< Nehemiya 10 >

1 Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
Te vaengah catui aka hnap rhoek tah Hakaliah capa tongmang boei Nehemiah neh Zedekiah.
2 Seraya, Azariya, Yeremiya
Seraiah, Azariah, Jeremiah.
3 Pasuri, Amariya, Malikiya,
Pashur, Amariah, Malkhiah.
4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Hattush, Shebaniah, Mallukh.
5 Harimu, Meremoti, Obadiya,
Harim, Meremoth, Obadiah.
6 Danieli, Ginetoni, Baruki,
Daniel, Ginnethon, Barukh.
7 Mesulamu, Abiya, Miyamini
Meshullam, Abijah, Mijamin.
8 Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
Maaziah, Bilgai, Shemaiah khosoih rhoek.
9 Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
Levi rhoek neh Azaniah capa Jeshua, Henadad koca kah Binnui neh Kadmiel.
10 ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
Amih boeinaphung te Shebaniah, Hodiah, Kelita, Pelaiah, Hanan.
11 Mika, Rehobu, Hasabiya,
Mikha, Rehob, Hashabiah.
12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
Zakkuur, Sherebiah, Shebaniah.
13 Hodiya, Bani ndi Beninu.
Hodiah, Bani, Beninu.
14 Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
Pilnam kah a lu rhoek tah, Parosh, Pahathmoab, Elam, Zattu, Bani.
15 Buni, Azigadi, Bebai,
Buni, Azgad, Bebai.
16 Adoniya, Bigivai, Adini,
Adonijah, Bigvai, Adin,
17 Ateri, Hezekiya, Azuri,
Ater, Hezekiah, Azzur.
18 Hodiya, Hasumu, Bezayi
Hodiah, Hashum, Bezai.
19 Harifu, Anatoti, Nebayi,
Hariph, Anathoth, Nebai.
20 Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
Magpiash, Meshullam, Hezir.
21 Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Mezhezabel, Zadok, Jaddua.
22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Pelatiah, Hanan, Anaiah.
23 Hoseya, Hananiya, Hasubu
Hosea, Hananiah, Hasshub.
24 Halohesi, Piliha, Sobeki,
Hallohesh, Pilha, Shobek.
25 Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Rehum, Hashabnah, Maaseiah.
26 Ahiya, Hanani, Anani,
Ahijah, Hanan, Anan.
27 Maluki, Harimu ndi Baana.
Mallukh, Harim, Baanah.
28 Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
Pilnam kah a coih rhoek, khosoih rhoek, Levi rhoek, thoh tawt rhoek, laa sa rhoek, tamtaeng rhoek, khohmuen pilnam lamloh aka hoep boeih, a yuu rhoek, a capa rhoek, a canu rhoek long khaw aka yakming boeih long tah Pathen olkhueng te a ming uh.
29 tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
Amih a khuet rhoek te a boeinaphung ah moem uh thae tih, Pathen kah sal Moses kut ah a paek Pathen kah olkhueng dongah pongpa ham khaw, ka Boeipa Yahweh kah olpaek boeih, a laitloeknah neh a oltlueh te ngaithuen ham neh vai ham khaw, olcaeng neh, olhlo neh pawk uh.
30 “Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
Kaimih nu rhoek te khohmuen pilnam taengah ka paek pawt ham khaw. Amih nu te khaw kaimih ca rhoek ham loh pah pawt ham khaw.
31 “Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
Khohmuen pilnam kah hnoyoih hang khuen khaw, Sabbath hnin kah a yoih ham cangtham boeih khaw, Sabbath neh a cim khohnin ah tah amih taengkah te lo uh pawt ham. Kum rhih nen tah kut tom kah a casai te yoe sak uh eh.
32 “Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
Kaimih Pathen im kah thothuengnah ham kaimih kah te kum khat ah shekel hlop thum paek ham olpaek te,
33 Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
Rhungkung buh neh sainoek khocang ham khaw, hlasae Sabbath kah sainoek hmueihhlutnah ham khaw, khoning ham neh hmuencim ham khaw, Israel ham tholh aka dawth boirhaem ham khaw, kaimih Pathen im kah bitat cungkuem ham khaw kaimih soah ka pai puei eh.
34 “Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
Olkhueng dongkah a daek bangla kaimih kah Pathen BOEIPA hmueihtuk dongah a toih ham te, a kum, kum kah a tue a hol vaengah, a pa imkhui loh kaimih Pathen im la, Levi khosoih neh pilnam kah nawnnah thing thak ham khaw,
35 “Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
Maimih kah khohmuen thaihcuek, thaih boeih khuikah thaihcuek, thing boeih te a kum, kum ah BOEIPA im la khuen ham khaw,
36 “Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
Olkhueng dongkah a daek bangla kaimih kah capa neh rhamsa caming, ka saelhung neh ka boiva cacuek khaw kaimih kah Pathen im ah kaimih Pathen im kah aka thotat khosoih rhoek taengla khuen ham,
37 “Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
kaimih kah buhhuem neh ka khosaa tanglue khaw, thing cungkuem kah a thaih khaw, misur thai neh situi khaw, Pathen im kah imkhan ah khosoih taengla, amih Levi rhoek tah kho takuem ah kaimih kah thohtatnah lamloh a duen dongah kaimih khohmuen kah parha pakhat te Levi taengla thak ham hmulung ka naan uh.
38 Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
Levi rhoek loh a duen vaegah Aaron koca khosoih rhoek te Levi taengah om kuekluek saeh. Parha pakhat dongkah parha pakhat te Levi rhoek loh kaimih Pathen im ah thakvoh im kah imkhan khuila thak uh saeh.
39 Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”
Israel ca rhoek neh Levi ca rhoek loh cangpai khocang khaw, misur thai neh situi khaw imkhan khuila thak uh saeh. Teah te rhokso kah hnopai neh aka thotat khosoih rhoek khaw, thoh tawt rhoek khaw, laa sa rhoek khaw a om dongah kaimih kah Pathen im te ka hnoo uh mahpawh.

< Nehemiya 10 >