< Nehemiya 10 >

1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
NOW those that sealed were, Nehemiah, the Tirshatha, the son of Hachaliah, and Zidkijah,
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
Seraiah, Azariah, Jeremiah,
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pashur, Amariah, Malchijah,
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Hattush, Shebaniah, Malluch,
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Harim, Meremoth, Obadiah,
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Ginnethon, Baruch,
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Meshullam, Abijah, Mijamin,
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Maaziah, Bilgai, Shemaiah: these were the priests.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
And the Levites: both Jeshua the son of Azaniah, Binnui of the sons of Henadad, Kadmiel;
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
And their brethren, Shebaniah, Hodijah, Kelita, Pelaiah, Hanan,
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Micha, Rehob, Hashabiah,
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zaccur, Sherebiah, Shebaniah,
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Hodijah, Bani, Beninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
The chief of the people; Parosh, Pahath-moab, Elam, Zatthu, Bani,
15 Buni, Azigadi, Bebai,
Bunni, Azgad, Bebai,
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adonijah, Bigvai, Adin,
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Hizkijah, Azzur,
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Hodijah, Hashum, Bezai,
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Hariph, Anathoth, Nebai,
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Magpiash, Meshullam, Hezir,
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Meshezabeel, Zadok, Jaddua,
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pelatiah, Hanan, Anaiah,
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Hoshea, Hananiah, Hashub,
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Hallohesh, Pileha, Shobek,
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Rehum, Hashabnah, Maaseiah,
26 Ahiya, Hanani, Anani,
And Ahijah, Hanan, Anan,
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Malluch, Harim, Baanah.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
And the rest of the people, the priests, the Levites, the porters, the singers, the Nethinims, and all they that had separated themselves from the people of the lands unto the law of God, their wives, their sons, and their daughters, every one having knowledge, and having understanding;
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
They clave to their brethren, their nobles, and entered into a curse, and into an oath, to walk in God’s law, which was given by Moses the servant of God, and to observe and do all the commandments of the Lord our Lord, and his judgments and his statutes;
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
And that we would not give our daughters unto the people of the land, nor take their daughters for our sons:
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
And if the people of the land bring ware or any victuals on the sabbath day to sell, that we would not buy it of them on the sabbath, or on the holy day: and that we would leave the seventh year, and the exaction of every debt.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
Also we made ordinances for us, to charge ourselves yearly with the third part of a shekel for the service of the house of our God;
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
For the shewbread, and for the continual meat offering, and for the continual burnt offering, of the sabbaths, of the new moons, for the set feasts, and for the holy things, and for the sin offerings to make an atonement for Israel, and for all the work of the house of our God.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
And we cast the lots among the priests, the Levites, and the people, for the wood offering, to bring it into the house of our God, after the houses of our fathers, at times appointed year by year, to burn upon the altar of the Lord our God, as it is written in the law:
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
And to bring the firstfruits of our ground, and the firstfruits of all fruit of all trees, year by year, unto the house of the Lord:
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
Also the firstborn of our sons, and of our cattle, as it is written in the law, and the firstlings of our herds and of our flocks, to bring to the house of our God, unto the priests that minister in the house of our God:
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
And that we should bring the firstfruits of our dough, and our offerings, and the fruit of all manner of trees, of wine and of oil, unto the priests, to the chambers of the house of our God; and the tithes of our ground unto the Levites, that the same Levites might have the tithes in all the cities of our tillage.
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
And the priest the son of Aaron shall be with the Levites, when the Levites take tithes: and the Levites shall bring up the tithe of the tithes unto the house of our God, to the chambers, into the treasure house.
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
For the children of Israel and the children of Levi shall bring the offering of the corn, of the new wine, and the oil, unto the chambers, where are the vessels of the sanctuary, and the priests that minister, and the porters, and the singers: and we will not forsake the house of our God.

< Nehemiya 10 >