< Nehemiya 10 >

1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
Et à la tête de ceux qui apposèrent leur sceau furent: Néhémie, le Thirshatha, fils de Hacalia, et Sédécias.
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
– Seraïa, Azaria, Jérémie,
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pashkhur, Amaria, Malkija,
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Hattush, Shebania, Malluc,
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Harim, Merémoth, Abdias,
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Guinnethon, Baruc,
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Meshullam, Abija, Mijamin,
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Maazia, Bilgaï, Shemahia: c’étaient là les sacrificateurs.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
– Et les lévites: Jéshua, fils d’Azania; Binnuï, des fils de Hénadad; Kadmiel,
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
et leurs frères, Shebania, Hodija, Kelita, Pelaïa, Hanan,
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Michée, Rehob, Hashabia,
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zaccur, Shérébia, Shebania,
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Hodija, Bani, Beninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
– Les chefs du peuple: Parhosh, Pakhath-Moab, Élam, Zatthu, Bani,
15 Buni, Azigadi, Bebai,
Bunni, Azgad, Bébaï,
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adonija, Bigvaï, Adin,
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Ézéchias, Azzur,
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Hodija, Hashum, Bétsaï,
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Hariph, Anathoth, Nébaï,
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Magpiash, Meshullam, Hézir,
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Meshézabeël, Tsadok, Jaddua,
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pelatia, Hanan, Anaïa,
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Osée, Hanania, Hashub,
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Hallokhesh, Pilkha, Shobek,
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Rehum, Hashabna, Maascéïa
26 Ahiya, Hanani, Anani,
et Akhija, Hanan, Anan,
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Malluc, Harim, Baana.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
Et le reste du peuple, les sacrificateurs, les lévites, les portiers, les chantres, les Nethiniens, et tous ceux qui s’étaient séparés des peuples des pays [pour s’attacher] à la loi de Dieu, leurs femmes, leurs fils et leurs filles, tous ceux qui avaient de la connaissance [et] de l’intelligence,
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
se joignirent à leurs frères, les principaux d’entre eux, et s’engagèrent par exécration et par serment de marcher selon la loi de Dieu qui avait été donnée par Moïse, serviteur de Dieu, et d’observer et de pratiquer tous les commandements de l’Éternel, notre Seigneur, et ses ordonnances et ses statuts,
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
et [promettant] que nous ne donnerions pas nos filles aux peuples du pays, et que nous ne prendrions pas leurs filles pour nos fils;
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
et que, si les peuples du pays apportaient des marchandises ou toutes sortes de grains, le jour du sabbat, pour les vendre, nous n’en prendrions pas le [jour du] sabbat, ni en un jour saint; et que nous laisserions [la terre en friche] la septième année, et remettrions toute espèce de dettes.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
Et nous nous sommes établi des commandements, nous imposant le tiers d’un sicle par an pour le service de la maison de notre Dieu,
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
pour les pains à placer en rangées, et pour l’offrande de gâteau continuelle, et pour les holocaustes, l’[holocauste] continuel, [celui] des sabbats, [et celui] des nouvelles lunes, pour les jours solennels et pour les choses saintes, et pour les sacrifices pour le péché, afin de faire propitiation pour Israël, et pour toute l’œuvre de la maison de notre Dieu.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
Et nous avons jeté le sort, sacrificateurs, lévites, et peuple, au sujet de l’offrande du bois à amener à la maison de notre Dieu, selon nos maisons de pères, à des époques fixes, chaque année, pour le brûler sur l’autel de l’Éternel, notre Dieu, comme il est écrit dans la loi.
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
Et [nous nous sommes engagés] à apporter les prémices de notre terre, et les prémices de tous les fruits de tous les arbres, chaque année, à la maison de l’Éternel,
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
et les premiers-nés de nos fils et de nos bêtes, comme il est écrit dans la loi; et à apporter les premiers-nés de notre gros et de notre menu bétail, à la maison de notre Dieu, aux sacrificateurs qui font le service dans la maison de notre Dieu:
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
et nous apporterons les prémices de notre pâte et nos offrandes élevées, et le fruit de tout arbre, le moût et l’huile, aux sacrificateurs, dans les chambres de la maison de notre Dieu, et les dîmes de notre terre aux lévites; et eux, les lévites, prélèveront la dîme dans toutes les villes de notre labour;
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
et le sacrificateur, fils d’Aaron, sera avec les lévites quand les lévites prélèveront la dîme, et les lévites apporteront la dîme de la dîme à la maison de notre Dieu, dans les chambres de la maison du trésor;
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
car les fils d’Israël et les fils de Lévi apporteront l’offrande élevée du blé, du moût, et de l’huile, dans les chambres où sont les ustensiles du sanctuaire, et les sacrificateurs qui font le service, et les portiers et les chantres. Et nous n’abandonnerons pas la maison de notre Dieu.

< Nehemiya 10 >