< Mika 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
Dette er Herrens ord som kom til Mika fra Moreset i de dager da Jotam, Akas og Esekias var konger i Juda, det som han skuet om Samaria og Jerusalem.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Hør, I folk, alle sammen! Gi akt, du jord med alt som på dig er! Og Herren, Israels Gud, være vidne mot eder, Herren fra sitt hellige tempel!
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
For se, Herren går ut fra sin bolig; han stiger ned og farer frem over jordens høider.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
Fjellene smelter under ham, og dalene revner - som voks for ilden, som vann når det øses ut over et stup.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
For Jakobs frafall skjer alt dette, for de synder Israels hus har gjort. Hvem er ophavet til Jakobs frafall? Mon ikke Samaria? Og hvem til Judas offerhauger? Mon ikke Jerusalem?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
Så vil jeg da gjøre Samaria til en grusdynge på marken, til et sted for vindyrkning, og jeg vil velte dets stener ned i dalen og avdekke dets grunnvoller.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
Og alle dets utskårne billeder skal sønderslås, og alle dets horegaver brennes op med ild, og alle dets avgudsbilleder vil jeg ødelegge; for av horelønn har det samlet dem, og til horelønn skal de atter bli.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
Over dette vil jeg klage og hyle, jeg vil gå barbent og naken; jeg vil opløfte klageskrik som sjakalene og jamre mig som strutsene.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
For dets sår er ulægelige; for ulykken er kommet like til Juda, den har nådd like til mitt folks port, til Jerusalem.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Forkynn det ikke i Gat, gråt ikke der! I Bet-Leafra velter jeg mig i støvet.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
Dra bort, I Sjafirs innbyggere, i nakenhet og vanære! Sa'anans innbyggere våger sig ikke ut. Bet-Haesels klageskrik gjør det umulig for eder å bli der.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
For Marots innbyggere vrir sig i smerte over sin tapte lykke; for ulykke er faret ned fra Herren, like til Jerusalems port.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
Spenn traveren for vognen, I innbyggere av Lakis! Syndens ophav var du for Sions datter, for hos dig blev Israels overtredelser funnet.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
Derfor skal du gi avkall på Moreset-Gat; husene i Aksib blir som en sviktende bekk for Israels konger.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Ennu en gang skal jeg la eder få en eiermann, I Maresas innbyggere! Til Adullam skal Israels stormenn komme.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Gjør dig skallet, klipp håret vekk for dine barns skyld, de som var din lyst! Gjør ditt hode så skallet som gribbens, for de er ført bort fra dig.

< Mika 1 >