< Nahumu 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Ô ville de sang, toute pleine de mensonges et d'iniquités, tes rapines ne s'amoncelleront plus.
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
Voilà le bruit des fouets, le bruit des roues ébranlées, des chevaux lancés, des chars frémissants et des cavaliers en marche;
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
voilà le glaive étincelant, l'armure brillante de la multitude des blessés, et une ruine profonde. Et ses peuples étaient sans nombre, mais ils ont énervé leurs corps dans la multitude de leurs prostitutions.
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
Courtisane belle et gracieuse, reine des enchantements, tu vendais les peuples par tes débauches, et les nations par tes sortilèges.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Et voilà que Je M'attaque à toi, dit le Seigneur Dieu tout-puissant; Je dévoilerai tes nudités à tous les yeux, Je montrerai aux nations ta honte, et aux royaumes ton opprobre.
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
Et Je ferai retomber sur toi l'abomination que méritent tes impuretés, et Je ferai de toi un exemple.
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
Et il arrivera que tout homme, en te voyant, s'éloignera de toi, disant: Malheureuse Ninive, qui se lamentera sur elle? Où chercher pour elle une consolation?
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Prépare ta partie, ajuste tes cordes, prépare ta partie pour Ammon, qui demeure au milieu des fleuves; les flots l'entourent; la mer est son empire, et l'eau lui sert de remparts,
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
et l'Éthiopie est sa force, et aussi l'Égypte; et pourtant il n'y aura pas de terme à sa fuite. En vain les Libyens sont ses auxiliaires.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Elle-même sera transportée captive, et ses enfants seront écrasés à terre, à l'entrée de toutes les rues, et l'on se partagera au sort toutes les richesses qui faisaient sa gloire; et tous ses grands auront les mains chargées de chaînes.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
Et toi, tu seras enivrée, et tu seras méprisée, et tu solliciteras l'appui de tes propres ennemis.
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
Toutes tes forteresses seront comme des figuiers gardés; si on les secoue, les figues tombent dans la bouche et sont mangées.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Voilà que ton peuple sera comme un peuple de femmes; les portes de ton pays seront ouvertes à tes ennemis; le feu consumera tes barrières.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Tire de l'eau pour soutenir un siège; fortifie tes remparts; entre dans l'argile; foule-la aux pieds; mêle-la de lits de paille; sois toi-même plus ferme que la brique.
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
C'est là que la flamme te dévorera, que le glaive te détruira; comme une nuée de sauterelles tu seras engloutie; tu seras appesantie comme de grandes sauterelles.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
Tu as multiplié tes marchandises plus que les étoiles du ciel; la nuée de sauterelles les a attaquées et s'est envolée.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
La multitude étrangère mêlée à toi s'est enfuie comme l'escarbot, ou comme la sauterelle perchée sur la haie un jour de gelée; le soleil s'élève, elle saute dehors, et nul ne sait où elle s'était posée. Malheur à eux!
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
Tes pasteurs se sont assoupis; ton roi assyrien s'est endormi avec tes hommes de guerre; ton peuple s'est enfui sur les montagnes, et nul n'était là pour lui donner asile.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
Il n'est point de guérison pour tes blessures, ta plaie s'est enflammée; tous ceux qui entendent parler de tes malheurs battent des mains; car contre qui n'as-tu pas constamment tourné ta scélératesse?

< Nahumu 3 >