< Nahumu 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Woe [to] the city of blood, She is all full with lies [and] burglary, Prey does not depart.
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
The sound of a whip, And the sound of the rattling of a wheel, And of a prancing horse, and of a bounding chariot, Of a horseman mounting.
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
And the flame of a sword, and the lightning of a spear, And the abundance of the wounded, And the weight of carcasses, Indeed, there is no end to the bodies, They stumble over their bodies.
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
Because of the abundance of the fornications of a harlot, The goodness of the grace of the lady of witchcrafts, Who is selling nations by her fornications, And families by her witchcrafts.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
“Behold, I [am] against you,” A declaration of YHWH of Hosts, “And have removed your skirts before your face, And have showed nations your nakedness, And kingdoms your shame,
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
And I have cast on you abominations, And dishonored you, and made you as a sight.
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
And it has come to pass, Each of your beholders flees from you, And has said: Nineveh is spoiled, Who bemoans for her? From where do I seek comforters for you?”
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Are you better than No-Ammon, That is dwelling among brooks? Waters she has around her, Whose bulwark [is] the sea, waters her wall.
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
Cush her might, and Egypt, and there is no end. Put and Lubim have been for your help.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Even she becomes an exile, She has gone into captivity, Even her sucklings are dashed to pieces At the top of all out-places, And for her honored ones they cast a lot, And all her great ones have been bound in chains.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
Even you are drunken, you are hidden, Even you seek a strong place, because of an enemy.
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
All your fortresses [are] fig trees with first-fruits, If they are shaken, They have fallen into the mouth of the eater.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Behold, your people [are] women in your midst, To your enemies thoroughly opened Have been the gates of your land, Fire has consumed your bars.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Waters of a siege draw for yourself, Strengthen your fortresses, Enter into mire, and tread on clay, Make strong a brick-kiln.
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
There a fire consumes you, A sword cuts you off, It consumes you as a cankerworm! Make yourself heavy as the cankerworm, Make yourself heavy as the locust.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
Multiply your merchants above the stars of the heavens, The cankerworm has stripped off, and flees away.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
Your crowned ones [are] as a locust, And your princes as great grasshoppers, That encamp in hedges in a day of cold, The sun has risen, and it flees away, And its place where they are is not known.
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
Your friends have slumbered, king of Asshur, Your majestic ones rest, Your people have been scattered on the mountains, And there is none gathering.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
There is no weakening of your destruction, Your striking [is] grievous, All hearing your fame have clapped the hand at you, For over whom did your wickedness not pass continually?

< Nahumu 3 >