, amadoda alamandla.
7 Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
Lala ngamadodana kaBhenjamini: USalu indodana kaMeshulamu indodana kaJowedi indodana kaPhedaya indodana kaKolaya indodana kaMahaseya indodana kaIthiyeli indodana kaJeshaya,
8 Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
langemva kwakhe oGabayi, uSalayi, amakhulu ayisificamunwemunye lamatshumi amabili lesificaminwembili.
9 Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
LoJoweli indodana kaZikiri wayengumboni phezu kwabo, loJuda indodana kaHasenuwa engowesibili phezu komuzi.
10 Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
Kubapristi: OJedaya indodana kaJoyaribi, uJakini,
11 Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
uSeraya indodana kaHilikhiya indodana kaMeshulamu indodana kaZadoki indodana kaMerayothi indodana kaAhitubi, umphathi wendlu kaNkulunkulu,
12 ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
labafowabo ababesenza umsebenzi wendlu babengamakhulu ayisificaminwembili lamatshumi amabili lambili; loAdaya indodana kaJerohamu indodana kaPelaliya indodana kaAmzi indodana kaZekhariya indodana kaPashuri indodana kaMalikiya,
13 ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
labafowabo, inhloko zaboyise, babengamakhulu amabili lamatshumi amane lambili; loAmashayi indodana kaAzareli indodana kaAhizayi indodana kaMeshilemothi indodana kaImeri,
14 ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
labafowabo, amaqhawe alamandla, ikhulu lamatshumi amabili lesificaminwembili; lomboni phezu kwabo wayenguZabidiyeli indodana yomunye wabakhulu.
15 Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
LakumaLevi: OShemaya indodana kaHashubi indodana kaAzirikamu indodana kaHashabhiya indodana kaBuni;
16 Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
loShabethayi loJozabadi bezinhloko zamaLevi babephezu komsebenzi wangaphandle kwendlu kaNkulunkulu;
17 Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
loMathaniya indodana kaMika indodana kaZabidi indodana kaAsafi owayeyinhloko yokuqalisa ukubonga emkhulekweni; loBakibukiya owesibili kubafowabo; loAbida indodana kaShamuwa indodana kaGalali indodana kaJeduthuni.
18 Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
Wonke amaLevi emzini ongcwele ayengamakhulu amabili lamatshumi ayisificaminwembili lane.
19 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
Labalindimasango, oAkubi, uTalimoni, labafowabo ababelinda amasango babelikhulu lamatshumi ayisikhombisa lambili.
20 Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
Lensali yakoIsrayeli, ababapristi, amaLevi, babesemizini yonke yakoJuda, ngulowo elifeni lakhe.
21 Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
LamaNethini ayehlala eOfeli; loZiha loGishipa babephezu kwamaNethini.
22 Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
Njalo umboni wamaLevi eJerusalema wayenguUzi indodana kaBani indodana kaHashabhiya indodana kaMathaniya indodana kaMika. Owamadodana kaAsafi, abahlabeleli babeqondene lomsebenzi wendlu kaNkulunkulu.
23 Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
Ngoba kwakungumlayo wenkosi ngabo, njengokufunekayo kubahlabeleli, udaba losuku ngosuku lwalo.
24 Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
Njalo uPethahiya indodana kaMeshezabeli, owabantwana bakoZera indodana kaJuda, wayesesandleni senkosi kulo lonke udaba lwabantu.
25 Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
Lemizaneni lamasimu ayo, kwahlala abanye babantwana bakoJuda eKiriyathi-Arba lemizana yayo, laseDiboni lemizana yayo, laseJekabiseyeli lemizana yayo,
26 ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
laseJeshuwa, laseMolada, laseBeti-Peleti,
27 Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
laseHazari-Shuwali, laseBherishebha lemizana yayo,
28 Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
laseZikilagi, laseMekona lemizaneni yayo,
29 ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
laseEni-Rimoni, laseZora, laseJarimuthi,
30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
iZanowa, iAdulamu lemizana yayo, iLakishi lamasimu ayo, iAzeka lemizana yayo. Basebemisa inkamba kusukela eBherishebha kusiya esihotsheni seHinomu.
31 Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
Labantwana bakoBhenjamini kusukela eGeba babeseMikimashi, leAyija, leBhetheli lemizana yayo,
32 ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
iAnathothi, iNobi, iAnaniya,
33 ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
iHazori, iRama, iGithayimi,
34 ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
iHadidi, iZeboyimi, iNebalati,
35 ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
iLodi, leOno, isigodi sezingcitshi.
36 Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.
LakumaLevi kwakulezigaba zakoJuda loBhenjamini.

< Nehemiya 11 >