< Nehemiya 10 >
1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
Or, les signataires furent Néhémias Athersatha, fils d’Hachélaï, et Sédécias,
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
Saraïas, Azarias, Jérémie,
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pheshur, Amarias, Melchias,
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Hattus, Sébénia, Melluch,
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Harem, Mérimuth, Obdias,
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Genthon, Baruch,
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Mosollam, Abia, Miamin,
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Maazia, Belgaï, Séméia: ceux-là furent les prêtres.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
Mais les Lévites: Josué, fils d’Azanias; Bennuï, des fils de Hénadad, Cedmihel,
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
Et leurs frères, Sébénia, Odaïa, Célita, Phalaïa, Hanan,
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Micha, Rohob, Hasébia,
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zachur, Sérébia. Sabania,
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Odaïa, Bani, Baninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
Les chefs du peuple: Pharos, Phahathmoab, Elam, Zéthu, Bani,
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adonia, Bégoaï, Adin,
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Hézécia, Azur,
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Odaïa, Hasum, Bésaï,
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Hareph, Anathoth, Nébaï,
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Megphias, Mosollam, Hazir,
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Mésizabel, Sadoc, Jeddua,
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pheltia, Hanan, Anaïa,
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Osée, Hanania, Hasub,
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Alohès, Phaléa, Sobec,
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Réhum, Hasebna, Maasia,
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Melluch, Haran, Baana.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
Et le reste du peuple, les prêtres, les Lévites, les portiers et les chantres, les Nathinéens, et tous ceux qui s’étaient séparés des peuples de la terre pour la loi de Dieu, leurs femmes, leurs fils et leurs filles,
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
Tous ceux qui pouvaient être éclairés, répondant pour leurs frères; les grands aussi; enfin tous ceux qui venaient pour promettre et jurer qu’ils marcheraient dans la loi de Dieu, qu’il avait donnée par l’entremise de Moïse, serviteur de Dieu, qu’ils accompliraient et garderaient tous les commandements du Seigneur notre Dieu, et ses ordonnances et ses cérémonies,
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
Que nous ne donnerions point nos filles au peuple du pays, et que nous ne prendrions point leurs filles pour nos fils.
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
De plus, quant aux peuples du pays qui importent des objets de vente de toute sorte de choses de consommation, au jour du Sabbat, pour les vendre, nous ne les accepterons pas d’eux pendant le Sabbat, et en un jour sanctifié. Nous abandonnerons aussi la septième année et l’exaction de toute main.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
Et nous établirons pour nous comme préceptes de donner par an la troisième partie d’un sicle, pour l’œuvre de la maison de notre Dieu.
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
Pour les pains de proposition, et pour le sacrifice perpétuel, pour l’holocauste perpétuel dans les sabbats, dans les calendes, dans les solennités, et dans les choses sanctifiées et pour le péché, afin que l’on prie pour Israël, et pour le service de la maison de notre Dieu.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
Nous jetâmes donc les sorts, pour l’offrande des bois, entre les prêtres, les Lévites et le peuple, afin qu’ils fussent apportés dans la maison de notre Dieu, selon les maisons de nos pères, à des temps marqués, depuis les temps d’une année jusqu’à une autre année, afin qu’ils brûlassent sur l’autel du Seigneur notre Dieu, comme il est écrit dans la loi de Moïse.
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
Nous promîmes aussi et nous jurâmes, que nous apporterions les prémices de notre terre et les prémices de tous les fruits de tout arbre, d’année en année, dans la maison du Seigneur,
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
Et les premiers-nés de nos fils et de nos troupeaux, comme il est écrit dans la loi, et les prémices de nos bœufs et de nos brebis, pour être offerts dans la maison de notre Dieu, aux prêtres qui servent dans la maison de notre Dieu;
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
Les prémices aussi de nos aliments et de nos libations, et les fruits de tout arbre, de la vigne aussi bien que de l’olivier, nous les apporterons aux prêtres, pour le trésor de notre Dieu, et la dixième partie de notre terre aux Lévites. Eux-mêmes, les Lévites recevront de toutes les villes les dîmes de nos travaux.
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
Et le prêtre, fils d’Aaron, sera avec les Lévites dans les dîmes des Lévites; et les Lévites offriront la dixième partie de leur dîme dans la maison de notre Dieu, au lieu où on garde le trésor, dans la maison du trésor.
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
Car c’est au lieu où on garde le trésor que les enfants d’Israël et les enfants de Lévi apporteront les prémices du froment, du vin et de l’huile; et là seront les vases sanctifiés, les prêtres, les chantres, les portiers et les ministres, et nous n’abandonnerons pas la maison de notre Dieu.