< Nehemiya 10 >

1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
And with those whose seal was affixed were, Nehemiah the Tirshatha the son of Chachalyah, and Zidkiyah.
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
[Then] Serayah, 'Azaryah, Jeremiah,
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pashchui, Amaryah, Malkiyah,
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Chattush, Shebanyah, Malluch,
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Charim, Meremoth, 'Obadiah,
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Ginnethon, Baruch,
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Meshullam, Abiyah, Miyamin,
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Ma'azyah, Bilgai, Shema'yah: these were the priests.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
And the Levites: Jeshua' the son of Azanyah, Binnui [[of]] the sons of Chenadad, Kadmiel;
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
And their brethren, Shebanyah, Hodiyah, Kelita, Palayah, Chanan,
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Micha, Rechob, Chashabyah,
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zaccur, Sherebyah, Shebanyah,
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Hodiyah, Bani, Beninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
The chiefs of the people: Par'osh, Pachath-moab, 'Elam, Zatthu, Bani,
15 Buni, Azigadi, Bebai,
Bunni, 'Azgad, Bebai,
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adoniyah, Bigvai, 'Adin,
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Chizkiyah, 'Azzur,
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Hodiyah, Chashum, Bezai,
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Chariph, 'Anathoth, Nebai,
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Magpi'ash, Meshullam, Chezir,
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Meshezabel, Zadok, Jaddua',
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pelatyah, Chanan, 'Anayah,
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Hoshea', Chanayah, Chasshub,
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Hallochesh, Pilcha, Shobek,
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Rechum, Chashabnah, Ma'asseyah,
26 Ahiya, Hanani, Anani,
And Achiyah, Chanan, 'Anan,
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Malluch, Charim, Ba'anah.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
And the rest of the people, the priests, the Levites, the gate-keepers, the singers, the temple-servants, and all those that had separated themselves from the nations of the lands unto the law of God, their wives, their sons, and their daughters, every one having knowledge, and having understanding,
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
Held firmly with their brethren, their nobles, and entered into a curse, and into an oath, to walk in the law of God, which was given through means of Moses the servant of God, and to observe and to do all the commandments of the Eternal One, our Lord, and his ordinances and his statutes;
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
And that we would not give our daughters unto the people of the land, nor take their daughters for our sons;
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
And that if the people of the land should bring wares or any provisions on the sabbath day to sell, we would not buy of them on the sabbath, or on [another] holy day; and that we would leave [the fields without reaping in] the seventh year, and [give up] every loan of hand.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
And we established for us as one of the commandments to impose on ourselves [to give] the third part of a shekel in every year for the service of the house of our God;
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
For the shew-bread, and for the continual meat-offering, and for the continual burnt-offering, [for those of] the sabbaths, of the new-moons, for the appointed feasts, and for the holy things, and for the sin-offerings to make an atonement for Israel, and [for] all the work of the house of our God.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
And we, the priests, the Levites, and the people, cast lots concerning the procuring of the wood, to bring it into the house of our God, unto the house of our fathers, at fixed times, year by year, to burn upon the altar of the Lord our God, as it is written in the law;
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
And to bring the first-fruits of our ground, and the first-fruits of all fruit of all trees, year by year, unto the house of the Lord;
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
And also the first-born of our sons, and for our [unclean] cattle, as it is written in the law, and to bring the first-born of our herds and of our flocks to the house of our God, unto the priests that minister in the house of our God;
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
And that we would bring the first portion of our dough, and our heave-offerings, and this of the fruit of all manner of trees, of wine and of oil, to the priests, unto the chambers of the house of our God, and the tithes of our ground unto the Levites; and that these same Levites should be the receivers of the tithes in all the cities of our land-tillage;
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
And that the priest the son of Aaron should be with the Levites, when the Levites receive the tithes; and that the Levites should bring up the tithe of the tithes unto the house of our God, to the chambers, into the treasure-house.
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
For into the chambers shall the children of Israel and the children of Levi bring the heave-offering of the corn, of the new wine, and the oil, and there shall be the vessels of the sanctuary, and the priests that minister, and the gatekeepers, and the singers: and that we will not forsake the house of our God.

< Nehemiya 10 >