< Nehemiya 11 >
1 Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
Te vaengah pilnam mangpa rhoek tah Jerusalem ah kho a sak uh. Pilnam a coih te parha ah pakhat tah a cim khopuei Jerusalem ah khosa la khuen ham hmulung a naan uh. Pako rhoek tah khopuei kah hmatoeng ah omuh.
2 Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
Jerusalem kah khosa la aka puhlu hlang boeih te pilnam loh yoethen a paek.
3 Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
Paeng kah boeilu rhoek tah Jerusalem ah kho a sak uh. Tedae Judah khopuei khuikah rhoek tah amah kah khohut dongah rhip om uh. Amih kah khopuei rhoek ah Israel khosoih rhoek khaw, Levi rhoek khaw, tamtaeng rhoek khaw, Solomon kah sal koca rhoek khaw omuh.
4 Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
Jerusalem ah khaw Judah koca lamkah neh Benjamin koca lamkah rhoek loh kho a sak uh. Judah koca loh Uzziah capa Athaiah, Zekhariah capa Uzziah, Amariah capa Zekhariah, Shephatiah capa Amariah, Perez koca lamloh Mahalalel capa Shephatiah.
5 Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
Shiloh koca lamloh Zekhariah capa Joiarib, Joiarib capa Adaiah, Adaiah capa Hazaiah, Hazaiah capa Kolhozeh, Kolhozeh capa Barukh, Barukh capa Maaseiah.
6 Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
Jerusalem kah khosa Perez koca boeih he tatthai hlang ya li sawmrhuk parhet lo.
7 Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
Benjamin koca rhoek he tah Isaiah capa Ithiel, Ithiel capa Maaseiah, Maaseiah capa Kolaiah, Kolaiah capa Pedaiah, Pedaiah capa Joed, Joed capa Meshullam, Meshuulam capa Salu.
8 Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
A hnuk kah Gabbai, Salu neh ya ko pakul neh parhet lo.
9 Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
Amih soah Zikhri capa Joel te hlangtawt la om tih, Hassenuah capa Judah te hnukthoi khopuei ah om.
10 Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
Khosoih rhoek lamloh Joiarib capa Jedaiah, Jakhin.
11 Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Pathen im kah rhaengsang rhoek la Ahitub capa Meraioth, Meraioth capa Zadok, Zadok capa Meshullam, Meshullam capa Hikiah, Hilkiah capa Seraiah.
12 ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
A boeinaphung ah, BOEIPA im ham bitat aka saii rhoek tah ya rhet pakul panit lo. Malkhiah capa Pashur, Pashur capa Zekhariah, Zekhariah capa Amzi, Amzi capa Pelaliah, Pelaliah capa Jeroham, Jeroham capa Adaiah.
13 ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
A boeinaphung ah a napa rhoek kah boeilu he yahnih sawmli panit lo. Immer capa Meshillemoth, Meshillemoth capa Ahzai, Ahzai capa Azarel, Azarel capa Amashai.
14 ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
A boeinaphung ah tatthai hlangrhalh he ya pakul parhet lo tih amih soah Haggedolim capa Zabdiel te hlangtawt la om.
15 Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
Levi rhoek lamloh Buni capa Hashabiah, Hashabiah capa Azrikam, Azrikam capa Hasshub, Hasshub capa Shemaiah.
16 Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
Levi boeilu lamkah Shabbethai neh Jozabad loh Pathen im kah poengben kah bitat te a om thil.
17 Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
Boeilu lamhma Asaph capa Zabdi, Zabdi capa Maikah, Maikah capa Mattaniah loh thangthuinah te a uem. Bakbukiah khaw amah boeinaphung khuiah a pabae la om. Te phoeiah Jeduthun lamloh Jeduthun capa Galal, Galal capa Shammua, Shammua capa Abda.
18 Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
A cim khopuei kah Levi boeih tah yahnih sawmrhet pali lo.
19 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
Thoh tawt Akkub, Talmon neh a boeinaphung ah vongka aka ngaithuen rhoek te ya sawmrhih panit lo.
20 Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
Israel kah a coih, khosoih rhoek, Levi rhoek tah Judah kho tom ah amah rho dongah rhip omuh.
21 Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
Ophel kah khosa rhoek tah tamtaeng rhoek tih tamtaeng rhoek soah Ziha neh Gispha om.
22 Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
Jerusalem kah Levi hlangtawt khuiah khaw Asaph koca rhoek lamkah Mikha capa Mattaniah, Mattaniah capa Hashabiah, Hashabiah capa Bani, Bani capa Uzzi loh Pathen im kah bitat ham a hlai uh.
23 Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
Amih ham manghai olpaek neh a hnin, hnin kah bitat aka hlai rhoek ham olkamnah khaw om.
24 Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
Judah capa Zerah koca, Mezhezabel capa Pethahiah tah pilnam kah olka cungkuem dongah manghai kut la om.
25 Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
Judah koca lamkah rhoek khaw amah vongup, amah khohmuen neh kho a sak uh. Kiriatharba neh a khobuel ah, Dibon neh a khobuel ah, Jekabzeel neh a vangca rhoek ah omuh.
26 ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
Jeshua ah khaw, Moladah ah khaw, Bethpelet ah khaw,
27 Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
Hazarshual ah khaw, Beersheba neh a khobuel rhoek ah khaw,
28 Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
Ziklag ah khaw, Mekonah neh a khobuel rhoek ah khaw,
29 ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
Enrimmon ah khaw, Zorah ah khaw, Jarmuth ah khaw,
30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
Zanoah, Adullam neh a vangca rhoek, Lakhish neh a khohmuen rhoek, Azekah neh a khobuel rhoek ah khaw Beersheba lamloh kolrhawk duela rhaeh uh.
31 Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
Benjamin koca rhoek khaw Geba lamloh Mikmash, Ai, Bethel neh a khobuel rhoek ah,
32 ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
Anathoth, Nob, Ananiah,
33 ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
Hazor, Ramah, Gatayim,
34 ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
Hadid, Zeboim, Neballat,
35 ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
Lod neh Ono kolrhawk ah.
36 Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.
Levi lamkah rhoek khaw Benjamin kah Judah boelnah khuiah.