< Nahumu 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Woe to the city of blood! She is all full of deceit and robbery; She ceaseth not from plunder.
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
[[Hark!]] The noise of the whip! The noise of the rattling of the wheels, And of the prancing horses, And of the bounding chariots!
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
The horseman lifteth up the flame of the sword, And the lightning of the spear; There is a multitude of the slain; heaps of dead bodies; There is no end to the carcasses; they stumble over the carcasses.
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
It is because of the many whoredoms of the harlot, The graceful beauty, the mistress of enchantments, That sold nations by her whoredoms, And kingdoms by her enchantments.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Behold, I am against thee, saith Jehovah of host, And I will lift up thy trail over thy face, And I will show the nations thy nakedness, And the kingdoms thy shame.
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
And I will cast abominable filth upon thee, And I will dishonor thee, and make thee a gazing-stock,
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
And all that see thee shall flee from thee, And shall say, “Nineveh is laid waste; Who will bemoan her? Whence shall I seek comforters for thee?”
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Art thou better than No-Ammon, That dwelt by the rivers, That had the waters round about her, Whose fortress was the sea, And whose wall was from the waters?
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
Ethiopia and Egypt were her strength, a countless multitude; Phut and Lybia were thy helpers!
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Yet was she carried away; she went into captivity; Her children were dashed in pieces at the head of all the streets; For her honorable men they cast lots, And all her great men were bound in chains.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
Thou also shalt drink to the full; Thou, too, shalt be hidden; Thou shalt seek a refuge from the enemy!
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
All thy strong-holds shall be like fig-trees with the first ripe figs; If they be shaken, they fall into the mouth of the eater.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Behold, thy people shall be women in the midst of thee; The gates of thy land shall be set wide open to thine enemies; The fire shall devour thy bars.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Draw thee water for the siege, Fortify thy strongholds. Go into the clay, and tread the mortar; Repair the brick-kiln!
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
Then shall the fire devour thee; The sword shall cut thee off, It shall devour thee like the locust; Though thou art increased like the locusts, Though thou art increased like the thick locusts.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
Thy merchants have been more numerous than the stars of heaven; The locusts spread themselves and fly away.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
Thy princes are like locusts, And thy captains like swarms of locusts, Which encamp in the hedges in the time of cold; But when the sun ariseth, they flee away, And the place is not known where they are.
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
Thy shepherds slumber, O king of Assyria! Thy nobles take their rest, Thy people are scattered on the mountains, and none gathereth them.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
Thy bruise is incurable; Thy wound is mortal. All that hear of thee shall clap their hands over thee; For upon whom hath not thy wickedness passed continually?

< Nahumu 3 >