< Nahumu 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
What a disaster is coming upon this murderous city with all its treachery! It is full of wealth it has robbed, and always has plenty of victims.
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
Listen to the noise: whips crack, wheels clatter, horses gallop, chariots rattle!
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
Horsemen charge, swords flash, spears glitter! Many dead, piles of corpses, countless bodies—so many that people stumble over them.
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
All this happens because the repeated prostitution of Nineveh the prostitute, the beautiful mistress with her deadly charms who seduces nations into slavery by her prostitution and her witchcraft.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Watch out! For I am against you, declares the Lord Almighty. I will lift your skirts over your face and let the nations see your nakedness, and kingdoms see your shame.
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
I will throw filth at you. I will treat you with contempt, and make a spectacle of you.
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
Then everyone who sees you will shun you saying, “Nineveh is ruined! But who is going to mourn your loss?” Where should I look to find anyone to comfort you?
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Are you any better than the city of Thebes on the River Nile, surrounded by water? Water was its defense, water was its wall.
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
The city ruled Egypt and Ethiopia. Put and Libya were its allies.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Yet its people were also taken away into exile, into captivity. Their babies were dashed to pieces in every street. Their nobles were bound in chains and taken away as servants, chosen by lot.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
You too will behave like a drunk. You will hide in fear, trying to find a place safe from the enemy.
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
All your fortresses are like fig trees ripe with fruit—they fall when they are shaken into the mouth of the one eating.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Look! Your soldiers are women among you. The gates of your land are wide open to your enemies; the bars of the gates will be set on fire.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Store water to prepare for a siege! Strengthen your fortresses! Go to the clay pits to tread it well, mix the cement, get your brick molds ready!
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
But even so, there the fire will consume you, you will be cut down by the sword. You will be destroyed as if you were devoured by a swarm of locusts. So multiply yourselves like locusts, like a swarm of locusts.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
You increased your merchants so that there are more of them than the stars of heaven. But like locusts they strip everything and then fly away.
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
Your leaders are like locusts, your officials like a swarm of locusts. They rest on walls on a cold day, but when the sun rises they fly away, and no one knows where they've gone.
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
King of Assyria, your shepherds are asleep, your princes are slumbering. Your people are scattered across the mountains and no one can gather them.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
There is no way to heal your injuries, you are too badly wounded. Everyone who hears this news will applaud what has happened to you, for was there anyone who escaped your continuous cruelty?

< Nahumu 3 >