< Nahumu 3 >
1 Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
Горко на кръвнишкия град; Цял е пълен с лъжа и грабеж; Плячката не липсва.
2 Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
Пукот на бичове се чува, и шум от тропот на колела, На тичащи коне, и на подскачащи колесници.
3 Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
Конникът се качва с лъскав меч и бляскаво копие; Има и много ранени и голямо число убити, и труповете са безчислени; Спъват се в труповете им.
4 Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
Това е поради многото блудства на привлекателната блудница, Изкусна в баяния, Която продава народи чрез блудствата си, И племена чрез баянията си.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
Ето, Аз съм против тебе, казва Господ на Силите; Ще издигна полите ти върху лицето ти, И ще покажа на народите голотата ти, И на царствата срама ти.
6 Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
Ще хвърля върху тебе гнусна нечистота и ще те омърся, И ще те поставя като позорище.
7 Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
Всички, които те гледат, ще бягат от тебе, И ще рекат: Ниневия запустя! Кой ще я оплаче? От где да потърся утешители за тебе?
8 Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
Ти по-добра ли си от Но Амон, Който лежеше между реките, Окръжен от води, Чието предстение бе Нил, И стената му Нилови води?
9 Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
Етиопия, и Египет бяха негова сила и тя беше безгранична; Фут и ливийците бяха твои помощници.
10 Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
Но и той беше откаран, отиде в плен; Младенците му тоже бяха смазани По кръстопътищата на всичките улици; Хвърлиха жребие за почтените му мъже, И всичките му големци бидоха вързани с вериги.
11 Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
Също и ти ще се опиеш, Ще се скриеш, Ще потърсиш и ти защита против неприятеля.
12 Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
Всичките ти крепости ще бъдат Като смоковници с първозрелите си смокини; Ако се затресат; Ще паднат в устата на ядящия.
13 Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
Ето, людете ти всред тебе са жени; Портите на земята ти се отвориха широко на неприятелите ти; Огънят изпояде лостовете ти.
14 Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
Извади си вода за обсадата, Уякчи крепостите си, Влез в калта и стъпчи глината, Поправи тухлената пещ.
15 Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
Там ще те изяде огън; Меч ще те отсече, Ще те изяде като изедника, Па и да се размножиш като изедника, Па и да се размножиш като скакалеца.
16 Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
(Умножила си търговците си Повече от небесните звезди; ) Както изедникът опустоши и отлетя,
17 Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
Така и коронясаните ти са като скакалци, Които се настаняват на плетищата в студен ден, Но които, като изгрее слънцето, бягат, И не се познава мястото гдето бяха.
18 Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
Пастирите ти задрямват царю асирийски, Благородните ти лежат бездейни; Людете ти се разпръснаха по планините, И няма кой да ги събира.
19 Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?
Няма лек за язвата ти; Раната ти е люта; Всички, които чуят вестта за тебе, Изпляскват с ръце поради тебе; Защото върху кого не е падало всякога нечестието ти?