< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
He is come up that shall destroy before thy face, that shall keep the siege: watch the way, fortify thy loins, strengthen thy power exceedingly.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
For the Lord hath rendered the pride of Jacob, as the pride of Israel: because the spoilers have laid them waste, and have marred their vine branches.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
The shield of his mighty men is like fire, the men of the army are clad in scarlet, the reins of the chariot are flaming in the day of his preparation, and the drivers are stupefied.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
They are in confusion in the ways, the chariots jostle one against another in the streets: their looks are like torches, like lightning running to and fro.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
He will muster up his valiant men, they shall stumble in their march: they shall quickly get upon the walls thereof: and a covering shall be prepared.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
The gates of the rivers are opened, and the temple is thrown down to the ground.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
And the soldier is led away captive: and her bondwomen were led away mourning as doves, murmuring in their hearts.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
And as for Ninive, her waters are like a great pool, but the men flee away. They cry: Stand, stand, but there is none that will return back.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Take ye the spoil of the silver, take the spoil of the gold: for there is no end of the riches of all the precious furniture.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
She is destroyed, and rent, and torn: the heart melteth, and the knees fail, and all the loins lose their strength: and the faces of them all are as the blackness of a kettle.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Where is now the dwelling of the lions, and the feeding place of the young lions, to which the lion went, to enter in thither, the young lion, and there was none to make them afraid?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
The lion caught enough for his whelps, and killed for his lionesses: and he filled his holes with prey, and his den with rapine.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Behold I come against thee, saith the Lord of hosts, and I will burn thy chariots even to smoke, and the sword shall devour thy young lions: and I will cut off thy prey out of the land, and the voice of thy messengers shall be heard no more.

< Nahumu 2 >