< Nahumu 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Woe to the city of blood! it is all full of lies and robbery; never ceaseth the preying;
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
The noise of a whip, and the noise of the rattling of wheels, and of prancing horses, and of the skipping chariots.
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
Horsemen mount, and there are the flaming sword and the glittering spear: and there is a multitude of slain, and heaps of carcasses; and without end are the corpses; they stumble on their corpses;
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
Because of the multitude of the lewd deeds of the harlot, that is rich in gracefulness, the mistress of witchcrafts, that selleth nations through her lewd deeds, and families through her witchcrafts.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Behold, I will be against thee, saith the Lord of hosts; and I will lay thy skirts open over thy face, and I will let nations see thy nakedness, and kingdoms thy shame.
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
And I will cast abominable filth upon thee, and defile thee, and will render thee a dirt-heap.
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
And it shall come to pass, that all they that see thee shall flee from thee, and say, Laid waste is Nineveh: who will condole with her? whence shall I seek comforters for thee?
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Art thou better than No-amon, that was situated on the rivers, that had water round about her, the rampart of which was the sea, and the walls of which rose out of the sea?
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
Ethiopia the numerous, and Egypt that was without end, Put and Lubim were thy helpers.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Yet also she was exiled, was carried away into captivity; also her young children were dashed in pieces at the corners of all streets: and for her honorable men they cast lots, and all her great ones were bound with chains.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
Thou also shalt be made drunken, thou shalt be hidden from view: thou also shalt seek refuge because of the enemy.
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
All thy strong-holds shall be like fig-trees with the first ripe figs, which, if they be shaken, will fall into the mouth of the eater.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Behold, thy people are become women in the midst of thee: unto thy enemies are the gates of thy land set wide open; the fire hath devoured thy bars.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Water for the siege draw for thyself, fortify thy strongholds: go into the clay, and tread the mortar, make strong the brick-kiln.
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
There shall the fire devour thee; the sword shall cut thee off, it shall devour thee up like the cankerworm: [though] thou make thyself many as the cankerworm; make thyself many as the locusts.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
[Though] thou hadst multiplied thy merchants more than the stars of heaven: the cankerworm spreadeth itself out, and flieth away.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
Thy crowned ones are like the locusts, and thy leaders like the swarms of locusts, which camp in the hedges on a cold day, but when the sun ariseth they flee away, and their place is not known where they are.
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
Thy shepherds slumber, O king of Assyria; thy valiant men are at rest: scattered are thy people upon the mountains, and there is none that gathereth them.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
There is no healing for thy breach; fatal is thy wound: all that hear the report of thee will clap their hands over thee; for over whom did not thy wickedness pass continually?

< Nahumu 3 >