< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
The one who will dash you to pieces is coming up against you. Man the city walls, guard the roads, make yourselves strong, assemble your armies.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
For Yahweh is restoring the majesty of Jacob, like the majesty of Israel, although the plunderers devastated them and destroyed their vine branches.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
The shields of his mighty men are red, and the soldiers are clothed in scarlet; the chariots flash with their metal on the day that they are made ready, and the cypress spears are waved in the air.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
The chariots speed through the streets; they rush back and forth in the wide streets. They look like torches, and they run like lightning.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
The one who will dash you to pieces calls his officers; they stumble over each other in their march; they hurry to attack the city wall. The large shield is made ready to protect these attackers.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
The gates at the rivers are forced open, and the palace falls to ruins.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
Huzzab is stripped of her clothes and is taken away; her female servants moan like doves, beating on their breasts.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
Nineveh is like a leaking pool of water, with its people fleeing away like rushing water. Others shout, “Stop, stop,” but no one looks back.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Take the silver plunder, take the gold plunder, for there is no end to it, to the splendor of all Nineveh's beautiful things.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
Nineveh is empty and ruined. Everyone's heart melts, everyone's knees strike together, and anguish is in everyone; their faces are all pale.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Where now is the lions' den, the place where the young lion cubs were fed, the place where the lion and lioness walked, with the cubs, where they were afraid of nothing?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
The lion tore his victims to pieces for his cubs; he strangled victims for his lionesses, and filled his cave with victims, his dens with torn carcasses.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
“See, I am against you—this is the declaration of Yahweh of hosts. I will burn your chariots in the smoke, and the sword will devour your young lions. I will cut off your prey from your land, and the voices of your messengers will be heard no more.”

< Nahumu 2 >