< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
He ascends, who would scatter before your eyes, who would maintain the blockade. Contemplate the way, fortify your back, reinforce virtue greatly.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
For the Lord has repaid the arrogance of Jacob, just like the arrogance of Israel. For the despoilers have scattered them, and they have corrupted their procreation.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
The shield of his strong ones is fire, the men of war are in scarlet. The reins of the chariot are fiery in the day of his preparation, and the drivers have been drugged.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
They have become confused on their journey. The four-horse chariots have collided in the streets. Their appearance is like torches, like lightning dashing around.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
He will call to mind his strong ones; they will destroy along their journey. They will quickly ascend its walls, and a shelter will be prepared.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
The gates of the rivers have been opened, and the temple has been pulled down to the ground.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
And the foot soldier has been led away captive, and her handmaids were driven away, mourning like doves, murmuring in their hearts.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
And Nineveh, her waters are like a fish pond. Yet truly, they have fled away: “Stand, stand!” But there is no one who will turn back.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Despoil the silver, despoil the gold. And there is no end to all the riches of desirable equipment.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
She has been scattered, and cut, and torn apart. And the heart melts, and the knees buckle, and weakness is in every temperament. And the faces of them all are like a black kettle.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Where is the dwelling place of the lions, and the feeding ground of the young lions, to which the lion went, so as to open a way for the young lion, and so that there would be none to make them afraid?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
The lion seized enough for his young, and killed enough for his lionesses, and he filled his caves with prey, and his den with spoils.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Behold, I will come to you, says the Lord of hosts, and I will burn your chariots even to smoke, and the sword will devour your young lions. And I will exterminate your prey from the land, and the voice of your messengers shall no longer be heard.

< Nahumu 2 >