< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
因為上主要恢復雅各伯的葡萄園,因為劫掠者搶掠了他們,且破壞了他們的葡萄蔓。
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
尼尼微,有個破壞者上來攻擊你,你應把守堡壘,防守要道,朿緊你的腰,集中你的全力!
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
他勇士的盾牌是赤色的,戰士穿的衣服是深紅的;在他整裝待發之日,戰車閃爍如火,騎士疾馳如飛。
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
戰車在大路上奔馳,在廣場上疾駛,形狀有如火炬,疾行有如閃電。
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
亞述王召集了他的精銳,而他們卻在行軍時顛仆;急忙跑近城堡,但高楯已舉起。
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
河閘打開了,皇宮大為震驚。
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
漆布裸體被擄去,她的使女們呻吟如鴿,各自搥胸。
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
尼尼微好似一個水池,池水洶湧流出,出有人喊:「止住! 止住! 」但無一人回顧。
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
「你們搶奪銀子,搶奪金子! 」有無盡的寶藏,有無數的珍器。
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
搶掠、洗劫。蹂躪! 人心沮喪,兩膝打顫,雙腰發抖,面無血色。
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
獅子穴,幼獅洞,今在何處﹖哪裏原是雄獅、母獅和幼獅出竹之所,無人敢驚它們!
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
雄獅曾為幼獅撕裂獵物,為母獅扼死野獸,將獵物簊滿牠的洞穴,將掠物充塞牠的窟穴。
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
看,我必攻擊你! ──上主的斷語──我要在濃煙中燒毀你的洞穴,使刀劍吞食你的幼獅,由地上掃除你的掠物,令人再也聽不到你使者的聲音。

< Nahumu 2 >