< Nahumu 2 >
1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
Kdor razbija na koščke je prišel gor, pred tvoj obraz. Varuj oporišče, pazi na pot, naredi svoja ledja močna, mogočno utrdi svojo moč.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
Kajti Gospod je odvrnil Jakobovo odličnost kakor odličnost Izraela, kajti izpraznjevalci so jih izpraznili in skazili njihove trtne mladike.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
Ščit njegovih mogočnih mož je pordečel, hrabri možje so v škrlatu. Bojni vozovi bodo s plamenečimi baklami na dan njegove priprave in ciprese bodo strašno stresene.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
Bojni vozovi bodo besneli po ulicah, zadevali se bodo drug ob drugega na širokih poteh, zdeli se bodo kakor bakle, tekli bodo kakor bliski.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
Spomnil se bo svojih vrlih. Spotaknili se bodo v svoji hoji, podvizali se bodo k njegovemu obzidju in obramba bo pripravljena.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Velika vrata rek bodo odprta in palača se bo raztopila.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
Huzzab bo odvedena v ujetništvo, privedena bo gor in njene služabnice jo bodo vodile kakor z glasom golobic, ki se bijejo po svojih prsih.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
Toda Ninive so od davnine podobne vodnemu zbiralniku, vendar bodo pobegnile. »Stojte, stojte; « bodo kričali toda, nihče ne bo pogledal nazaj.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Vzemite plen srebra, vzemite plen zlata, kajti ni konca zaloge in slave vseh dragocenih stvari.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
Prazna je, izpraznjena in opustošena. Srce se topi in kolena udarjajo skupaj in precej bolečine je v vseh ledjih in vsi njihovi obrazi zbirajo črnino.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Kje je prebivališče levov in kraj za hranjenje mladih levov, kjer je hodil lev, celó star lev in levji mladič in nihče ju ni prestrašil?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
Lev je raztrgal na koščke dovolj za svoje mladiče in zadavil za svoje levinje in svoje jame napolnil s plenom in svoje brloge z ropom.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
»Glej, jaz sem zoper tebe, « govori Gospod nad bojevniki, »in jaz bom sežgal njene bojne vozove v dimu in meč bo použil tvoje mlade leve in iztrebil bom tvoj plen z zemlje in glasu tvojih poslancev ne bo več slišati.«