< Nahumu 1 >
1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
The birthun of Nynyue; the book of visioun of Naum Helcesei.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
The Lord is a punyschere, and the Lord is vengynge; the Lord is venginge, and hauynge strong veniaunce; the Lord is vengynge ayens hise aduersaries, and he is wraththing to hise enemyes.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
The Lord is pacient, and greet in strengthe, and he clensynge schal not make innocent. The Lord cometh in tempest, and the weies of hym ben in whirlwynd, and cloudis ben the dust of hise feet;
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
he blameth the see, and drieth it, and bryngith alle flodis to desert. Basan is maad sijk, and Carmel, and the flour of Liban langwischide.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Mounteyns ben mouyd togidere of hym, and litil hillis ben desolat. And erthe tremblide togidere fro the face of him, and the roundenesse of erthe, and alle dwellynge ther ynne.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Who schal stonde bifore the face of his indignacioun? and who schal ayenstonde in the wraththe of his stronge veniaunce? His indignacioun is sched out as fier, and stoonys ben brokun of hym.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
The Lord is good, and coumfortynge in the dai of tribulacioun, and knowynge hem that hopen in hym.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
And in greet flood passynge forth, he schal make ende of his place; and derknessis schulen pursue hise enemyes.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
What thenken ye ayens the Lord? He schal make ende; double tribulacioun schal not rise togidere.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
For as thornes byclippen hem togidere, so the feeste of hem drynkynge togidere schal be wastyd, as stobul ful of drienesse.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
Of thee schal go out a man thenkynge malice ayens the Lord, and trete trespassyng in soule.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
The Lord seith these thingis, If thei schulen be parfit, and so manye, and thus thei shulen be clippid, and it schal passe bi. I turmentide thee, and Y schal no more turmente thee.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
And now Y schal al to-breke the yerde of hym fro thi bak, and Y schal breke thi bondis.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
And the Lord schal comaunde on thee, it schal no more be sowun of thi name. Of the hous of thi god Y schal sle; Y schal putte thi sepulcre a `grauun ymage, and wellid togidere, for thou art vnworschipid.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Lo! on hillis the feet of the euangelisynge and tellynge pees. Juda, halewe thou thi feeste daies, and yelde thi vowis, for whi Belial schal no more put to, that he passe forth in thee; al Belial perischide.