< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
Umhlakazi ukhuphukile phambi kobuso bakho; gcina inqaba, linda indlela, qinisa ukhalo, yenza amandla akho aqine kakhulu.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
Ngoba iNkosi ibuyisile ubukhosi bukaJakobe, njengobukhosi bukaIsrayeli. Ngoba abathululayo babathululile, bona izingatsha zevini zabo.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
Isihlangu samaqhawe akhe senziwe saba bomvu, amadoda alesibindi agqoke okubomvu; izinqola ziphakathi lomlilo wensimbi ngosuku lokuzilungiselela kwakhe; lezihlahla zamafiri zizazanyazanyiswa.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
Izinqola ziyahlanya ezitaladeni, zihaluzela ziye le lale emidangeni; ukubonakala kwazo kunjengezibane, zigijime njengemibane.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
Uzakhumbula izikhulu zakhe; zizakhubeka ekuhambeni kwazo; ziphangise emthangaleni wakhe, sesimisiwe isivikelo.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Amasango emifula azavulwa, lesigodlo sincibilike.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
Njalo uHuzabhi uzakhokhelwa engothunjiweyo, uzakhutshulwa, lezincekukazi zakhe zimkhokhele kwangathi ngelizwi lamajuba, zitshaya ezifubeni zazo.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
Loba iNineve injengechibi lamanzi kusukela kwasendulo, kanti bazabaleka. Bathi: Manini! manini! kodwa kakho ozaphenduka.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Phangani isiliva, phangani igolide; ngoba kakulakuphela kokubuthelelweyo, lenkanzimulo kuzo zonke izitsha eziloyisekayo.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
Iyize, kayiselalutho, ichithekile; inhliziyo iyancibilika, lamadolo ayatshayana, lobuhlungu obukhulu busezinkalweni zonke, lobuso babo bonke bunyukumele.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Ingaphi indawo yokuhlala yezilwane, lendawo yokudlela yamabhongo esilwane, lapho esasihamba khona isilwane, isilwane esidala, lomdlwane wesilwane, njalo kungekho okuzethusayo?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
Isilwane sadabudabula okwenele imidlwane yaso, sakhamela izilwanekazi zaso, sagcwalisa imilindi yaso ngempango, lezindawo zaso zokuhlala ngokudatshuliweyo.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Khangela, ngimelene lawe, itsho iNkosi yamabandla, ngizazitshisa inqola zakhe entuthwini, lenkemba izaqeda amabhongo ezilwane akho; njalo ngizaquma impango yakho kusuke emhlabeni, lelizwi lezithunywa zakho kalisayikuzwakala.

< Nahumu 2 >