< Nehemiya 11 >

1 Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
And the rulers of the people dwelt in Jerusalem. The rest of the people also cast lots to bring one of ten to dwell in Jerusalem the holy city, and nine parts in the other cities.
2 Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
And the people blessed all the men who willingly offered themselves to dwell in Jerusalem.
3 Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
Now these are the chiefs of the province who dwelt in Jerusalem. But in the cities of Judah everyone dwells in his possession in their cities, namely, Israel, the priests, and the Levites, and the Nethinim, and the sons of Solomon's servants.
4 Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
And in Jerusalem certain of the sons of Judah, and of the sons of Benjamin dwelt. Of the sons of Judah: Athaiah the son of Uzziah, the son of Zechariah, the son of Amariah, the son of Shephatiah, the son of Mahalalel, of the sons of Perez;
5 Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
and Maaseiah the son of Baruch, the son of Col-hozeh, the son of Hazaiah, the son of Adaiah, the son of Joiarib, the son of Zechariah, the son of the Shilonite.
6 Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
All the sons of Perez who dwelt in Jerusalem were four hundred sixty-eight valiant men.
7 Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
And these are the sons of Benjamin: Sallu the son of Meshullam, the son of Joed, the son of Pedaiah, the son of Kolaiah, the son of Maaseiah, the son of Ithiel, the son of Jeshaiah.
8 Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
And after him Gabbai, Sallai, nine hundred twenty-eight.
9 Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
And Joel the son of Zichri was their overseer, and Judah the son of Hassenuah was second over the city.
10 Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
Of the priests: Jedaiah the son of Joiarib, Jachin,
11 Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Seraiah the son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub, the ruler of the house of God,
12 ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
and their brothers who did the work of the house, eight hundred twenty-two; and Adaiah the son of Jeroham, the son of Pelaliah, the son of Amzi, the son of Zechariah, the son of Pashhur, the son of Malchijah,
13 ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
and his brothers, chiefs of fathers, two hundred forty-two; and Amashsai the son of Azarel, the son of Ahzai, the son of Meshillemoth, the son of Immer,
14 ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
and their brothers, mighty men of valor, a hundred twenty-eight, and their overseer was Zabdiel, the son of Haggedolim.
15 Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
And of the Levites: Shemaiah the son of Hasshub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, the son of Bunni,
16 Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
and Shabbethai and Jozabad of the chiefs of the Levites who had the oversight of the outward business of the house of God,
17 Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
and Mattaniah the son of Mica, the son of Zabdi, the son of Asaph, who was the chief to begin the thanksgiving in prayer, and Bakbukiah, the second among his brothers, and Abda the son of Shammua, the son of Galal, the son of Jeduthun.
18 Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
All the Levites in the holy city were two hundred eighty-four.
19 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
Moreover the porters, Akkub, Talmon, and their brothers, who kept watch at the gates, were a hundred seventy-two.
20 Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
And the rest of Israel, of the priests, the Levites, were in all the cities of Judah, everyone in his inheritance.
21 Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
But the Nethinim dwelt in Ophel. And Ziha and Gishpa were over the Nethinim.
22 Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
The overseer also of the Levites at Jerusalem was Uzzi the son of Bani, the son of Hashabiah, the son of Mattaniah, the son of Mica, of the sons of Asaph, the singers, over the business of the house of God.
23 Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
For there was a commandment from the king concerning them, and a settled provision for the singers, as every day required.
24 Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
And Pethahiah the son of Meshezabel, of the sons of Zerah the son of Judah, was at the king's hand in all matters concerning the people.
25 Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
And as for the villages, with their fields, some of the sons of Judah dwelt in Kiriath-arba and the towns of it, and in Dibon and the towns of it, and in Jekabzeel and the villages of it,
26 ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
and in Jeshua, and in Moladah, and Beth-pelet,
27 Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
and in Hazar-shual, and in Beersheba and the towns of it,
28 Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
and in Ziklag, and in Meconah and in the towns of it,
29 ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
and in En-rimmon, and in Zorah, and in Jarmuth,
30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
Zanoah, Adullam, and their villages, Lachish and the fields of it, Azekah and the towns of it. So they encamped from Beersheba to the valley of Hinnom.
31 Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
The sons of Benjamin also dwelt from Geba onward, at Michmash and Aija, and at Bethel and the towns of it,
32 ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
at Anathoth, Nob, Ananiah,
33 ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
Hazor, Ramah, Gittaim,
34 ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
Hadid, Zeboim, Neballat,
35 ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
Lod, and Ono, the valley of craftsmen.
36 Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.
And of the Levites, certain courses in Judah were joined to Benjamin.

< Nehemiya 11 >