< Nahumu 2 >
1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
Saldırı altındasın, ey Ninova, surlarını koru, Yolu gözle, belini doğrult, topla bütün gücünü.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
Çünkü RAB Yakup'un soyunu İsrail'in eski görkemine kavuşturacak; Düşmanları onları perişan edip asmalarını harap etmiş olsa bile.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
Askerlerinin kalkanları kıpkızıl, Yiğitler allar kuşanmış. Savaş arabalarının demirleri hazırlık günü nasıl da parıldıyor! Çam mızraklar sallanıyor havada.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
Sokaklardan fırtına gibi geçiyor savaş arabaları, Meydanlardan koşuşuyorlar her yöne, Şimşek gibi seğirtiyorlar. Görünüşleri meşalelerden farksız.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
Ninova Kralı topluyor seçkin askerlerini, Ama sendeliyorlar yolda. Saldıranlar kent surlarına doğru seğirtiyor, Siperler kuruluyor.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Irmakların kapıları açıldı Ve yerle bir oldu saray.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
Tanrı'nın dediği oldu, soyup götürdüler kenti. Güvercinler gibi inliyor kadın köleler, Göğüslerini döverek.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
Kaçıp gidiyor Ninova halkı, Boşalan bir havuzun suyu gibi, “Durun, durun!” diye bağırıyorlar, Ama geri dönüp bakan yok.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Yağmalayın altınını, gümüşünü, Yok servetinin sonu. Her tür değerli eşyayla dolup taşıyor.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
Yıkıldı, yerle bir oldu, viraneye döndü Ninova. Eriyor yürekler, Bükülüyor dizler, titriyor bedenler, Herkesin beti benzi soluyor.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Aslanların inine, Yavru aslanların beslendiği yere ne oldu? Aslanla dişisinin ve yavrularının korkusuzca gezindiği yere ne oldu?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
Aslan, yavrularına yetecek kadarını avladı, Dişileri için avını boğazladı. Mağarasını avladıklarıyla, İnini kurbanlarıyla doldurdu.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Her Şeye Egemen RAB, “Sana karşıyım” diyor, “Yakacağım savaş arabalarını, Dumanları tütecek. Genç aslanlarını kılıç yiyip tüketecek. Yeryüzünde av bırakmayacağım sana Ulaklarının sesi işitilmeyecek artık.”