< Mika 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
KA olelo a Iehova ka mea i hiki mai ia Mika no Moreseta, i na la o Iotama, Ahaza, a o Hezekia, na'lii o ka Iuda, ka mea ana i ike ai no Samaria, a no Ierusalema.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
E hoolohe, e na kanaka a pau; E haliu mai, e ka honua, a me kona mea i piha ai: A e lilo o Iehova ka Haku i mea hoike ku e ia oukou, O ka Haku mai kona luakini hoano mai.
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
No ka mea, aia hoi, e hele mai o Iehova mai kona wahi mai, A e iho ilalo a e hehi maluna o na wahi kiekie o ka honua.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
A hehee na mauna malalo iho ona, A e wahiia na awawa, E like me ke kepau imua o ke ahi, A me ka wai i nininiia ma kahi pali.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
No ka lawehala ana o ka Iakoba keia mea a pau, a no na hewa o ko ka hale o Iseraela. He aha ka hala o ka Iakoba? aole anei o Samaria? A owai na wahi kiekie o Iuda? aole anei o Ierusalema?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
A e hoohalike au ia Samaria me he puu la o ke kula, A me he wahi kanu la no ka pawaina; A e hoolei iho au i na pohaku ona ma ke awawa, A e hoike aku au i kona mau kahua.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
A e ulupaia kona mau kii kalai a pau, A o kona waiwai moe kolohe e puhiia i ke ahi, A e luku aku au i kona mau kii a pau: No ka mea, ua loaa ia ia ua mea la no ka uku o ka wahine moe kolohe, A e hoihoiia aku ia i ka uku o ka wahine moe kolohe.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
No keia mea, e auwe iho au, a e aoa, A e hele wale au, me ke kapa aahu ole; E hoohalike au i ka auwe ana me ko ka ilio hihiu, A i ka alala ana me ko ka iana wahine.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
No ka mea, o kona eha he eha make ia, a ua hiki mai ia i ka Iuda; Ua hiki mai i ka pukapa o kou poe kanaka, a i Ierusalema.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Mai hai aku oukou ia ma Gata, mai auwe oukou i ka auwe ana; Ma ka hale o Apera e kau i ka lepo maluna iho ou.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
E hele aku oe, e ka mea e noho ana ma Sapira, me kou hilahila uhi ole; Aole i hele mai iwaho ka mea o noho ana ma Zaanana, ma ka auwe ana o Betezela; E lawe no ia i kona noho ana mai o oukou aku.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
No ka mea, o ka mea e noho ana ma Marota, ua nawaliwali ia no ka iini i ka maikai; Aka, iho mai la ka ino mai Iehova mai ma ka pukapa o Ierusalema.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
E ka mea o noho la ma Lakisa, e hoopaa i ka halekaa i ka lio mama; Oia ke poo o ka hewa no ke kaikamahine o Ziona; No ka mea, ua loaa na lawehala o ka Iseraela iloko ou.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
No ia mea, e haawi aku oe i na makana no Moresetagata: E lilo na hale o Akeziba i mea hoopunipuni no na'lii o ka Iseraela.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Aka hoi, e lawe mai no au i hooilina nou, e ka mea e noho ana ma Maresa: A e hele mai ka nani o ka Iseraela i Adulama.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
E hooohule oe, a e ako i ke oho no na keiki o kou makemake; E hoomahuahua oe i kou ohule ana, e like me ka aeto; No ka mea, ua hele pio aku la lakou mai ou aku la.

< Mika 1 >